Aroma 9 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 9:1-33

Chisankho Chopambana cha Mulungu

1Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni. 2Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga. 3Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga, 4anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake. 5Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni.

6Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli. 7Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 8Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu. 9Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

10Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake. 11Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire, 12osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.” 13Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”

14Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe! 15Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti,

“Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo,

ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”

16Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu. 17Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.” 18Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.

19Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?” 20Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’ ” 21Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?

22Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko. 23Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake 24ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina. 25Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti,

“Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’

ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”

26ndipo,

“Pamalo omwewo pamene ananena kuti,

‘Sindinu anthu anga,’

pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ ”

27Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti,

“Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja,

otsala okha ndiye adzapulumuke.

28Pakuti Ambuye adzagamula milandu

ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”

29Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti,

“Ngati Yehova Wamphamvuzonse

akanapanda kutisiyira zidzukulu,

ife tikanawonongeka

ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”

Kusakhulupirira kwa Aisraeli

30Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro 31koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire. 32Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.” 33Monga momwe kwalembedwa kuti,

“Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu,

thanthwe limene limagwetsa anthu.

Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”

Persian Contemporary Bible

رومیان 9:1‏-33

قوم واقعی خدا

1‏-3ای برادران يهودی من! ای قوم من اسرائيل! چقدر مشتاقم كه به عيسی مسيح ايمان آوريد. من به خاطر شما به شدت اندوهگينم و دائماً دردی جانكاه در وجود خود احساس می‌كنم، حتی حاضرم خودم از نجات محروم شوم تا شما نجات يابيد. عيسی مسيح شاهد است و روح‌القدس می‌داند كه اين را راست می‌گويم. 4خدا شما را مورد لطف خاص خود قرار داده است، اما شما هنوز هم مايل نيستيد به او گوش دهيد. او شما را به عنوان قوم مخصوص و برگزيدهٔ خود تعيين كرد؛ با ابر درخشندهٔ جلال خود، شما را در بيابان هدايت نمود؛ و بركات خود را به شما وعده فرمود. او شريعت و احكام خود را به شما بخشيد تا ارادهٔ او را برای زندگی خود بدانيد؛ مراسم عبادت را نيز به شما آموخت تا او را پرستش كنيد و وعده‌های عالی به شما عطا فرمود. 5مردان بزرگ خدا، اجداد شما بودند. مسيح نيز كه اكنون بر همه چيز حاكم است، از لحاظ طبيعت بشری خود، مانند شما يهودی بود. خدا را تا ابد سپاس باد!

6پس آيا خدا در انجام وعده‌های خود به يهوديان كوتاهی كرده است؟ هرگز! زيرا اين وعده‌ها به كسانی داده نشده كه فقط از پدر و مادر يهودی متولد می‌شوند، بلكه به آنانی داده شده كه براستی يهودی‌اند. 7كافی نيست كه شخص از نسل ابراهيم باشد؛ همهٔ آنانی كه از نسل ابراهيم هستند، فرزندان حقيقی او نيستند. كتاب آسمانی نيز می‌فرمايد كه گرچه ابراهيم فرزندان ديگری هم داشت، اما وعده‌های خدا فقط به پسر او اسحاق و نسل او مربوط می‌شود. 8اين نشان می‌دهد كه تمام فرزندان ابراهيم، فرزندان خدا نيستند، بلكه فقط آنانی فرزند خدا هستند كه به آن وعدهٔ نجات كه به ابراهيم داد، ايمان بياورند. 9زيرا خدا به ابراهيم فرموده بود: «سال آينده، به تو و به سارا پسری خواهم بخشيد.»

10‏-13سالها گذشت و اين پسر بزرگ شد و با دختری به نام ربكا ازدواج كرد. ربكا دوقلو آبستن شد؛ اما پيش از آنكه بزايد، خدا به او فرمود پسری كه اول به دنیا بيايد، خدمتگزار برادر دوقلوی خود خواهد شد. در كتاب آسمانی در اين باره اين گونه آمده است: «من اراده كرده‌ام كه يعقوب را بركت دهم و نه عيسو را.» خدا اين را پيش از تولد اين دو كودک فرمود، يعنی قبل از آنكه آنها عملی خوب يا بد انجام دهند. اين امر ثابت می‌كند كه كار خدا طبق تصميمی بود كه از ابتدا گرفته بود. بلی، خدا اين تصميم را به خاطر اعمال آن دو كودک اتخاذ نكرد، بلكه فقط به اين علت كه چنين اراده كرده بود.

14پس چه بگوييم؟ آيا خدا از روی بی‌انصافی عمل می‌كرد؟ هرگز! 15او يكبار به موسی فرمود: «اگر بخواهم با كسی مهربان باشم، با او مهربان خواهم بود؛ و اگر بخواهم بر كسی رحم كنم، بر او رحم خواهم كرد.»

