Chivumbulutso 3 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 3:1-22

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Sarde

1“Lembera mngelo wampingo wa ku Sarde kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene amasunga mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri. Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zako; umadziwika kuti ndiwe wamoyo koma ndiwe wakufa. 2Dzuka! Limbitsa zimene zatsalira zomwe zatsala pangʼono kufa, pakuti ndaona kuti ntchito zako nʼzosakwanira pamaso pa Mulungu. 3Choncho, kumbukira zimene unalandira ndi kumva; uzisunge ndipo ulape. Koma ngati sudzuka, ndidzabwera ngati mbala ndipo sudzadziwa nthawi imene ndidzabwere kwanu.

4Komabe uli ndi anthu angapo mu Sarde amene sanadetse zovala zawo. Amenewa adzayenda ndi Ine atavala zoyera popeza ndi oyenera kutero. 5Amene adzapambane adzavala zoyera ngati ena aja. Sindidzafafaniza dzina lake mʼbuku lamoyo, koma ndidzamuchitira umboni pamaso pa Atate anga ndi angelo ake. 6Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Filadefiya

7“Lembera mngelo wampingo wa ku Filadefiya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi woyera ndi woonadi, amene ali ndi kiyi ya Davide. Iye akatsekula palibe amene angatseke; ndipo akatseka palibe amene angatsekule. 8Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa ntchito zako. Taona, ndakutsekulira pa khomo ndipo palibe wina amene angatseke. Ndikudziwa kuti uli ndi mphamvu zochepa komabe wasunga mawu anga ndipo sunandikane. 9Amene ndi mpingo wa Satana, amene amadzitcha kuti ndi Ayuda pamene sali choncho, koma ndi onama, ndidzawabweretsa kwa inu ndi kuwagwetsa pansi pa mapazi anu kuti adzazindikire kuti ndimakukondani. 10Popeza mwasunga mawu anga woti mupirire ndipo mwawugwira mtima, Inenso ndidzakupulumutsani nthawi ya mayesero imene idzabwera pa dziko lonse lapansi kuyesa onse okhala pa dziko lapansi.

11Ine ndikubwera msanga. Gwiritsitsa chimene uli nacho kuti wina angakulande chipewa chako chaufumu. 12Iye amene adzapambane ndidzamusandutsa mzati wa mʼNyumba ya Mulungu wanga. Sadzatulukamonso. Pa iye ndidzalemba dzina la Mulungu wanga ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, Yerusalemu watsopano, umene ukubwera pansi kuchokera kumwamba kwa Mulungu wanga; ndipo pa iye ndidzalembanso dzina langa latsopano. 13Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.’ ”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Laodikaya

14“Lembera mngelo wampingo wa ku Laodikaya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa Ameni, mboni yokhulupirika ndi yoona, gwero la zolengedwa zonse za Mulungu. 15Ine ndimadziwa ntchito zako, kuti sindiwe wozizira kapena wotentha. Ndikanakonda ukanakhala wozizira kapena wotentha! 16Tsono popeza ndiwe wofunda chabe, sindiwe wotentha kapena wozizira, ndatsala pangʼono kuti ndikulavule mʼkamwa mwanga. 17Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche. 18Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.

19Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa. 20Taonani ndayima pa khomo ndikugogoda. Ngati wina amva mawu anga natsekula chitseko, Ine ndidzalowamo ndi kudya naye, Ine ndi iyeyo.

21Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wokhala nane pamodzi pa mpando wanga waufumu monga mmene Ine ndinapambana ndi kukhala pansi ndi Atate anga pa mpando wawo waufumu. 22Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

Habrit Hakhadasha/Haderekh

התגלות 3:1-22

1”את המכתב החמישי כתוב אל ראש קהילת סרדיס.

אלה דבריו של המחזיק בידו את שבע רוחות האלוהים ואת שבעת הכוכבים:

’אני יודע את מעשיך; יש לך שם שאתה חי, אך למעשה אתה מת! 2התעורר! חזק את מה שנותר לך, לפני שגם המעט הזה ימות! מעשיך אינם מוצאים־חן בעיני אלוהים. 3זכור את מה שקיבלת ולמדת; חזור בתשובה וקיים את דברי אלוהים. אם תסרב להתעורר ולהתנער ממצבך, אבוא אליך בשעה בלתי־צפויה, כגנב, ואעניש אותך.

4עלי לציין שיש אצלכם בסרדיס אנשים מעטים שלא טימאו את לבושם בחלאת העולם. אנשים אלה יתהלכו איתי בלבוש לבן, כי הם ראויים לכך.

5המנצח ילבש בגדים לבנים, ולא אמחק את שמו מספר החיים; לפני אבי ומלאכיו אכריז שהוא שלי!

6מי שמסוגל לשמוע – שיקשיב לדברי הרוח אל הקהילות.‘

7”את המכתב השישי כתוב אל ראש קהילת פילדלפיא.

אלה דברי הקדוש האמיתי שבידו מפתח דוד, הפותח את אשר איש אינו יכול לסגור, והסוגר את אשר איש אינו יכול לפתוח:

8’אני מכיר אותך היטב. ראה, פתחתי לפניך דלת שאיש אינו יכול לסגרה, כי למרות שאינך חזק ביותר שמרת את דברי ולא התכחשת לשמי. 9שים לב, אני אכריח את קהילת השטן – אלא שמשקרים וטוענים שהם יהודים – להשתחוות לפניך ולהודות שאני אוהב אותך. 10מאחר ששמרת את דברי בסבלנות למרות הסבל והרדיפות, גם אני אשמור אותך משעת הסבל העומדת לבוא על העולם כולו, לבחון ולנסות את תושביו.

11אני עומד לבוא בקרוב! שמור היטב על המעט שבידך, כדי שאיש לא יגזול ממך את הכתר שמובטח לך.

12את המנצח אציב כעמוד במקדש אלוהי; הוא יהיה מוגן ובטוח, ולא יעזוב יותר את המקדש. אכתוב עליו את שם אלוהי, את שם עיר אלוהי, ירושלים החדשה היורדת מן השמים מאת אלוהי, ואת שמי החדש.

13מי שמסוגל לשמוע – שיקשיב לדברי הרוח אל הקהילות.‘

14”את המכתב השביעי כתוב אל ראש קהילת לודקיא.

אלה דברי האמן, העד הנאמן והאמיתי שהוא ראשית בריאת אלוהים:

15’אני מכיר אותך היטב – אינך קר ואינך חם. הלוואי שהיית קר או חם! 16אך מאחר שאתה פושר, אקיא אותך מפי! 17אתה חי באשליה שהינך עשיר, בעל־כוח ואינך חסר דבר, בעוד שהאמת המרה היא שאתה אומלל, עלוב, עני, עיוור ועירום! 18אני מציע לך לקנות ממני זהב טהור צרוף באש, כדי שתהיה עשיר באמת. אני גם מציע לך לקנות ממני בגדים לבנים וטהורים, כדי שלא תהיה ערום יותר ולא תתבייש, וכן תרופה לרפא את עיניך ולהשיב לך את ראייתך.

19אני תמיד מייסר ומוכיח את מי שאני אוהב. לכן, אם לא תתעורר ותחזור בתשובה, אעניש גם אותך. 20ראה, אני עומד ליד הדלת ודופק. מי שישמע את קולי ויפתח את הדלת, אבוא אליו ואתחבר איתו, והוא יתחבר איתי.

21המנצח יישב לצדי על כיסאי, כשם שאני יושב לצד אבי לאחר שניצחתי.

22מי שמסוגל לשמוע – שיקשיב לדברי הרוח אל הקהילות.‘ “