Chivumbulutso 16 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 16:1-21

Mbale Zisanu ndi Ziwiri za Mkwiyo wa Mulungu

1Kenaka ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Nyumba ya Mulungu ija kuwuza angelo asanu ndi awiri kuti, “Pitani, katsanulireni pa dziko lapansi ukali wa Mulungu umene uli mʼmbale zisanu ndi ziwirizi!”

2Mngelo woyamba anapita natsanula mbale yake pa dziko lapansi ndipo zilonda zoyipa ndi zowawa zinabuka pa anthu amene anali ndi chizindikiro cha chirombo chija, napembedza fano lake.

3Mngelo wachiwiri anapita natsanula mbale yake pa nyanja ndipo madzi ake anasanduka magazi, magazi ake ngati a munthu wakufa. Chamoyo chilichonse cha mʼnyanjamo chinafa.

4Mngelo wachitatu anapita natsanula mbale yake pa mitsinje ndi akasupe amadzi ndipo zinasanduka magazi. 5Kenaka ndinamva mngelo wolamulira madzi uja akuti,

“Inu mwachita chilungamo, Inu Woyerayo,

amene mulipo ndipo munalipo;

6pakuti iwo anakhetsa magazi a oyera anu ndi aneneri anu,

nʼchifukwa chake mwawapatsa magazi kuti amwe, zomwe zikuwayenera.”

7Kenaka ndinamva mawu ochokera ku guwa lansembe akuti,

“Inde, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,

chiweruzo chanu ndi choona ndi cholungama.”

8Mngelo wachinayi anapita natsanula mbale yake pa dzuwa ndipo dzuwa linapatsidwa mphamvu yopsereza anthu ndi moto. 9Anapserera nako kutentha kwakukuluko ndipo anatukwana Mulungu, amene anali ndi ulamuliro pa miliri imeneyi, koma anakana kulapa ndi kumulemekeza.

10Mngelo wachisanu anapita natsanula mbale yake pa mpando waufumu wa chirombo chija ndipo mdima unagwa ponse pamene panali ufumu wake. Anthu analuma malilime awo chifukwa cha ululu. 11Ndipo anatukwana Mulungu wakumwamba chifukwa cha maululu awo ndi zilonda zawo koma anakana kulapa pa zimene anachita.

12Mngelo wachisanu ndi chimodzi anapita natsanula mbale yake pa mtsinje waukulu wa Yufurate, ndipo madzi ake anaphwa kuti pakhale njira yodzera mafumu ochokera kummawa. 13Kenaka ndinaona mizimu yoyipa itatu imene inkaoneka ngati achule; inatuluka mʼkamwa mwa chinjoka chija, mʼkamwa mwa chirombo chija ndi mʼkamwa mwa mneneri wonyenga uja. 14Imeneyi ndiyo mizimu ya ziwanda imene imachita zizindikiro zodabwitsa ndipo imatuluka kupita kwa mafumu a dziko lonse, kukawasonkhanitsa ku nkhondo ya pa tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuzonse.

15“Taonani, ndikubwera ngati mbala! Wodala munthu amene ali maso, nasunga zovala zake, kuti asayende maliseche kuti angaonetse maliseche ake.”

16Kenaka mizimu ija inasonkhanitsa pamodzi mafumu ku malo amene mʼChihebri amatchedwa Armagedo.

17Mngelo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mu mlengalenga ndipo ku Nyumba ya Mulungu kunamveka mawu ofuwula kuchokera ku mpando waufumu kuti, “Kwatha!” 18Kenaka kunachitika mphenzi, phokoso, mabingu ndi chivomerezi choopsa. Chivomerezi ngati ichi sichinachitikepo chikhalire cha munthu pa dziko lapansi. Chinali chivomerezi choopsa kwambiri. 19Mzinda waukuluwo unagawika magawo atatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Mulungu anakumbukira Babuloni Wamkulu namupatsa chikho chake chodzaza ndi vinyo wa ukali wa mkwiyo wake. 20Chilumba chilichonse chinathawa ndipo mapiri sanaonekenso. 21Matalala akuluakulu olemera pafupifupi makilogalamu makumi asanu anagwa kuchokera kumwamba kugwera pa anthu. Ndipo anthu anatukwana Mulungu chifukwa cha mliri wa matalala popeza unali mliri woopsa kwambiri.

Knijga O Kristu

Otkrivenje 16:1-21

1Začujem zatim kako jak glas iz hrama dovikuje sedmorici anđela: “Idite i izlijte sedam čaša Božjega gnjeva na zemlju!”

2Prvi anđeo ode i izlije posudu na zemlju. Strašni i bolni čirovi pojave se na ljudima koji nose žig Zvijeri i koji se klanjaju njezinu kipu.

3Drugi anđeo izlije posudu na more. Ono postane poput mrtvačeve krvi te svako živo biće u njemu ugine.

4Treći anđeo izlije posudu na rijeke i izvore. Oni se pretvore u krv. 5Začujem anđela koji ima vlast nad vodom kako kaže:

“Pravedan si, Ti koji jesi i koji si bio,

Sveti, što si tako dosudio.

6Oni su prolili krv tvojih svetih i tvojih proroka.

Zato ih sada krvlju napajaš.

To su i zaslužili.”

7Začujem zatim žrtvenik kako govori:

“Da, Svemogući Gospodine Bože!

Tvoje su presude pravedne i istinite!”

8Zatim četvrti anđeo izlije posudu na sunce te ono počne žeći ljude ognjem. 9Silna je žega palila ljude pa su psovali ime Boga koji ima vlast nad tim zlima. Nisu se pokajali i dali mu slavu.

10Peti anđeo izlije posudu na Zvijerino prijestolje. Njezinim kraljevstvom nato zavlada tmina. Ljudi su od muke grizli jezik 11i psovali nebeskoga Boga zbog svojih boli i čirova. Ali nisu se pokajali i obratili od svojih zlih djela.

12Šesti anđeo izlije posudu na veliku rijeku Eufrat te ona presuši da onuda mogu proći kraljevi sa sunčeva istoka. 13Ugledam zatim kako tri žabe iskaču iz usta Zmaja, Zvijeri i lažnoga proroka. 14Ti nečisti duhovi, koji čine čudesa, okupe vladare svega svijeta na rat protiv Boga, koji će se zbiti na veliki Dan Svemogućega Boga.

15“Pazite: dolazim kao tat! Blago onima koji bdiju i koji čuvaju svoje haljine da ne idu goli i da im se ne vidi sramota.”

16Oni okupe sve vojske svijeta na mjestu koje se hebrejski zove Harmagedon.

17Sedmi anđeo izlije posudu u zrak. Iz hrama, s prijestolja, jaki glas vikne: “Svršeno je!” 18Nato udare munje, grmljavina i gromovi te nastane jak potres. Otkako je ljudi, nije bilo tako silna potresa. 19Veliki grad Babilon prasne na tri dijela, gradovi naroda po svijetu sruše se. Sjetio se Bog velikome Babilonu zbog njegovih grijeha dati da pije vino iz čaše strašnoga Božjega gnjeva. 20Svi otoci pobjegnu, sve gore iščeznu. 21Na ljude s neba zapljušti strašna tuča. Padali su komadi teški po trideset pet kilograma.16:21 U grčkome: tuča teška jedan talenat. Ljudi su psovali Boga zbog tuče jer je nanosila strašno zlo.