Danieli 3 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 3:1-30

Fano la Golide ndi Ngʼanjo ya Moto

1Mfumu Nebukadinezara anapangitsa fano la golide lotalika mamita 27 ndi mulifupi mwake mamita atatu, ndipo analiyimika mʼchigwa cha Dura mʼchigawo cha Babuloni. 2Kenaka iye anayitanitsa akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, kuti abwere ku mwambo wotsekula fano limene analiyimika lija. 3Choncho akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa, ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, anasonkhana kudzachita mwambo wotsekulira fano limene mfumu Nebukadinezara analiyimika, ndipo mlaliki anayimirira pamaso pa fanolo nati:

4“Inu anthu a mitundu yonse ndi a ziyankhulo zonse, mukulamulidwa kuti muchite izi: mitundu ya anthu ndi a chiyankhulo chilichonse 5mukadzamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muyenera kulambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika. 6Aliyense amene sadzalambira ndi kupembedza adzaponyedwa nthawi yomweyo mʼngʼanjo ya moto.”

7Choncho anthu onse aja atangomva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, analambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika.

8Pa nthawi imeneyi alawuli ena anafika ndi kuwanenera zoyipa Ayuda. 9Iwo anati kwa mfumu Nebukadinezara, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali! 10Inu mfumu, mwakhazikitsa lamulo kuti aliyense akamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, ayenera kulambira ndi kupembedza fano la golide, 11ndi kuti aliyense osalambira ndi kupembedza adzaponyedwa mʼngʼanjo ya moto. 12Koma alipo Ayuda ena Sadirake, Mesaki ndi Abedinego amene munawayika kuti ayangʼanire ntchito ya dera la ku Babuloni. Anthu amenewa sakumvera inu mfumu. Iwo sakutumikira milungu yanu kapena kulambira fano la golide limene munaliyimikalo.”

13Tsono Nebukadinezara anakwiya ndi kupsa mtima kwambiri, ndipo anayitanitsa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego. Choncho amuna awa anabwera pamaso pa mfumu, 14ndipo Nebukadinezara anawafunsa kuti, “Kodi ndi zoona, Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti simukutumikira milungu yanga kapena kupembedza fano la golide ndinaliyikalo? 15Tsopano ngati muli okonzeka kulambira ndi kupembedza fano ndinalipanga, mukangomva kulira kwa lipenga chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muchita bwino. Koma ngati simulipembedza, mudzaponyedwa mʼnganjo ya moto. Nanga ndi mulungu uti amene adzatha kukupulumutsani mʼmanja anga?”

16Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anayankha mfumu Nebukadinezara kuti, “Sikoyenera kuti tikuyankheni pa nkhani imeneyi. 17Ngati tiponyedwa mʼngʼanjo ya moto, Mulungu amene timamutumikira akhoza kutipulumutsa ku ngʼanjo yamotoyo, ndipo adzatilanditsa mʼdzanja lanu mfumu. 18Koma ngakhale Mulungu wathu atapanda kutipulumutsa, tikufuna mudziwe inu mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu kapena kupembedza fano la golide limene munaliyimika.”

19Pamenepo Nebukadinezara anapsa mtima ndi Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, ndipo anayipidwa nawo. Iye analamulira kuti ngʼanjo ayitenthetse kasanu ndi kawiri kuposa nthawi zonse, 20ndipo analamula ena mwa asilikali amphamvu kwambiri mʼgulu lake lankhondo kuti amange Sadirake, Mesaki ndi Abedenego ndi kuwaponya mʼngʼanjo ya moto. 21Choncho amuna awa, atavala mikanjo yawo, mabuluku, nduwira ndi zovala zina zonse, anamangidwa ndi kuponyedwa mʼngʼanjo ya moto. 22Tsono popeza lamulo la mfumu linali lofulumiza, ngʼanjo inatenthetsedwa kowirikiza mwakuti malawi ake anapha asilikali amene ananyamula Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, 23ndipo anyamata atatuwa, ali chimangidwire, anagwera mʼngʼanjo ya moto.

24Kenaka mfumu Nebukadinezara anadabwa ndipo anafunsa nduna zake kuti, “Kodi sanali amuna atatu amene anamangidwa ndi kuponyedwa mʼmoto?”

