Aroma 12 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 12:1-21

Nsembe za Moyo

1Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu. 2Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro.

3Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani. 4Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana. 5Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake. 6Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake. 7Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse. 8Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.

Chikondi

9Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.

14Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.

17Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20Koma,

“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.

Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.

Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”

21Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Romanos 12:1-21

Sacrificios vivos

1Por lo tanto, hermanos, tomando en cuenta la misericordia de Dios, os ruego que cada uno de vosotros, en adoración espiritual,12:1 espiritual. Alt. racional. ofrezca su cuerpo como sacrificio vivo, santo y agradable a Dios. 2No os amoldéis al mundo actual, sino sed transformados mediante la renovación de vuestra mente. Así podréis comprobar cuál es la voluntad de Dios, buena, agradable y perfecta.

3Por la gracia que se me ha dado, os digo a todos vosotros: Nadie tenga un concepto de sí más alto que el que debe tener, sino más bien piense de sí mismo con moderación, según la medida de fe que Dios le haya dado. 4Pues, así como cada uno de nosotros tiene un solo cuerpo con muchos miembros, y no todos estos miembros desempeñan la misma función, 5también nosotros, siendo muchos, formamos un solo cuerpo en Cristo, y cada miembro está unido a todos los demás. 6Tenemos dones diferentes, según la gracia que se nos ha dado. Si el don de alguien es el de profecía, que lo use en proporción con su fe;12:6 en proporción con su fe. Alt. de acuerdo con la fe. 7si es el de prestar un servicio, que lo preste; si es el de enseñar, que enseñe; 8si es el de animar a otros, que los anime; si es el de socorrer a los necesitados, que dé con generosidad; si es el de dirigir, que dirija con esmero; si es el de mostrar compasión, que lo haga con alegría.

El amor

9El amor debe ser sincero. Aborreced el mal; aferraos al bien. 10Amaos los unos a los otros con amor fraternal, respetándoos y honrándoos mutuamente. 11Nunca dejéis de ser diligentes; antes bien, servid al Señor con el fervor que da el Espíritu. 12Alegraos en la esperanza, mostrad paciencia en el sufrimiento, perseverad en la oración. 13Ayudad a los hermanos necesitados. Practicad la hospitalidad. 14Bendecid a quienes os persigan; bendecid y no maldigáis. 15Alegraos con los que están alegres; llorad con los que lloran. 16Vivid en armonía los unos con los otros. No seáis arrogantes, sino haceos solidarios con los humildes.12:16 haceos … humildes. Alt. estad dispuestos a ocuparos en oficios humildes. No os creáis que sois los únicos que sabéis.

17No paguéis a nadie mal por mal. Procurad hacer lo bueno delante de todos. 18Si es posible, y en cuanto dependa de vosotros, vivid en paz con todos. 19No os venguéis, hermanos míos, sino dejad el castigo en las manos de Dios, porque está escrito: «Mía es la venganza; yo pagaré»,12:19 Dt 32:35 dice el Señor. 20Antes bien,

«Si tu enemigo tiene hambre, dale de comer;

si tiene sed, dale de beber.

Actuando así, harás que se avergüence de su conducta».12:20 harás … conducta. Lit. ascuas de fuego amontonarás sobre su cabeza (Pr 25:21,22).

21No te dejes vencer por el mal; al contrario, vence el mal con el bien.