Deuteronomo 11 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 11:1-32

Kukonda ndi Kumvera Yehova

1Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake. 2Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka; 3zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse; 4zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero. 5Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu, 6ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo. 7Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.

8Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani, 9ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi. 10Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba. 11Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba. 12Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.

13Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, 14pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta. 15Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.

16Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira. 17Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani. 18Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu. 19Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka. 20Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu, 21kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.

22Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye 23Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu. 24Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo. 25Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.

26Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu, 27dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero. 28Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe. 29Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala. 30Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala. 31Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo, 32mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 11:1-32

要聽從耶和華

1「你們要愛你們的上帝耶和華,時刻遵守祂的吩咐、律例、典章和誡命。 2要記住,我現在是對你們,而不是對你們的孩子說話。他們沒有親身經歷、親眼見過你們上帝耶和華的管教、威嚴、大能的手和伸出的臂膀; 3祂怎樣在埃及行神蹟奇事對付法老及其國家; 4怎樣使紅海淹沒追趕你們的埃及軍隊和車馬,將他們永遠毀滅; 5怎樣在曠野一路看顧你們,一直來到這裡; 6怎樣對付呂便以利押的兒子大坍亞比蘭,使大地在以色列人當中裂開,吞沒了他們及其家人、帳篷和所有隨從。 7你們親眼目睹了耶和華的這些偉大作為。

8「因此,你們要遵守我今天吩咐你們的誡命,以便有力量過河攻取你們將要攻取的土地, 9長久居住在耶和華起誓賜給你們祖先及其後裔的奶蜜之鄉。 10那片土地不像你們離開的埃及。在埃及你們撒種後,要像澆菜園一樣辛勤灌溉11·10 辛勤灌溉」希伯來文是「用腳灌溉」。11而你們將要佔領的那片土地卻有山有谷,雨水充足, 12你們的上帝耶和華從歲首到年終時時看顧那裡。

13「如果你們謹遵我今天吩咐你們的誡命,全心全意地愛你們的上帝耶和華,事奉祂, 14祂就會按時降下秋雨和春雨,使你們收穫穀物、新酒和油, 15有草場飼養牲畜,豐衣足食。 16你們要謹慎,免得被迷惑,轉而祭拜、供奉其他神明。 17否則,耶和華必向你們發怒,使天不下雨、地無出產,以致你們在祂賜給你們的佳美之地上迅速滅亡。

18「所以,你們要把我的這些吩咐銘記在心,繫在手上,戴在額上作記號; 19要用這些話教導你們的兒女,無論在家在外、或起或臥,都要講論; 20也要寫在城門上和自家的門框上。 21這樣,你們及子孫就可以生活在耶和華起誓賜給你們祖先的土地上,與天地同長。 22如果你們謹遵我吩咐你們的這一切誡命——愛你們的上帝耶和華,遵行祂的旨意,依靠祂, 23耶和華就會為你們趕走那些比你們強大的民族,你們也必佔領他們的土地。 24你們腳掌踏過的地方都要歸你們。你們的疆界南到曠野,北到黎巴嫩,東到幼發拉底河,西到地中海。 25所到之處無人能抵擋你們,因為你們的上帝耶和華會使那些地方的人對你們充滿懼怕,正如祂對你們的應許。

26「看啊,我今天把祝福和咒詛擺在你們面前。 27你們若遵行我今天吩咐你們的誡命,就會得到祝福。 28你們若不遵行你們的上帝耶和華的誡命,偏離我今天吩咐你們當走的道路,隨從不認識的神明,必受咒詛。 29你們的上帝耶和華帶領你們進入並佔領那片土地時,你們要在基利心山上宣告祝福,在以巴路山上宣告咒詛。 30基利心山和以巴路山屬於住在亞拉巴迦南人,位於約旦河西岸的日落之處,在吉甲對面,靠近摩利橡樹。 31你們穿過約旦河,佔領耶和華賜給你們的土地,定居下來以後, 32要謹遵我今天頒佈給你們的一切律例和典章。