Danieli 8 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 8:1-27

Masomphenya a Danieli a Nkhosa Yayimuna ndi Mbuzi Yayimuna

1Chaka chachitatu cha ulamuliro wa mfumu Belisazara, Ine Danieli, ndinaonanso masomphenya, ena atatha amene anandionekera poyamba. 2Ndinaona mʼmasomphenya kuti ndinali mu mzinda wotetezedwa wa Susa mʼchigawo cha Elamu. Mʼmasomphenyawo ndinaona nditayima pafupi ndi mtsinje wa Ulai. 3Nditakweza maso ndinaona nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri, itayima pafupi ndi mtsinje. Nyanga zakezo zinali zazitali. Nyanga imodzi inali yotalika kuposa inzake, ndipo iyi inaphuka inzakeyo itamera kale. 4Ndinaona nkhosa yayimunayo ikuthamanga mwaukali kupita kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. Palibe chirombo chimene chikanatha kulimbana nayo, ndipo palibe akanatha kulanditsa kanthu kwa iyo. Iyo inachita monga inafunira ndipo inali ndi mphamvu zambiri.

5Pamene ndinali kulingalira za zinthu zimenezi, mwadzidzidzi mbuzi yayimuna inatulukira cha kumadzulo, kudutsa dziko lonse lapansi mwaliwiro ikuyenda mʼmalele mokhamokha. Mbuzi yayimunayo inali ndi nyanga yayikulu pakati pa maso ake. 6Inabwera molunjika nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri ija imene ndinaona itayima pafupi ndi mtsinje. Ndipo inayithamangira mwaukali. 7Inafika pafupi ndipo inalimbana nayo mwaukali nkhosa yayimuna ija nʼkuthyola nyanga zake ziwiri. Nkhosa yayimunayo inalibenso mphamvu zogonjetsera mbuziyo; choncho mbuzi ija inagwetsa nkhosayo pansi nʼkuyipondaponda, ndipo palibe akanatha kulanditsa nkhosayo kwa mbuziyo. 8Mbuziyo inayamba kudzikuza kwambiri chifukwa cha mphamvu zake koma pamene mphamvuzo zinakula kwambiri nyanga yake yayikulu inathyoka, ndipo mʼmalo mwake panamera nyanga zinayi moloza mbali zonse zinayi.

9Pa imodzi mwa nyangazo panatuluka nyanga imene inali yocheperapo koma inakula kwambiri kuloza kummwera ndi kummawa ndi kuloza dziko lokongola. 10Inakula mpaka inafikira gulu lankhondo la kumwamba, ndipo inagwetsera ena a gulu lankhondolo ndi ena a gulu la nyenyezi ku dziko lapansi ndi kuwapondaponda. 11Inadzikuza yokha mpaka kufikira kwa mfumu ya gululo: inathetsa nsembe zimene zinkaperekedwa tsiku ndi tsiku, ndipo inagwetsa nyumba yake yopatulika. 12Gulu lake la nkhondo linathetsa nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku; chipembedzo choonadi chinaponderezedwa pansi. Nyangayi inapambana mu zonse zimene inachita.

13Kenaka ndinamva wina akuyankhula; ndipo woyera winanso anamufunsa kuti, “Kodi zimene ndikuziona mʼmasomphenyazi zidzatha liti? Nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku zidzakhala zoletsedwa mpaka liti? Nanga chonyansa chosokoneza chidzakhalapo mpaka liti? Kodi gulu la ankhondo lidzapondereza malo opatulika mpaka liti?”

14Iye anandiyankha kuti, “Zidzachitika patapita masiku 2,300; pambuyo pake malo opatulika adzabwezeretsedwa monga kale.”

Kumasulira kwa Masomphenya

15Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga. 16Ndipo ndinamva mawu a munthu kuchokera mʼmbali mwa mtsinje wa Ulai akuyitana kuti, “Gabrieli, muwuze munthuyu tanthauzo la masomphenyawo.”

17Atayandikira kumene ndinayima, ndinachita mantha ndi kugwa chafufumimba. Iye anati, “Mwana wa munthu, zindikira kuti masomphenyawa akunena za nthawi yachimaliziro.”

18Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.

19Iye anati, “Ine ndikuwuza zimene zidzachitike ukadzatha mkwiyo, chifukwa masomphenyawa ndi a nthawi ya chimaliziro.” 20Nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri imene unayiona, ikuyimira mafumu a Amedi ndi Aperezi. 21Mbuzi yayimuna ija ndi mfumu ya Agriki, ndipo nyanga yayikulu pakati pa maso ake aja ndi mfumu yoyamba. 22Kunena za nyanga inathyoka ija ndi nyanga zinayi zimene zinaphuka mʼmalo mwake zikutanthauza maufumu anayi amene adzatuluka mʼdziko lake; koma sizidzafanana mphamvu ndi ufumu woyambawo.

23“Pa masiku otsiriza a maufumuwa, machimo awo atachulukitsa, padzadzuka mfumu yaukali ndi yochenjera kwambiri. 24Idzakhala yamphamvu kwambiri koma osati mphamvu za iyo yokha. Idzawononga koopsa ndipo idzapambana mu chilichonse chimene idzachite. Mfumuyi idzawononga anthu amphamvu ndi anthu oyera omwe. 25Chifukwa cha kuchenjera kwake chinyengo chidzachuluka pa nthawi ya ulamuliro wake, ndipo idzadzikuza kuposa onse. Pamene oyera mtima adzaona ngati kuti ali otetezedwa, iyo idzawononga ambiri ndi kuwukira ngakhale Mfumu ya mafumu. Komabe idzawonongedwa, koma osati ndi mphamvu za munthu.