Iwo anayankha kuti, “Ndi zoonadi, mfumu.”

25Iye anati, “Taonani! Ndikuona amuna anayi akuyendayenda mʼmoto, osamangidwa ndi osapwetekedwa ndipo wachinayi akuoneka ngati mwana wa milungu.”

26Pamenepo Nebukadinezara anayandikira pa khomo langʼanjo ya moto ndi kufuwula kuti, “Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, tulukani! Bwerani kuno!”

Ndipo Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anatuluka mʼmoto, 27ndipo akalonga, akazembe, abwanamkubwa ndi nduna zamfumu anasonkhana mowazungulira. Anaona kuti moto sunatenthe matupi awo ngakhale tsitsi kumutu kwawo silinapse; zovala zawo sizinapse, ndipo sankamveka fungo la moto.

28Kenaka Nebukadinezara anati, “Atamandike Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, amene anatumiza mngelo wake ndi kupulumutsa atumiki ake! Iwo anakhulupirira Iye ndi kunyozera lamulo la mfumu ndipo anali okonzeka kutaya moyo wawo koposa kutumikira kapena kupembedza mulungu wina aliyense wosakhala Mulungu wawo. 29Tsono ndikulamula kuti anthu a mitundu ina kaya chiyankhulo china chili chonse amene anganyoze Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego adulidwe nthulinthuli ndipo nyumba zawo ndidzagwetsa ndi kusandutsa bwinja, popeza palibe Mulungu amene akhoza kupulumutsa mʼnjira yotere.”

30Ndipo mfumu Nebukadinezara anakweza pa ntchito Sadirake, Mesaki ndi Abedenego mʼchigawo cha Babuloni.

Ang Pulong Sa Dios

Daniel 3:1-30

Nagmando si Nebucadnezar nga Simbahon ang Estatuwa

1Unya nagpahimo si Haring Nebucadnezar ug estatuwa nga bulawan.3:1 estatuwa nga bulawan: Ang buot ipasabot, estatuwa nga gihaklapan ug bulawan. Ang gitas-on niini 90 ka piye ug ang gilapdon siyam ka piye. Gipahimutang niya kini didto sa patag sa Dura, sa probinsya sa Babylon. 2-3Pagkahuman, gipatawag ni Haring Nebucadnezar ang mga gobernador, mga mayor, mga tinugyanan, mga magtatambag, mga tresurero, mga maghuhukom, mga tigdumala, ug ang uban pang mga opisyal sa mga probinsya aron motambong sa pagdedikar sa estatuwa. Sa dihang didto na sila nagtindog atubangan sa estatuwa, 4misinggit ang tigbalita, “Kamong mga katawhan sa nagkalain-laing nasod, tribo, ug pinulongan, 5pangluhod kamo ug simbaha ninyo ang estatuwa nga bulawan nga gipatindog ni Haring Nebucadnezar inigkadungog ninyo sa tingog sa budyong, plawta, kudyapi, harpa, ug uban pang mga instrumento. 6Si bisan kinsa nga dili mosimba ilabay diha-diha sa nagadilaab nga hudno.” 7Busa pagkadungog nila sa tingog sa mga instrumento miluhod dayon sila ug misimba sa estatuwa.

8Niadtong panahona, adunay mga taga-Babylon3:8 taga-Babylon: o, manalagna. Sa literal, Kaldeanhon. nga miduol sa hari ug miakusar sa mga Judio. 9Miingon sila kang Haring Nebucadnezar, “Hinaut pa nga motaas pa ang imong kinabuhi, Halangdon nga Hari! 10Dili ba nagmando ka man nga ang tanan nga makadungog sa tingog sa mga instrumento moluhod ug mosimba sa estatuwa nga bulawan, 11ug ang dili moluhod ug mosimba ilabay sa nagadilaab nga hudno? 12Angay kang masayod nga wala motuman sa imong sugo ang mga Judio nga imong gipadumala sa probinsya sa Babylon nga sila si Shadrach, Meshach, ug Abednego. Wala sila moalagad sa imong mga dios, ug wala sila mosimba sa estatuwa nga bulawan nga imong gipatindog.”

