Chivumbulutso 19 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 19:1-21

Babuloni Wagwa, Haleluya!

1Zitatha izi, ndinamva chimene chinamveka ngati phokoso la gulu lalikulu mmwamba likufuwula kuti,

“Haleluya!

Chipulumutso ndi ulemerero ndi mphamvu ndi za Mulungu wathu,

2pakuti chiweruzo chake ndi choona ndi cha chilungamo.

Iye waweruza mkazi wadama wotchuka uja

amene anayipitsa dziko lonse lapansi ndi zigololo zake.

Iye wabwezera pa mkaziyo magazi a atumiki ake.”

3Ndipo anafuwulanso kuti,

“Haleluya!

Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.”

4Akuluakulu 24 aja ndi zamoyo zinayi zija anadzigwetsa pansi kupembedza Mulungu amene anakhala pa mpando waufumu. Ndipo anafuwula kuti,

“Ameni, Haleluya!”

5Kenaka mawu anachoka ku mpando waufumu kuti,

“Lemekezani Mulungu wathu

inu nonse atumiki ake,

inu amene mumamuopa,

nonse angʼono ndi akulu!”

6Kenaka ndinamva chimene chinamveka ngati gulu lalikulu, ngati mkokomo wamadzi othamanga ndipo ngati kugunda kwakukulu kwa bingu, ndipo anati,

“Haleluya!

Pakuti Ambuye Mulungu wathu Wamphamvuzonse akulamulira.

7Tiyeni tisangalale ndi kukondwera

ndi kumutamanda!

Pakuti nthawi ya ukwati wa Mwana Wankhosa yafika,

ndipo Mkwatibwi wakonzekeratu.

8Wapatsidwa nsalu yoyera kwambiri, yowala ndi yosada

kuti avale.”

(Nsalu yoyera kwambiri ikuyimira ntchito zolungama za oyera mtima).

9Kenaka mngelo anandiwuza kuti, “Lemba kuti, Odala amene ayitanidwa ku phwando la ukwati wa Mwana Wankhosa.” Ndipo anatinso, “Awa ndiwo mawu woona a Mulungu.”

10Pamenepo ndinadzigwetsa pa mapazi ake kumupembedza. Koma anandiwuza kuti, “Usatero ayi, ine ndine mtumiki mnzako ngati iwe yemwe, ndiponso ngati abale ako amene asunga umboni wa Yesu. Pembedza Mulungu. Pakuti umboni wa Yesu ndiye mzimu wa uneneri.”

Wokwera pa Kavalo Woyera

11Ndinaona kumwamba kutatsekuka ndipo patsogolo panga panali kavalo woyera, amene anakwerapo dzina lake linali Wokhulupirika ndiponso Woona. Poweruza ndi kuchita nkhondo, amachita molungama. 12Maso ake anali ngati malawi amoto, ndipo pamutu pake panali zipewa zaufumu zambiri. Anali ndi dzina lolembedwa, lodziwika ndi Iye yekha, osati wina aliyense. 13Iye anavala mkanjo woviyika mʼmagazi, ndipo dzina lake ndi Mawu a Mulungu. 14Magulu ankhondo akumwamba ankamutsatira atakwera pa akavalo oyera, ndipo iwowo atavala nsalu zoyera kwambiri ndi zosada. 15Mʼkamwa mwake munatuluka lupanga lakuthwa limene anati akaphe nalo mitundu ya anthu. Iye adzalamulira ndi ndodo yachitsulo. Iye anaponda choponderamo mphesa cha ukali wa Mulungu Wamphamvuzonse. 16Pa chovala ndi pa ntchafu pake panalembedwa dzina ili:

MFUMU YA MAFUMU NDI MBUYE WA AMBUYE.

17Ndipo ndinaona mngelo atayimirira pa dzuwa amene anafuwula ndi mawu okweza kwa mbalame zonse zowuluka mlengalenga kuti, “Bwerani, sonkhanani pamodzi ku phwando lalikulu la Mulungu. 18Kuti mudye mnofu wa mafumu, wa akulu a ankhondo, ndi wa anthu amphamvu, wa akavalo ndi okwerapo awo, ndi wa anthu onse, mfulu ndi akapolo, angʼono ndi aakulu.”

