Aroma 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 2:1-29

Kuweruza Kolungama kwa Mulungu

1Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo. 2Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi. 3Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo? 4Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?

5Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa. 6Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake. 7Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. 8Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa. 9Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 10Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 11Pajatu Mulungu alibe tsankho.

12Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo. 13Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama. 14Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo. 15Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza. 16Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.

Ayuda ndi Malamulo

17Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu, 18ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo; 19ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima, 20mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi, 21tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso? 22Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo? 23Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo? 24Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”

25Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe. 26Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe? 27Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.

28Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu. 29Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.

New International Reader’s Version

Romans 2:1-29

God Judges Fairly

1If you judge someone else, you have no excuse for it. When you judge another person, you are judging yourself. You do the same things you blame others for doing. 2We know that when God judges those who do evil things, he judges fairly. 3Though you are only a human being, you judge others. But you yourself do the same things. So how do you think you will escape when God judges you? 4Do you disrespect God’s great kindness and favor? Do you disrespect God when he is patient with you? Don’t you realize that God’s kindness is meant to turn you away from your sins?

5But you are stubborn. In your heart you are not sorry for your sins. You are storing up anger against yourself. The day of God’s anger is coming. Then his way of judging fairly will be shown. 6God “will pay back each person in keeping with what they have done.” (Psalm 62:12; Proverbs 24:12) 7God will give eternal life to those who keep on doing good. They want glory, honor, and life that never ends. 8But there are others who only look out for themselves. They don’t accept the truth. They go astray. God will pour out his great anger on them. 9There will be trouble and suffering for everyone who does evil. That is meant first for the Jews. It is also meant for the Gentiles. 10But there will be glory, honor and peace for everyone who does good. That is meant first for the Jews. It is also meant for the Gentiles. 11God treats everyone the same.

12Some people do not know God’s law when they sin. They will not be judged by the law when they die. Others do know God’s law when they sin. They will be judged by the law. 13Hearing the law does not make a person right with God. People are considered to be right with God only when they obey the law. 14Gentiles do not have the law. Sometimes they just naturally do what the law requires. They are a law for themselves. This is true even though they don’t have the law. 15They show that what the law requires is written on their hearts. The way their minds judge them proves this fact. Sometimes their thoughts find them guilty. At other times their thoughts find them not guilty. 16This will happen on the day God appoints Jesus Christ to judge people’s secret thoughts. That’s part of my good news.

The Jews and the Law

17Suppose you call yourself a Jew. You trust in the law. You brag that you know God. 18You know what God wants. You agree with what is best because the law teaches you. 19You think you know so much more than the people you teach. You think you’re helping blind people. You think you are a light for those in the dark. 20You think you can make foolish people wise. You act like you’re teaching little children. You think that the law gives you all knowledge and truth. 21You claim to teach others, but you don’t even teach yourself! You preach against stealing. But you steal! 22You say that people should not commit adultery. But you commit adultery! You hate statues of gods. But you rob temples! 23You brag about the law. But when you break it, you rob God of his honor! 24It is written, “The Gentiles say evil things against God’s name because of you.” (Isaiah 52:5; Ezekiel 36:22)

25Circumcision has value if you obey the law. But if you break the law, it is just as if you hadn’t been circumcised. 26And sometimes those who aren’t circumcised do what the law requires. Won’t God accept them as if they had been circumcised? 27Many are not circumcised physically, but they obey the law. They will prove that you are guilty. You are breaking the law, even though you have the written law and are circumcised.

28A person is not a Jew if they are a Jew only on the outside. And circumcision is more than just something done to the outside of a man’s body. 29No, a person is a Jew only if they are a Jew on the inside. And true circumcision means that the heart has been circumcised by the Holy Spirit. The person whose heart has been circumcised does more than obey the written law. The praise that matters for that kind of person does not come from other people. It comes from God.