Danieli 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 2:1-49

Maloto a Nebukadinezara

1Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona. 2Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu, 3mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”

4Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”

5Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja. 6Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”

7Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”

8Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita. 9Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”

10Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi. 11Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”

12Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe. 13Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.

14Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni. 15Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli. 16Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.

17Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya. 18Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni. 19Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba, 20ndipo anati:

“Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi;

nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.

21Amasintha nthawi ndi nyengo;

amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso.

Amapatsa nzeru kwa anzeru

ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.

22Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika;

amadziwa zimene zili mu mdima,

ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.

23Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga:

mwandipatsa nzeru ndi mphamvu,

mwandiwululira zomwe tinakupemphani,

mwatiwululira maloto a mfumu.”

Danieli Atanthauzira Maloto

24Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”

25Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”

26Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”

27Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa, 28koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:

29“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika. 30Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.

31“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe. 32Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa. 33Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo. 34Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya. 35Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.

36“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu. 37Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero; 38Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.

39“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi. 40Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse. 41Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita. 42Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka. 43Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.

44“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya. 45Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa.

“Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”

46Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani. 47Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”

48Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru. 49Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

Persian Contemporary Bible

دانيال 2:1-49

خواب نبوكدنصر

1نبوكدنصر در سال دوم سلطنتش خوابی ديد. اين خواب چنان او را مضطرب كرد كه سراسيمه بيدار شد و نتوانست دوباره به خواب رود. 2پس همهٔ منجمان، جادوگران، طالع‌بينان و رمالان خود را احضار كرد تا خوابش را تعبير كنند.

وقتی همه در حضورش ايستادند 3گفت: «خوابی ديده‌ام كه مرا مضطرب كرده، از شما می‌خواهم آن را برای من تعبير كنيد.»

4آنها به زبان ارامی به پادشاه گفتند: «پادشاه تا به ابد زنده بماند! خوابتان را بگوييد تا تعبيرش كنيم.»

5ولی پادشاه جواب داد: «حكم من اين است: اگر شما به من نگوييد چه خوابی ديده‌ام و تعبيرش چيست، دستور می‌دهم شما را تكه‌تكه كنند و خانه‌هايتان را خراب نمايند! 6ولی اگر بگوييد چه خوابی ديده‌ام و تعبيرش چيست، به شما پاداش و انعام می‌دهم و عزت و افتخار می‌بخشم. حال، بگوييد چه خوابی ديده‌ام و تعبيرش چيست؟»

7ايشان باز گفتند: «اگر شما خوابتان را برای ما تعريف نكنيد چطور می‌توانيم تعبيرش كنيم؟»

8پادشاه جواب داد: «مطمئنم دنبال فرصت می‌گرديد كه از حكم من جان به در ببريد؛ 9ولی بدانيد اگر خواب را نگوييد حكم من در مورد شما اجرا خواهد شد. شما با هم تبانی كرده‌ايد كه به من دروغ بگوييد به اميد اينكه باگذشت زمان اين موضوع فراموش شود. خواب مرا بگوييد تا من هم مطمئن شوم تعبيری كه می‌كنيد درست است.»

10حكيمان در جواب پادشاه گفتند: «در تمام دنيا كسی پيدا نمی‌شود كه بتواند اين خواستهٔ پادشاه را انجام دهد. تا به حال هيچ پادشاه يا حاكمی، از منجمان و جادوگران و طالع‌بينان خود چنين چيزی نخواسته است. 11آنچه كه پادشاه می‌خواهند ناممكن است. هيچكس جز خدايان نمی‌تواند به شما بگويد چه خوابی ديده‌ايد. خدايان هم با انسانها زندگی نمی‌كنند تا از ايشان كمک بگيريم.»

12پادشاه وقتی اين را شنيد چنان خشمگين شد كه فرمان قتل تمام حكيمان بابل را صادر كرد. 13دانيال و يارانش هم جزو كسانی بودند كه می‌بايست كشته شوند.

14‏-15اما دانيال نزد اريوک رئيس جلادان كه مأمور اجرای فرمان بود، رفت و با حكمت و بصيرت در اين باره با او سخن گفت. دانيال پرسيد: «چرا پادشاه چنين فرمانی صادر كرده است؟» آنگاه اريوک تمام ماجرا را برای دانيال تعريف كرد.

16پس دانيال به حضور پادشاه رفت و از او مهلت خواست تا خواب او را تعبير كند. 17سپس به خانه رفت و موضوع را با ياران خود حننيا، ميشائيل و عزريا در ميان نهاد. 18او از ايشان خواست كه از خدای آسمانها درخواست نمايند تا بر ايشان رحم كند و نشان دهد كه پادشاه چه خوابی ديده و تعبيرش چيست، مبادا با ساير حكيمان كشته شوند. 19همان شب در رؤيا آن راز بر دانيال آشكار شد و او خدای آسمانها را ستايش نموده، 20گفت: «بر نام خدا تا ابد سپاس باد! زيرا حكمت و توانايی از آن اوست، 21وقتها و زمانها در دست اوست و اوست كه پادشاهان را عزل و نصب می‌كند. اوست كه به حكيمان، حكمت و به دانايان، دانايی می‌بخشد. 22اوست كه اسرار عميق و نهان را آشكار می‌سازد. او نور است و آنچه را كه در تاريكی مخفی است، می‌داند. 23ای خدای اجدادم، از تو سپاسگزارم، زيرا به من حكمت و توانايی بخشيده‌ای و دعای ما را اجابت كرده، مرا از خواب پادشاه و معنی آن آگاه ساخته‌ای.»