19Kenaka ndinaona chirombo chija ndi mafumu a dziko lapansi ndi magulu ankhondo atasonkhana pamodzi kuti achite nkhondo ndi wokwera pa kavalo ndi ankhondo ake. 20Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. 21Ena onse anaphedwa ndi lupanga lija linatuluka mʼkamwa mwa wokwera pa kavalo uja, ndipo mbalame zonse zinadya mokwanira mnofu wa anthu akufawo.

O Livro

Apocalipse 19:1-21

Cântico de vitória no céu

1A seguir ouvi a alta voz de uma enorme multidão no céu, clamando:

“Louvem o Senhor!

Só nele há salvação!

Pertencem-lhe, só a ele, toda a honra, todo o poder!

2Porque as suas sentenças são justas e conforme a verdade.

Castigou essa grande prostituta

que corrompia a Terra com a sua imoralidade sexual.

E foi assim que lhe pediu conta

do sangue daqueles que serviam a Deus,

e que foram assassinados no meio dela.”

3E repetiam sempre:

“Louvem o Senhor!

Para sempre há de subir o fumo do seu incêndio!”

4Então os vinte e quatro anciãos e os quatro seres viventes inclinaram-se até ao chão e adoraram a Deus, que estava sentado no trono, com estas palavras:

“É essa a verdade! Louvem o Senhor!”

5Veio uma voz do trono que dizia:

“Louvem o nosso Deus,

todos os que o servem e o temem,

tanto grandes como pequenos.”

6E ouvi de novo um clamor enorme como o de uma multidão imensa, como o de muitas vagas de um mar agitado ou como o de sucessivos trovões:

“Louvem o Senhor!

Porque o Senhor, nosso Deus,

que tem todo o poder, é quem reina.

7Alegremo-nos, com intenso júbilo,

prestemos-lhe a nossa profunda homenagem.

Chegou a altura do Cordeiro receber a sua noiva,

a qual já se aprontou.

8Ela tem o direito de se vestir

do linho mais fino e mais branco.”

Esse linho representa as obras justas e boas que praticam os filhos de Deus.

9E foi-me dito por um anjo que escrevesse o seguinte: “Felizes aqueles que são convidados para a festa de casamento do Cordeiro.” E ainda: “Foi Deus mesmo quem declarou isto.”

10Então lancei-me aos pés do anjo para o adorar, mas ele disse-me: “Não! Não faças isso! Só a Deus deves adorar! Eu estou ao serviço de Deus, tal como tu e os teus irmãos, que são testemunhas de Jesus. Adora a Deus. O motivo da profecia é para dar um testemunho claro de Jesus.”

O cavaleiro do cavalo branco

11Vi então o céu aberto e aparecer um cavalo branco montado por alguém que se chamava Fiel e Verdadeiro; aquele que julga e combate com justiça. 12Os seus olhos eram como labaredas e na cabeça tinha muitas coroas. E tinha um nome escrito nela que só ele sabia. 13A roupa que vestia tinha marcas de sangue; o seu nome é a Palavra de Deus. 14Os exércitos do céu, vestidos de linho fino, do mais branco e puro, seguiam-no em cavalos igualmente brancos. 15Na sua boca segurava uma espada afiada para com ela vencer as nações. Ele as governará com uma vara de ferro; será ele próprio quem há de pisar no lagar de Deus Todo-Poderoso o vinho da sua justa cólera contra o pecado. 16No manto que trazia, e abaixo da cintura, tinha escrito este título:

rei dos reis e senhor dos senhores.

17Vi então um anjo que recebia a luz que vinha do Sol e que bradava em alta voz a todas as aves de rapina que cruzam os ares: “Venham! Juntem-se para comer aquilo que o grande Deus vos dá; 18a carne dos que governam e a carne dos reis, generais e dos grandes guerreiros, a carne dos cavalos e dos que os montavam; enfim, a carne de todos, livres e escravos, grandes e pequenos.”

19Depois vi o monstro reunindo os governantes da Terra e os seus exércitos para lutarem contra aquele que está montado no cavalo e contra o seu exército. 20E o monstro foi feito prisioneiro e com ele o falso profeta; aquele que tinha podido fazer sinais na presença do monstro e com os quais enganava aqueles que tinham aceitado ser marcados com o sinal e adoravam a sua estátua. Ambos foram jogados vivos no lago de fogo que queima com enxofre ardente. 21E todos os soldados daqueles exércitos foram mortos com a espada afiada que estava na boca do que montava o cavalo, e todas as aves de rapina se fartaram com aquela carne humana.