Aroma 3 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 3:1-31

Kukhulupirika kwa Mulungu

1Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

3Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula

ndi kupambana pamene muweruza.”

5Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

9Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.

11Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,

palibe amene amafunafuna Mulungu.

12Onse apatukira kumbali,

onse pamodzi asanduka opandapake.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,

palibe ngakhale mmodzi.”

13“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”

“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”

14“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”

15“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.

16Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,

17ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”

18“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס השליח אל-הרומיים 3:1-31

1אם כן, מהו יתרונו של היהודי? ומה יתרונה של המילה? 2יש יתרון רב בכל דרך.

ראשית כל, אלוהים הפקיד את דברו הכתוב בידי היהודים. 3אמנם חלק מהם לא האמין, אך האם אתם חושבים כי משום שהיהודים הפרו את הבטחתם לאלוהים, יפר אלוהים את הבטחותיו להם? 4חלילה! גם אם כל בני האדם משקרים, אלוהים נאמן ודובר אמת! הרי כתוב בתהלים שדברי אלוהים הם דברי אמת, ומשפטו תמיד משפט צדק.3‏.4 ג 4 כלשונו: למען תצדק בדבריך, תזכה בשפטיך. תהלים נא 6

5אך אם הרשעות שלנו מבליטה ומדגישה את טובו של ה׳, האם נאמר שאלוהים גורם לנו עוול בהענישו אותנו? (יש אנשים החושבים כך!)

6חלילה! אם אלוהים יתעלם מחטא, כיצד יוכל לשפוט את העולם? 7אנו כאילו אומרים, שאם על־ידי השקרים שלנו יוצאת אמת אלוהים לאור וגדל כבודו, מדוע עלינו להישפט כחוטאים? 8אם־כך, מדוע שלא נרבה לעשות מעשים רעים כדי שתצא מהם טובה? (שונאינו העלילו עלינו שכך אמרנו!) אמרו אתם, האין זה צודק להרשיע ולהעניש את אלה האומרים זאת?

9אם כן, האם היהודים טובים מהגויים? כלל לא. כבר הוכחנו שכל בני־האדם חוטאים – יהודים וגויים ללא הבדל. 10כפי שכתוב בתהלים3‏.10 ג 10 ראה תהלים נג, קמ, י, ישעיעהו נט, תהלים לו

”אין עושה טוב, אין גם אחד.

אין אף צדיק!

11אין משכיל, אין דורש את אלוהים;

12הכול סר3‏.12 ג 12 כלשונו: כולו סג יחדיו נאלחו.

אין עושה טוב, אין גם אחד.

13גרונם כקבר פתוח,

פיהם מלוכלך ומלא שקר

ולשונם נוטפת ארס.

14כן, הם מנבלים את פיהם,

15צמאי דם וחמי מזג.

16לכל מקום שהם הולכים

הם מותירים אחריהם סבל וצער.

17הם מעולם לא התנסו בתחושת השלום

והשלווה שאלוהים לבדו מעניק.

18אין הם מקדישים לאלוהים כל מחשבה,

ולא אכפת להם מה הוא חושב עליהם.“

19אנחנו יודעים כי דברי התורה מכוונים אל אלה הכפופים לה – היהודים – ואלוהים ישפוט ויעניש אותם, שכן עליהם לשמור את מצוותיו ולא להתנהג בצורה כזאת. לאיש מהם אין תירוץ! למעשה, העולם כולו עומד אשם לפני אלוהים. 20שהרי איש לא יצדק לפני אלוהים בזכות קיום התורה, מכיוון שחוקי התורה מצביעים על חטאינו ומראים לנו שאנו חוטאים. 21עתה נתגלה האופן שבו מצדיק ה׳ את האדם ללא התורה, אם כי התורה והנביאים כבר העידו על כך. 22צידוק זה ניתן לכל המאמינים בישוע המשיח, ללא הפליה. 23כי כל בני־האדם חטאו, וכולם חסרי כבוד אלוהים. 24בכל זאת, אלוהים הצדיק אותנו בחסדו חינם, על־ידי קורבנו של ישוע המשיח שהוקרב למעננו.

25אלוהים שלח את המשיח לשאת את העונש על חטאינו, כדי שעל־ידי אמונה בדמו, הוא יהיה כפרתנו – כלומר, יכפר על חטאינו. וכל זאת כדי להראות לנו את צדקתו, לאחר שברחמיו הרבים מחק את חטאי העבר. 26במעשה זה רצה אלוהים לגלות לנו את צדקתו – את סליחתו לחוטאים – ולהוכיח כי הוא עצמו צדיק, וכי הוא מצדיק את כל המאמין בישוע המשיח בנו.

27ובכן, האם יש למישהו סיבה להתגאות? ודאי שלא. מדוע? משום שאלוהים זיכה והצדיק אותנו בזכות קרבנו של המשיח ואמונתנו בו, ולא בזכות מעשינו הטובים. 28לפיכך אנו מסיקים שאדם נצדק לפני אלוהים על־ידי אמונתו בישוע המשיח בן־האלוהים, ולא על־ידי הישגיו בקיום מצוות התורה.

29החושבים אתם שאלוהים הוא אלוהי היהודים בלבד, ורק אותם הוא מושיע? ודאי שלא! אלוהים הוא גם אלוהי הגויים. 30ומכיוון שאלוהי היהודים הוא גם אלוהי הגויים, הוא מצדיק את כולנו על־ידי האמונה. 31האם בהדגישנו את חשיבות האמונה מבטלים אנו את התורה? חס וחלילה! למעשה אנחנו מקיימים אותה – דבר האפשרי רק על־ידי אמונה במשיח.