24آنگاه دانيال نزد اريوک كه از طرف پادشاه دستور داشت حكيمان بابل را بكشد، رفت و گفت: «حكيمان بابل را نكش. مرا نزد پادشاه ببر تا آنچه را می‌خواهد بداند به او بگويم.»

25پس اريوک با عجله دانيال را به حضور پادشاه برد و گفت: «من يكی از اسيران يهودی را پيدا كرده‌ام كه می‌تواند خواب پادشاه را بگويد.»

26پادشاه به دانيال گفت: «آيا تو می‌توانی بگويی چه خوابی ديده‌ام و تعبيرش چيست؟»

27دانيال جواب داد: «هيچ حكيم، منجم، جادوگر و طالع‌بينی نمی‌تواند اين خواستهٔ پادشاه را به جا آورد. 28ولی خدايی در آسمان هست كه رازها را آشكار می‌سازد. او آنچه را كه در آينده می‌بايد اتفاق بيفتد، از پيش به پادشاه خبر داده است. خوابی كه پادشاه ديده، اين است:

29«ای پادشاه، وقتی در خواب بوديد، خدايی كه رازها را آشكار می‌سازد شما را از آنچه كه در آينده اتفاق خواهد افتاد آگاه ساخت. 30اما اين خواب از آن جهت كه از ديگران داناترم بر من آشكار نشد، بلكه از اين نظر بر من آشكار شد تا پادشاه از تعبير آن آگاه شوند.

31«ای پادشاه، در خواب مجسمهٔ بزرگی را ديديد كه بسيار درخشان و ترسناک بود. 32سر اين مجسمه از طلای خالص، سينه و بازوهايش از نقره، شكم و رانهايش از مفرغ، 33ساقهايش از آهن، پاهايش قسمتی از آهن و قسمتی از گل بود. 34در همان حالی كه به آن خيره شده بوديد، سنگی بدون دخالت دست انسان از كوه جدا شد و به پاهای آهنی و گلی آن مجسمه اصابت كرد و آنها را خرد نمود. 35سپس مجسمه، كه از طلا و نقره و مفرغ و گل و آهن بود، فرو ريخت و به شكل ذرات ريز درآمد و باد آنها را مانند كاه پراكنده كرد، به طوری كه اثری از آن باقی نماند. اما سنگی كه آن مجسمه را خرد كرده بود كوه بزرگی شد و تمام دنيا را در برگرفت.

36«خواب اين بود، اما حال تعبير آن:

37«ای پادشاه، شما شاه شاهان هستيد، زيرا خدای آسمانها به شما سلطنت و قدرت و توانايی و شكوه بخشيده است. 38او شما را بر تمام مردم جهان و حيوانات و پرندگان مسلط گردانيده است. سر طلايی آن مجسمه شما هستيد. 39اما وقتی سلطنت شما به پايان رسد، سلطنت ديگری2‏:39 منظور از «سلطنت ديگر» حکومت ماد و پارس است و منظور از «سلطنت سوم» حکومت يونان می‌شد.‏ روی كار خواهد آمد كه ضعيفتر از سلطنت شما خواهد بود. پس از آن، سلطنت سومی كه همان شكم مفرغی آن مجسمه باشد روی كار خواهد آمد و بر تمام دنيا سلطنت خواهد كرد. 40پس از آن، سلطنت چهارم2‏:40 «سلطنت چهارم» احتمالاً حکومت روم می‌شد.‏ به ظهور خواهد رسيد و همچون آهن قوی خواهد بود و همه چيز را در هم كوبيده خرد خواهد كرد. 41‏-42همانطور كه ديديد پاها و انگشتهای مجسمه قسمتی از آهن و قسمتی از گل بود. اين نشان می‌دهد كه اين سلطنت تقسيم خواهد شد و بعضی از قسمتهای آن مثل آهن قوی و بعضی مثل گل ضعيف خواهد بود. 43مخلوط آهن و گل نشان می‌دهد كه خانواده‌های سلطنتی سعی خواهند كرد از راه وصلت، با يكديگر متحد شوند، ولی همانطور كه آهن با گل مخلوط نمی‌شود، آنها نيز متحد نخواهند شد.

44«در دوران سلطنت آن پادشاهان، خدای آسمانها سلطنتی برقرار خواهد ساخت كه هرگز از بين نخواهد رفت و كسی بر آن پيروز نخواهد شد، بلكه همهٔ آن سلطنتها را در هم كوبيده مغلوب خواهد ساخت و خودش تا ابد پايدار خواهد ماند. 45اين است معنی آن سنگی كه بدون دخالت دست انسان از كوه جدا شد و تمام آهن، مفرغ، گل، نقره و طلا را خرد كرد. به اين وسيله خدای بزرگ آنچه را كه در آينده اتفاق خواهد افتاد، به پادشاه نشان داده است. تعبير خواب عين همين است كه گفتم.»

46آنگاه نبوكدنصر در برابر دانيال خم شده او را تعظيم كرد و دستور داد برای او قربانی كنند و بخور بسوزانند. 47پادشاه به دانيال گفت: «براستی خدای شما خدای خدايان و خداوند پادشاهان و آشكار كنندهٔ اسرار است، چون او اين راز را بر تو آشكار كرده است.»

48سپس، پادشاه به دانيال مقام والايی داد و هدايای ارزندهٔ فراوانی به او بخشيد و او را حاكم تمام بابل و رئيس همهٔ حكيمان خود ساخت. 49آنگاه پادشاه در پی درخواست دانيال، شدرک و ميشک و عبدنغو را بر ادارهٔ امور مملكتی گماشت، اما خود دانيال در دربار نبوكدنصر ماند.