Danieli 6 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 6:1-28

Danieli Mʼdzenje la Mikango

1Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse, 2ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke. 3Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse. 4Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito. 5Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”

6Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali! 7Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango. 8Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.” 9Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.

10Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale. 11Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize. 12Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?”

Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”

13Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.” 14Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.

15Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”

16Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”

17Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli. 18Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.

19Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija. 20Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”

21Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali! 22Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”

23Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.

24Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.

25Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti,

“Mtendere uchuluke pakati panu!

26“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.

“Popeza Iye ndi Mulungu wamoyo

ndi wamuyaya;

ufumu wake sudzawonongeka,

ulamuliro wake sudzatha.

27Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,

amachita zizindikiro ndi zozizwitsa

kumwamba ndi pa dziko lapansi.

Iye walanditsa Danieli

ku mphamvu ya mikango.”

28Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

Thai New Contemporary Bible

ดาเนียล 6:1-28

ดาเนียลในถ้ำสิงโต

1ดาริอัสทรงเห็นชอบให้แต่งตั้งเสนาบดี 120 คนปกครองทั่วราชอาณาจักร 2โดยมีผู้บริหารการปกครองสามนายปกครองเหนือคนเหล่านั้น หนึ่งในสามนั้นคือดาเนียล เสนาบดีจะรายงานต่อผู้บริหารการปกครองเพื่อรักษาผลประโยชน์ของกษัตริย์ 3ดาเนียลมีคุณสมบัติดีเด่นเหนือกว่าผู้บริหารการปกครองคนอื่นและเสนาบดีทั้งหลาย กษัตริย์จึงดำริจะแต่งตั้งให้เขาดูแลทั่วราชอาณาจักร 4ด้วยเหตุนี้ผู้บริหารการปกครองคนอื่นและเสนาบดีทั้งหลายจึงพยายามจับผิดดาเนียลในงานราชการแผ่นดินแต่ไม่สำเร็จ พวกเขาไม่พบข้อบกพร่องของดาเนียลเลยเพราะเขาซื่อสัตย์ ไม่เคยฉ้อราษฎร์บังหลวงหรือละเลยหน้าที่ 5ในที่สุดคนเหล่านี้ก็พูดกันว่า “เราไม่มีทางหาเรื่องจับผิดดาเนียลคนนี้ได้เลย นอกจากเรื่องเกี่ยวกับพระบัญญัติของพระเจ้าของเขา”

6ฉะนั้นผู้บริหารการปกครองคนอื่นและเหล่าเสนาบดีจึงรวมกลุ่มกันเข้าเฝ้ากษัตริย์และทูลว่า “ข้าแต่กษัตริย์ดาริอัส ขอจงทรงพระเจริญ! 7ข้าพระบาททั้งหลาย ผู้บริหารการปกครอง ข้าหลวงภาค เสนาบดี ราชมนตรี และผู้ว่าการทั้งปวง เห็นพ้องต้องกันว่าฝ่าพระบาทควรออกพระราชกฤษฎีกาว่า หากผู้หนึ่งผู้ใดอธิษฐานต่อเทพเจ้าหรือขอต่อมนุษย์นอกเหนือจากฝ่าพระบาทในช่วงสามสิบวันที่จะถึงนี้ ข้าแต่กษัตริย์ ผู้นั้นจะต้องถูกโยนลงในถ้ำสิงโต 8บัดนี้ ข้าแต่กษัตริย์ ขอทรงออกพระราชกฤษฎีกาเป็นลายลักษณ์อักษรที่ไม่มีผู้ใดเปลี่ยนแปลงได้ ซึ่งตามกฎหมายของชาวมีเดียและเปอร์เซียจะยกเลิกไม่ได้” 9ฉะนั้นกษัตริย์ดาริอัสจึงให้ออกพระราชกฤษฎีกาเป็นลายลักษณ์อักษร

10เมื่อดาเนียลทราบว่าพระราชกฤษฎีกาประกาศใช้แล้ว เขาก็กลับบ้านและขึ้นไปยังห้องชั้นบนซึ่งหน้าต่างเปิดไปทางกรุงเยรูซาเล็ม เขาคุกเข่า อธิษฐานขอบพระคุณพระเจ้าของเขาวันละสามครั้งตามที่เคยปฏิบัติเสมอมา 11แล้วคนเหล่านั้นรวมกลุ่มกันไปเฝ้าดูและพบดาเนียลอธิษฐานทูลวิงวอนขอความช่วยเหลือจากพระเจ้า 12พวกเขาจึงไปเข้าเฝ้ากษัตริย์และทูลเกี่ยวกับพระราชกฤษฎีกาว่า “ฝ่าพระบาททรงออกพระราชกฤษฎีกาแล้วไม่ใช่หรือว่า หากผู้หนึ่งผู้ใดอธิษฐานต่อเทพเจ้าหรือขอต่อมนุษย์นอกเหนือจากฝ่าพระบาทในช่วงสามสิบวันนี้ ข้าแต่กษัตริย์ ผู้นั้นจะต้องถูกโยนลงในถ้ำสิงโต?”