26“Masomphenya okhudza madzulo ndi mmawa amene unawaona aja ndi woona, koma uwasunge masomphenyawa mwachinsinsi popeza ndi onena za masiku a mʼtsogolo kwambiri.”

27Ine Danieli ndinafowoka ndipo ndinadwala masiku angapo. Kenaka ndinadzuka ndi kupitiriza ntchito za mfumu. Ndinada nkhawa ndi masomphenyawo; ndipo sindinathe kuwamvetsa.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Даниял 8:1-27

Видение о баране и козле

1В третий год правления царя Валтасара (в 551 г. до н. э.) мне, Даниялу, было видение, после того, которое уже являлось мне. 2В своём видении я находился в крепости города Сузы, что в провинции Елам; я видел, что нахожусь возле канала Улай. 3Я поднял взгляд и увидел барана, который стоял рядом с каналом. У него было два рога. Оба рога были длинными, но один был длиннее другого, и вырос он позже. 4Я видел, как баран бодался к западу, к северу и к югу. Ни один зверь не мог противостоять ему, и никто не мог спасти от него. Он делал, что хотел, и становился велик.

5Пока я размышлял об этом, внезапно с запада явился козёл, который шёл по всей земле, не касаясь её. У козла между глазами был большой рог. 6Он пошёл к двурогому барану, которого я видел стоящим у канала, и в страшной ярости бросился на него. 7Я видел, как он приблизился к барану и, рассвирепев, поразил барана и сломал ему оба рога. Баран не мог противостоять ему; козёл швырнул его на землю и растоптал его, и не было никого, кто мог бы спасти от него барана. 8Козёл сильно возвеличился, но на вершине его силы большой рог его был сломан, и на его месте выросли четыре больших рога, обращённые к четырём сторонам света.

9Из одного из них вышел другой рог, который сперва был мал, но потом очень сильно вырос к югу, и к востоку, и к прекрасной стране (Исраилу). 10Он вознёсся до небесного воинства, поверг на землю часть его и часть звёзд и растоптал их. 11Даже по отношению к Вождю небесного воинства он поступал высокомерно: он отнял у Него ежедневную жертву, и место Его святилища было поругано. 12Из-за мятежа воинство было отдано ему вместе с ежедневной жертвой. Он поверг истину на землю и преуспевал во всём, что творил8:9-12 Рог в этих стихах – это Антиох IV Епифан («прославленный»), получивший прозвище Епиман («безумец») (175–164 гг. до н. э.). Он с помощью интриг завладел престолом и стал страшным врагом народа Всевышнего, осквернив в 168 г. до н. э. Иерусалимский храм и прекратив жертвоприношения (см. ст. 23-25). Антиох Епифан также служит прообразом врага аль-Масиха, который должен появиться в конце времён (см. 11:21-45; 1 Ин. 2:18; 2 Фес. 2:3-4; Отк. 13:5-8)..

13Затем я услышал двух ангелов, говорящих друг с другом. Один из них спросил:

– Сколько времени продлится то, что было в этом видении о ежедневной жертве, о мятеже, что ведёт к опустошению, и о попрании святилища и воинства?

14Другой ответил ему8:14 Или: «мне».:

– Две тысячи триста вечерних и утренних жертв8:14 Если считать по две жертвы в день (утренняя и вечерняя) получается 1 150 дней, т. е. три с небольшим года.; затем святилище будет освящено заново.

Толкование видения

15Пока я, Даниял, видел это видение и старался понять его, передо мной встал некто в облике человека. 16И я услышал над каналом Улай человеческий голос, взывающий:

– Джабраил, объясни ему это видение.

17Когда он подошёл к тому месту, где я стоял, я испугался и пал лицом на землю.

– Человек, – сказал мне он, – пойми, что это видение относится к концу времён.

18Когда он говорил со мной, я провалился в глубокий обморок, упав лицом на землю. Но он прикоснулся ко мне и поднял меня на ноги.

19Он сказал:

– Слушай, и я расскажу тебе о том, что произойдёт потом, во времена гнева, потому что видение относится к установленному времени конца. 20Двурогий баран, которого ты видел, – это цари Мидии и Персии. 21Косматый козёл – это Греческое царство, а большой рог у него между глаз – это первый царь8:21 Это Александр Македонский (Великий) (336–323 гг. до н. э.). Арабский вариант его имени: Искандер Зу-л-карнайн («двурогий»).. 22Четыре рога, сменившие первый, который был сломан, – это четыре царства, которые возникнут из этого народа, но не будут обладать той же силой8:22 Империя Александра была разделена между его полководцами. Селевк получил Сирию и Месопотамию, Птолемей – Египет, Лисимах – Фракию и части Малой Азии, Кассандр – Македонию и Грецию..

23В конце их царствования, когда мятежники достигнут предела беззаконий, явится жестокосердный царь, искусный в кознях. 24Он станет очень силён, хотя и не своей собственной силой. Он произведёт непостижимое опустошение и преуспеет во всём, что ни сделает. Он будет губить сильных и святой народ. 25Его хитрость даст его коварным планам успех, и он сочтёт себя великим. Без предупреждения он погубит многих и на Владыку владык восстанет. Он будет сокрушён, но не человеческой рукой.

26Это видение о вечерних и утренних жертвах истинно, но ты сокрой это видение, потому что оно относится к далёкому будущему.

27Я, Даниял, был изнурён и несколько дней болел. Потом я встал и начал заниматься царскими делами. Я был потрясён видением и не понимал его.