Amosi 6 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 6:1-14

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

1Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,

ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,

inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,

kumene Aisraeli amafikako!

2Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;

mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,

ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.

Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?

Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?

3Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,

zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.

4Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,

mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.

Mumadya ana ankhosa onona

ndi ana angʼombe onenepa.

5Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka

nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.

6Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza

ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,

koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.

7Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;

maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

8Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,

ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;

Ine ndidzawupereka mzindawu

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

9Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11Pakuti Yehova walamula kuti

nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,

ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?

Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?

Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha

ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.

13Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara

ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,

“Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu

umene udzakuzunzani

kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

阿摩司書 6:1-14

預言以色列的毀滅

1錫安生活安逸舒適的人啊,

你們有禍了!

撒瑪利亞山上自覺無憂的人啊,

你們有禍了!

你們是列國之首以色列的顯要,

以色列人都仰望你們。

2你們去甲尼看看,

然後從那裡到哈瑪大城,

再到非利士人的迦特看看。

你們比這些國家更好嗎?

他們的領土不比你們的更廣闊嗎?

3你們以為災難的日子離得還遠,

就大肆施行暴政。

4你們躺在象牙床上,靠在臥榻上,

你們吃養在圈裡的肥嫩牛羊。

5你們伴著琴聲唱慵懶的歌,

大衛一樣為自己製造樂器。

6你們以大碗狂飲,

用上等膏油抹身,

卻漠不關心約瑟家的衰亡。

7所以,你們要首先被擄,

你們的宴樂將從此消逝!

8萬軍之上帝——主耶和華憑自己起誓:

「我憎惡雅各的驕傲,

厭棄他的城堡。

我要把城和城中的一切都交給敵人。」

9那時,如果一棟房子裡剩下十人,這十人也要死亡。 10親屬抬出屍體焚燒時,必問內屋的人:「你那裡還有別人嗎?」那人必回答:「沒有。」問的人必說:「不要作聲,我們不可提耶和華的名。」

11看啊,耶和華一聲令下,

大屋頓成瓦礫,小房化為碎片。

12馬能在懸崖上奔馳嗎?

牛能在海中耕作嗎?

你們卻使公正淪為毒藥,

使公義之果變成苦艾。

13你們炫耀自己征服了羅底巴

吹噓憑自己的能力奪取了加寧

14萬軍之上帝耶和華說:

以色列家啊,

我要使一個國家興起攻擊你們,

他們要從哈馬口直至亞拉巴河,

到處欺壓你們。」