Chivumbulutso 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 3:1-22

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Sarde

1“Lembera mngelo wampingo wa ku Sarde kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene amasunga mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri. Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zako; umadziwika kuti ndiwe wamoyo koma ndiwe wakufa. 2Dzuka! Limbitsa zimene zatsalira zomwe zatsala pangʼono kufa, pakuti ndaona kuti ntchito zako nʼzosakwanira pamaso pa Mulungu. 3Choncho, kumbukira zimene unalandira ndi kumva; uzisunge ndipo ulape. Koma ngati sudzuka, ndidzabwera ngati mbala ndipo sudzadziwa nthawi imene ndidzabwere kwanu.

4Komabe uli ndi anthu angapo mu Sarde amene sanadetse zovala zawo. Amenewa adzayenda ndi Ine atavala zoyera popeza ndi oyenera kutero. 5Amene adzapambane adzavala zoyera ngati ena aja. Sindidzafafaniza dzina lake mʼbuku lamoyo, koma ndidzamuchitira umboni pamaso pa Atate anga ndi angelo ake. 6Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Filadefiya

7“Lembera mngelo wampingo wa ku Filadefiya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi woyera ndi woonadi, amene ali ndi kiyi ya Davide. Iye akatsekula palibe amene angatseke; ndipo akatseka palibe amene angatsekule. 8Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa ntchito zako. Taona, ndakutsekulira pa khomo ndipo palibe wina amene angatseke. Ndikudziwa kuti uli ndi mphamvu zochepa komabe wasunga mawu anga ndipo sunandikane. 9Amene ndi mpingo wa Satana, amene amadzitcha kuti ndi Ayuda pamene sali choncho, koma ndi onama, ndidzawabweretsa kwa inu ndi kuwagwetsa pansi pa mapazi anu kuti adzazindikire kuti ndimakukondani. 10Popeza mwasunga mawu anga woti mupirire ndipo mwawugwira mtima, Inenso ndidzakupulumutsani nthawi ya mayesero imene idzabwera pa dziko lonse lapansi kuyesa onse okhala pa dziko lapansi.

11Ine ndikubwera msanga. Gwiritsitsa chimene uli nacho kuti wina angakulande chipewa chako chaufumu. 12Iye amene adzapambane ndidzamusandutsa mzati wa mʼNyumba ya Mulungu wanga. Sadzatulukamonso. Pa iye ndidzalemba dzina la Mulungu wanga ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, Yerusalemu watsopano, umene ukubwera pansi kuchokera kumwamba kwa Mulungu wanga; ndipo pa iye ndidzalembanso dzina langa latsopano. 13Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.’ ”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Laodikaya

14“Lembera mngelo wampingo wa ku Laodikaya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa Ameni, mboni yokhulupirika ndi yoona, gwero la zolengedwa zonse za Mulungu. 15Ine ndimadziwa ntchito zako, kuti sindiwe wozizira kapena wotentha. Ndikanakonda ukanakhala wozizira kapena wotentha! 16Tsono popeza ndiwe wofunda chabe, sindiwe wotentha kapena wozizira, ndatsala pangʼono kuti ndikulavule mʼkamwa mwanga. 17Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche. 18Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.

19Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa. 20Taonani ndayima pa khomo ndikugogoda. Ngati wina amva mawu anga natsekula chitseko, Ine ndidzalowamo ndi kudya naye, Ine ndi iyeyo.

21Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wokhala nane pamodzi pa mpando wanga waufumu monga mmene Ine ndinapambana ndi kukhala pansi ndi Atate anga pa mpando wawo waufumu. 22Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

New International Reader’s Version

Revelation 3:1-22

The Letter to the Church in Sardis

1“Here is what I command you to write to the church in Sardis.

Here are the words of Jesus, who holds the seven spirits of God. He has the seven stars in his hand. He says,

‘I know what you are doing. People think you are alive, but you are dead. 2Wake up! Strengthen what is left, or it will die. You have not done all that my God wants you to do. 3So remember what you have been taught and have heard. Hold firmly to it. Turn away from your sins. If you don’t wake up, I will come like a thief. You won’t know when I will come to you.

4‘But you have a few people in Sardis who are pure. They aren’t covered with evil like dirty clothes. They will walk with me, dressed in white, because they are worthy. 5Here is what I will do for anyone who has victory over sin. I will dress that person in white like those worthy people. I will never erase their names from the book of life. I will speak of them by name to my Father and his angels. 6Whoever has ears should listen to what the Holy Spirit says to the churches.’

The Letter to the Church in Philadelphia

7“Here is what I command you to write to the church in Philadelphia.

Here are the words of Jesus, who is holy and true. He holds the key of David. No one can shut what he opens. And no one can open what he shuts. He says,

8‘I know what you are doing. Look! I have put an open door in front of you. No one can shut it. I know that you don’t have much strength. But you have obeyed my word. You have not said no to me. 9Some people claim they are Jews but are not. They are liars. Their worship comes from Satan. I will make them come and fall down at your feet. I will make them say in public that I have loved you. 10You have kept my command to remain strong in the faith no matter what happens. So I will keep you from the time of suffering. That time is going to come to the whole world. It will test those who live on the earth.

11‘I am coming soon. Hold on to what you have. Then no one will take away your crown. 12Here is what I will do for anyone who has victory over sin. I will make that person a pillar in the temple of my God. They will never leave it again. I will write the name of my God on them. I will write the name of the city of my God on them. This is the new Jerusalem, which is coming down out of heaven from my God. I will also write my new name on them. 13Whoever has ears should listen to what the Holy Spirit says to the churches.’

The Letter to the Church in Laodicea

14“Here is what I command you to write to the church in Laodicea.

Here are the words of Jesus, who is the Amen. What he speaks is faithful and true. He rules over what God has created. He says,

15‘I know what you are doing. I know you aren’t cold or hot. I wish you were either one or the other! 16But you are lukewarm. You aren’t hot or cold. So I am going to spit you out of my mouth. 17You say, “I am rich. I’ve become wealthy and don’t need anything.” But you don’t realize how pitiful and miserable you have become. You are poor, blind and naked. 18So here’s my advice. Buy from me gold made pure by fire. Then you will become rich. Buy from me white clothes to wear. Then you will be able to cover the shame of your naked bodies. And buy from me healing lotion to put on your eyes. Then you will be able to see.

19‘I warn and correct those I love. So be sincere, and turn away from your sins. 20Here I am! I stand at the door and knock. If anyone hears my voice and opens the door, I will come in. I will eat with that person, and they will eat with me.

21‘Here is what I will do for anyone who has victory over sin. I will give that person the right to sit with me on my throne. In the same way, I had victory. Then I sat down with my Father on his throne. 22Whoever has ears should listen to what the Holy Spirit says to the churches.’ ”