Amosi 9 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.

Akuapem Twi Contemporary Bible

Amos 9:1-15

Wɔbɛsɛe Israel

1Mihuu Awurade sɛ ogyina afɔremuka no ho, na ɔkae se,

“Bɔ Asɔredan no afadum no atifi

na mma ne fapem no nwosow.

Munnwiriw ngu nnipa no nyinaa so;

wɔn a aka no mede afoa bekunkum wɔn.

Ɔbaako mpo rentumi nguan,

obiara rennya ne ho sɔnn.

2Mpo sɛ wotu fam kɔ ɔda mu a,

hɔ na me nsa bɛtwe wɔn afi aba.

Mpo sɛ wɔforo kɔ ɔsoro a,

hɔ na meyi wɔn afi aba fam.

3Mpo sɛ wɔkɔtetɛw bepɔw Karmel atifi a,

hɔ na metiw wɔn akɔkyere wɔn aba.

Mpo sɛ wɔde wɔn ho sie me wɔ po ase a,

hɔ na mɛhyɛ ɔwɔ no ama wakɔkeka wɔn.

4Mpo sɛ wɔn atamfo de wɔn kɔ nnommum mu a,

hɔ na mɛhyɛ afoa akunkum wɔn.

“Megyen mʼani ahwɛ wɔn.

Mede ɔsɛe bɛba wɔn so na meremmoa wɔn.”

5Awurade, Asafo Awurade,

Ɔno na ɔde ne nsa ka asase ma ɛnan,

ma wɔn a wɔte so nyinaa twa adwo.

Asase no nyinaa ma ne ho so te sɛ Nil

na ɛtwe te sɛ Misraim asubɔnten.

6Ɔno na osi nʼahemfi a ɛkorɔn wɔ ɔsoro

na ɔto ne fapem wɔ asase so.

Ɔno na ɔboaboa po mu nsu ano

na ohwie gu asase so.

Awurade ne ne din!

7“Mo Israelfo,

mo ho hia me sen Etiopiafo?”

Sɛnea Awurade se ni.

Manyi Israelfo amfi Misraim,

ne Filistifo amfi Kaftor,

ne Aramfo nso amfi Kir ana?

8“Ampa ara Otumfo Awurade ani

wɔ nnebɔne ahenni no so.

Mɛpepa no afi asase ani,

nanso merensɛe Yakobfi korakora,”

sɛnea Awurade se ni.

9“Na mɛhyɛ,

na mɛwosow Israelfi,

wɔ amanaman nyinaa mu,

sɛnea wohuhuw atoko so wɔ huhuamoa mu

na aba fua mpo ntɔ fam no.

10Nnebɔneyɛfo a wɔwɔ me nkurɔfo mu nyinaa

bɛtotɔ wɔ afoa ano,

wɔn a wɔka se,

‘Amanehunu rento yɛn anaa ɛremma yɛn so da no.’

Israel Nsiesiei

11“Saa da no, mɛsan aba abesi

“Dawid fi a abubu no bio.

Mesiesie ne mmeae a asɛesɛe no,

na masi no sɛnea na ɛte no,

12na wɔafa Edom nkae no

ne amanaman a me din da wɔn so.”

Awurade a waka no, ɔno na ɔbɛyɛ eyinom nyinaa.

13“Nna no reba,” sɛnea Awurade se ni,

“A nnɔbae no bɛba ntɛm ama otwafo no,

na bobe no abu so ama nea otiatia nsakyiamoa no so no.

Nsa foforo bɛsosɔ afi mmepɔw no so

na ateɛ afi nkoko no nyinaa so.

14Mede me nkurɔfo Israel nnommum bɛsan aba.

“Wɔbɛsan asiesie nkuropɔn a asɛe no na wɔatena mu.

Wɔbɛyɛ bobe nturo na wɔanom mu nsa;

wɔbɛyɛ mfikyifuw na wɔadi so nnuaba.

15Mede Israelfo bedua wɔn ankasa asase so

a wɔrentu bio da

mfi asase a mede ama wɔn no so,”

sɛnea Awurade, mo Nyankopɔn se ni.