16بنابراين، بركات خدا به خواهش يا كوشش مردم به آنان عطا نمی‌شود، بلكه به كسانی عطا می‌شود كه خدای رحيم انتخاب كرده باشد.

17فرعون، پادشاه مصر، نمونهٔ ديگری از اين واقعيت است، خدا به او فرمود كه سلطنت مصر را فقط به اين دليل به او بخشيده است تا قدرت عظيم خود را عليه او نشان دهد و تمام دنيا نام عظيم و الهی او را بشنوند. 18پس می‌بينيد كه خدا بر بعضی رحم می‌كند و بعضی ديگر را نامطيع و سرسخت می‌سازد، فقط به اين دليل كه چنين اراده فرموده است. 19ممكن است بپرسيد: «اگر چنين است، چرا خدا انسانها را برای اعمالشان سرزنش می‌كند؟ مگر ايشان می‌توانند كاری خارج از اراده و خواست او انجام دهند؟»

20اما سؤال اصلی اين است كه: «تو ای انسان، كيستی كه از خدا ايراد می‌گيری؟» آيا صحيح است كه مخلوق به خالق خود بگويد: «چرا مرا چنين ساختی؟» 21آيا كوزه‌گر حق ندارد از يک خمير، ظرفی زيبا برای مصارف عالی و ظرف ديگری برای مصارف عادی بسازد؟ 22آيا خدا حق ندارد خشم و قدرت خود را بر ضد آنانی كه شايستهٔ نابودی‌اند، نشان دهد، يعنی بر ضد آنانی كه با صبر بسيار گناهانشان را تحمل می‌كند؟ 23‏-24و آيا او حق ندارد كسان ديگری از جمله ما را، كه از پيش برای مشاهدهٔ جلالش آماده ساخته بود، چه از يهود و چه از غيريهود، دعوت كند تا عظمت جلال او را ببينيم؟

25پيشگويی «هوشع نبی» را به یاد آوريد! خدا به زبان اين نبی می‌فرمايد كه برای خود فرزندان ديگری اختيار خواهد كرد كه از قوم او، بنی‌اسرائيل نيستند؛ و با اينكه آنان قبلاً مورد مهر او نبودند، اما از آن پس ايشان را محبت خواهد نمود؛ 26و بت‌پرستانی كه خدا قبلاً دربارهٔ ايشان گفته بود كه «شما قوم من نيستيد»، اكنون آنان را با عنوان جديدی می‌شناسد: «فرزندان خدای زنده!»

27«اشعيای نبی» دربارهٔ يهوديان می‌گويد كه حتی اگر قوم اسرائيل به اندازهٔ دانه‌های شن كنار دريا زياد باشند، فقط تعداد كمی از آنان نجات خواهند يافت. 28زيرا «خداوند به سرعت و از روی انصاف، به اعمال مردم جهان رسيدگی كرده، ايشان را مجازات خواهد نمود.» 29همين نبی در جای ديگری از كتاب خود می‌گويد كه اگر خداوند قادر متعال بر يهوديان ترحم نمی‌كرد، تمام ايشان هلاک می‌شدند، همانگونه كه مردم شهرهای سدوم و عموره همگی هلاک شدند.

گمراهی قوم يهود

30بنابراين، چه نتيجه‌ای می‌گيريم؟ می‌توان چنين نتيجه گرفت كه خدا فرصتی عالی در اختيار غيريهوديان قرار داده است؛ ايشان با اينكه در گذشته در جستجوی خدا نبودند، اما اكنون می‌توانند بوسيلهٔ ايمان، بی‌گناه به حساب آيند و مورد قبول خدا قرار گيرند. 31اما يهوديان با اينكه سخت می‌كوشيدند تا با رعايت احكام و قوانين مذهبی، رضايت خدا را جلب كنند، موفق نشدند. 32به چه دليل؟ به اين دليل كه به ايمان تكيه نمی‌كردند، بلكه می‌خواستند از راه رعايت احكام شريعت و انجام اعمال نيک، در نظر خدا پاک و بی‌گناه جلوه كنند. به همين سبب نيز به آن «سنگ بزرگ لغزش» برخورد نموده، افتادند. 33خدا نيز در اين باره در كتاب آسمانی به ايشان اخطار فرموده و گفته بود:

«بر سر راه قوم يهود، سنگی گذارده‌ام كه بسياری به آن برخورده، خواهند لغزيد. (منظور از سنگ در اينجا، عيسی مسيح است.) اما كسانی كه به او ايمان آورند، هرگز پشيمان و شرمسار نخواهند شد.»