Amosi 7 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 7:1-17

Dzombe, Moto ndi Chingwe Chowongolera Khoma

1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene. 2Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

3Kotero Yehova anakhululuka.

Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”

4Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko. 5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

6Kotero Yehova anakhululuka.

Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”

7Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma. 8Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?”

Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.”

Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.

9“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa

ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja;

ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”

Amosi ndi Amaziya

10Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo. 11Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi:

“ ‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga,

ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

12Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa. 13Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”

14Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu. 15Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’ 16Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti,

“ ‘Usanenere zotsutsa Israeli,

ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’ ”

17“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi:

“ ‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu,

ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga.

Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa,

ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu.

Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

Nova Versão Internacional

Amós 7:1-17

As Três Visões de Amós

1Foi isto que o Senhor, o Soberano, me mostrou: ele estava preparando enxames de gafanhotos depois da colheita do rei, justo quando brotava a segunda safra. 2Depois que eles devoraram todas as plantas dos campos, eu clamei: “Senhor Soberano, perdoa! Como Jacó poderá sobreviver? Ele é tão pequeno!”

3Então o Senhor arrependeu-se e declarou: “Isso não acontecerá”.

4O Soberano, o Senhor, mostrou-me também que, para o julgamento, estava chamando o fogo, o qual secou o grande abismo e devorou a terra. 5Então eu clamei: “Soberano Senhor, eu te imploro que pares! Como Jacó poderá sobreviver? Ele é tão pequeno!”

6Então o Senhor arrependeu-se e declarou: “Isso também não acontecerá”.

7Ele me mostrou ainda isto: o Senhor, com um prumo na mão, estava junto a um muro construído no rigor do prumo. 8E o Senhor me perguntou: “O que você está vendo, Amós?”

“Um prumo”, respondi.

Então disse o Senhor: “Veja! Estou pondo um prumo no meio de Israel, o meu povo; não vou poupá-lo mais.

9“Os altares idólatras de Isaque serão destruídos,

e os santuários de Israel ficarão em ruínas;

com a espada me levantarei contra a dinastia de Jeroboão”.

O Confronto entre Amós e Amazias

10Então o sacerdote de Betel, Amazias, enviou esta mensagem a Jeroboão, rei de Israel: “Amós está tramando uma conspiração contra ti no centro de Israel. A nação não suportará as suas palavras. 11Amós está dizendo o seguinte:

“ ‘Jeroboão morrerá à espada,

e certamente Israel irá para o exílio,

para longe da sua terra natal’ ”.

12Depois Amazias disse a Amós: “Vá embora, vidente! Vá profetizar em Judá; vá ganhar lá o seu pão. 13Não profetize mais em Betel, porque este é o santuário do rei e o templo do reino”.

14Amós respondeu a Amazias: “Eu não sou profeta nem pertenço a nenhum grupo de profetas7.14 Hebraico: nem filho de profeta., apenas cuido do gado e faço colheita de figos silvestres. 15Mas o Senhor me tirou do serviço junto ao rebanho e me disse: ‘Vá, profetize a Israel, o meu povo’. 16Agora ouça, então, a palavra do Senhor. Você diz:

“ ‘Não profetize contra Israel,

e pare de pregar contra a descendência de Isaque’.

17“Mas o Senhor lhe diz:

“ ‘Sua mulher se tornará uma prostituta na cidade,

e os seus filhos e as suas filhas morrerão à espada.

Suas terras serão loteadas,

e você mesmo morrerá numa terra pagã7.17 Hebraico: impura..

E Israel certamente irá para o exílio,

para longe da sua terra natal’ ”.