กษัตริย์ตรัสตอบว่า “กฤษฎีกานั้นมีผลบังคับใช้ตามกฎหมายของชาวมีเดียและเปอร์เซียซึ่งยกเลิกไม่ได้”

13พวกเขาจึงทูลกษัตริย์ว่า “ข้าแต่กษัตริย์ ดาเนียลซึ่งเป็นเชลยคนหนึ่งจากยูดาห์ไม่ใส่ใจในฝ่าพระบาทหรือพระราชกฤษฎีกาที่ทรงให้บันทึกเป็นลายลักษณ์อักษร เขายังคงอธิษฐานวันละสามครั้ง” 14เมื่อกษัตริย์ทรงทราบเช่นนี้ก็ทุกข์พระทัยยิ่งนัก ทรงครุ่นคิดหาวิธีช่วยเหลือดาเนียลจนพลบค่ำ

15คนเหล่านั้นก็รวมกลุ่มกันมาเข้าเฝ้าและทูลว่า “ข้าแต่กษัตริย์ ขอทรงระลึกว่าตามกฎหมายของชาวมีเดียและเปอร์เซีย คำสั่งหรือกฤษฎีกาใดๆ ของกษัตริย์ที่ออกไปจะเปลี่ยนแปลงไม่ได้เลย”

16ฉะนั้นกษัตริย์จึงมีพระบัญชา และพวกเขาก็จับดาเนียลโยนลงในถ้ำสิงโต กษัตริย์ตรัสกับดาเนียลว่า “ขอให้พระเจ้าที่เจ้าปรนนิบัติเสมอมานั้นช่วยเหลือเจ้าเถิด!”

17เขานำหินก้อนหนึ่งมาปิดที่ปากถ้ำ แล้วกษัตริย์ประทับตราพระธำมรงค์ที่หินนั้น และบรรดาขุนนางประทับตราแหวนของตนเพื่อไม่ให้ใครมาเปลี่ยนแปลงแก้ไขสถานการณ์ของดาเนียลได้ 18แล้วกษัตริย์เสด็จกลับวัง ทรงงดเสวยและการบันเทิงทั้งปวง และพระองค์บรรทมไม่หลับตลอดทั้งคืนนั้น

19ทันทีที่ฟ้าสาง กษัตริย์ก็รีบรุดมายังถ้ำสิงโต 20เมื่อเข้ามาใกล้ถ้ำ พระองค์ตรัสเรียกดาเนียลด้วยพระสุรเสียงอันปวดร้าวว่า “โอ ดาเนียลผู้รับใช้ของพระเจ้าผู้ทรงพระชนม์อยู่ พระเจ้าที่เจ้ารับใช้เสมอมานั้นช่วยเจ้าให้พ้นจากสิงโตได้หรือเปล่า?”

21ดาเนียลทูลตอบว่า “ข้าแต่กษัตริย์ ขอจงทรงพระเจริญ! 22พระเจ้าของข้าพระบาททรงส่งทูตของพระองค์มาปิดปากสิงโตไว้ พวกมันไม่ได้ทำอะไรข้าพระบาทเลย เพราะข้าพระบาทบริสุทธิ์ในสายพระเนตรของพระเจ้า และไม่เคยทำผิดประการใดต่อหน้าองค์กษัตริย์เลย”

23กษัตริย์ทรงยินดีเป็นล้นพ้น ตรัสสั่งให้ดึงดาเนียลขึ้นจากถ้ำ เมื่อดาเนียลขึ้นมาแล้วปรากฏว่าเขาไม่มีบาดแผลใดๆ เพราะเขาไว้วางใจพระเจ้าของเขา

24กษัตริย์ทรงบัญชาให้จับบรรดาผู้ที่กล่าวหาดาเนียลอย่างผิดๆ โยนลงในถ้ำสิงโตพร้อมทั้งภรรยาและลูกๆ ร่างของคนเหล่านั้นก็ถูกสิงโตขย้ำจนกระดูกแหลกก่อนที่จะกระทบพื้นถ้ำ

25แล้วกษัตริย์ดาริอัสทรงเขียนถึงพลเมืองทุกชาติทุกภาษาทั่วอาณาจักรว่า

“ขอให้ท่านทั้งหลายเจริญรุ่งเรืองเถิด!

26“ข้าพเจ้าออกกฤษฎีกาให้ทุกคนทั่วราชอาณาจักรจงเคารพยำเกรงพระเจ้าของดาเนียล

“เพราะพระองค์ทรงเป็นพระเจ้าผู้ทรงพระชนม์อยู่

และทรงดำรงอยู่ตลอดกาล

ราชอาณาจักรของพระองค์จะไม่มีวันถูกทำลาย

ราชอำนาจของพระองค์ไม่มีที่สิ้นสุด

27พระองค์ทรงช่วยและทรงกอบกู้

ทรงกระทำหมายสำคัญและการอัศจรรย์ต่างๆ

ในสวรรค์และบนแผ่นดินโลก

พระองค์ทรงกอบกู้ดาเนียล

จากอำนาจของสิงโต”

28ดังนั้นดาเนียลจึงเจริญรุ่งเรืองในรัชกาลกษัตริย์ดาริอัส และในรัชกาลของกษัตริย์ไซรัส6:28 หรือดาริอัสนั่นคือในรัชสมัยของไซรัสแห่งเปอร์เซีย