13Pagkadungog niadto sa hari labihan gayod ang iyang kasuko. Gipatawag dayon niya sila si Shadrach, Meshach, ug Abednego. 14Pag-abot nila gipangutana sila sa hari, “Tinuod ba nga wala kamo moalagad sa akong mga dios o mosimba sa estatuwa nga bulawan nga akong gipatindog? 15Karon, pangandam kamo sa pagsimba sa estatuwa inigkadungog ninyo sa tingog sa mga instrumento. Kay kon dili, diha-diha ilabay kamo sa nagadilaab nga hudno. Tan-awon ta kon may dios ba nga makaluwas kaninyo.”

16Mitubag ang tulo, “Mahal nga Hari, dili na kami kinahanglang mangatarungan pa kanimo bahin niana. 17Kon mao man gayod kana ang mahitabo, luwason kami sa Dios nga among gialagaran gikan nianang nagadilaab nga hudno, ug gikan sa imong mga kamot. 18Apan kon dili niya kami luwason, dili gihapon kami moalagad sa imong mga dios o mosimba sa estatuwa nga bulawan nga imong gipatindog.”

19Tungod sa ilang tubag misamot ang kasuko sa hari kanila, ug makita kini sa iyang dagway. Busa nimando siya nga dugangan ug pito ka pilo ang kainit sa hudno. 20Unya gisugo niya ang iyang kinakusgan nga mga sundalo nga gapuson sila si Shadrach, Meshach, ug Abednego ug ilabay ngadto sa nagadilaab nga hudno. 21Busa gigapos sila ug gilabay didto sa hudno nga nagasul-ob sa ilang mga turban ug kompleto nga mga bisti. 22Tungod sa sugo sa hari nga painiton pag-ayo ang hudno, bisan ang mga sundalo nga naglabay kanila nangamatay tungod sa hilabihan nga kainit. 23Ug silang tulo nga ginapos nahagsa didto sa nagadilaab nga hudno.

24Samtang nagtan-aw si Haring Nebucadnezar kalit nga nakatindog siya sa dakong katingala. Nangutana siya sa iyang mga opisyal, “Dili ba tulo man ka tawong ginapos ang atong gilabay sa kalayo?” Mitubag sila, “Oo, Mahal nga Hari.” 25Miingon ang hari, “Tan-awa ninyo! Upat ang nakita ko nga nagalakaw-lakaw sa kalayo. Dili na sila ginapos ug wala sila maunsa. Ang usa kanila morag anghel.”3:25 anghel: sa literal, anak sa (mga) dios. Tan-awa ang bersikulo 28.

26Busa, miduol si Nebucadnezar sa pultahan sa nagadilaab nga hudno ug gitawag niya sila, “Shadrach, Meshach, ug Abednego, nga mga alagad sa Labing Halangdong Dios, gawas kamo diha! Anhi kamo dinhi!” Ug migawas silang tulo.

27Unya gitapokan sila sa mga gobernador, mga mayor, mga tinugyanan, ug sa ubang mga opisyal sa hari, ug nakita nila nga wala sila maunsa sa kalayo. Ang ilang buhok o bisti wala gayod masunog, ug bisan na lang baho sa aso wala gayod kanila.

28Tungod niadto miingon ang hari, “Dalaygon ang Dios nila ni Shadrach, Meshach, ug Abednego. Gipadala niya ang iyang anghel aron luwason ang iyang mga alagad nga misalig kaniya. Wala sila mosunod sa akong sugo nga mosimba sa estatuwa, ug mas gipalabi pa nila nga ilabay sila sa kalayo kaysa mosimba sa bisan unsang dios gawas sa ilang Dios. 29Busa nagamando ako nga si bisan kinsa nga tawo sa bisan unsa nga nasod, tribo, o pinulongan nga mosulti ug daotan batok sa Dios nila ni Shadrach, Meshach, ug Abednego, tadtaron ug gub-on ang ilang mga balay. Kay wala nay laing dios nga makaluwas sama niini.”

30Ug gihatagan sa hari sila si Shadrach, Meshach, ug Abednego ug mas taas pa nga katungdanan sa probinsya sa Babylon.