Aroma 5 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 5:1-21

Mtendere ndi Chimwemwe

1Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

6Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

9Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Slovo na cestu

Římanům 5:1-21

Víra přináší radost

1Poněvadž naše víra v Ježíše Krista má u Boha stejnou hodnotu jako nevinnost, nejsme již Bohu odcizeni. 2Právě Kristus nám umožnil tímto způsobem dosáhnout důstojného postavení u Boha. 3Naše výsada není však jen v této naději, nýbrž i v nesnázích. Víme přece, že když snášíme nesnáze, získáváme vytrvalost, 4vytrvalostí dosahujeme osvědčenost a ta nás opět vede k naději. 5A to není klamná naděje, protože Bůh nám dal svého Ducha a ten v nás probouzí lásku. 6Mějme na paměti, že za nás Kristus umíral v době, kdy jsme si zasloužili Boží odsouzení. 7A to je co říci, protože i za nejušlechtilejšího člověka málokdo takovou oběť podstoupí. 8Nám však Bůh dokázal svou lásku právě tím, že Kristus zemřel za nás, třebaže jsme byli špatní. 9Oč více můžeme počítat s jeho milostí teď, kdy jsme Kristovou obětí již očištěni od svých vin! 10Jestliže Kristova smrt smířila nás s Bohem ještě v době, kdy nás dělilo nepřátelství, tím spíše nás Kristův život zachrání před Božím hněvem nyní, kdy jsme již smířeni. 11I Bohem se tedy můžeme chlubit díky Ježíši Kristu, který nás s ním smířil.

Rozdíl mezi Adamem a Kristem

12Hřích se v tomto světě usadil prostřednictvím jednoho člověka a stejně i důsledek hříchu – smrt. A protože všichni podlehli hříchu, propadli také všichni smrti. 13Již před vydáním zákona lidé Boha neposlouchali, ale nemohli být odsouzeni podle zákona, protože ještě nebyl vydán. 14Ale výsledkem jejich neposlušnosti byla stejně smrt, i když nešlo o stejné provinění jako Adamovo. Ježíš je jakýmsi Adamovým protějškem; 15jeho působnost má pro nás stejně zásadní význam, jenže ve smyslu opačném. 16Tak jako Adamova neposlušnost přivedla k smrti celé množství lidí, tak dar Boží milosti prostřednictvím Ježíše Krista ruší všechna provinění bez ohledu na jejich množství. 17A jako vinou jediného člověka ovládla smrt celý svět, tím spíš budou prostřednictvím Ježíše Krista vládnout ti, kterým on jediný vydobyl milost a bezhříšnost. 18-19Shrnuto: Jako pro neposlušnost jednoho byli všichni lidé odsouzeni, tak zase poslušnost jednoho přinesla celému lidstvu odpuštění znamenající život. 20-21Zákon ovšem přispěl k tomu, že přestupků jen přibylo. Čím větší však odpadnutí od Boha, tím většího významu nabývá jeho milost. Odpadnutí od Božího zákona přineslo člověku smrt. Bůh však nabídl člověku milost, tedy dokonalost získanou prostřednictvím Ježíše Krista, která mu opět vrací život.