Amosi 2 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 2:1-16

1Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,

mpaka kuwasandutsa phulusa,

2Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.

Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,

mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.

3Ndidzawononga wolamulira wake

ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”

akutero Yehova.

4Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo akana lamulo la Yehova

ndipo sanasunge malangizo ake,

popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,

milungu imene makolo awo ankayitsatira,

5Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”

Chilango cha Anthu a ku Israeli

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,

ndi osauka ndi nsapato.

7Amapondereza anthu osauka

ngati akuponda fumbi,

ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.

Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,

ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.

8Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe

pa zovala zimene anatenga ngati chikole.

Mʼnyumba ya mulungu wawo

amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.

9“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,

ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza

ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.

Ndinawononga zipatso zawo

ndiponso mizu yawo.

10“Ine ndinakutulutsani ku Igupto,

ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,

kudzakupatsani dziko la Aamori.

11Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,

ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.

Kodi si choncho, inu Aisraeli?”

akutero Yehova.

12“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,

ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13“Tsono Ine ndidzakupsinjani

monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.

14Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,

munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,

wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.

15Munthu wa uta sadzalimbika,

msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,

ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.

16Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri

adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”

akutero Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Amosʼ Bog 2:1-16

1Herren siger:

„Moab har gjort oprør gang på gang,

jeg vil ikke holde min straf tilbage.

De hånede Edoms afdøde konge

ved at brænde hans knogler til kalk.

2Derfor sætter jeg ild til Moab

nedbrænder Kerijots fæstningsværker.

Moab vil gå til i kampens hede,

vædderhorn og krigshyl viser dets fald.

3Jeg tilintetgør landets konge

og gør det af med alle dets ledere.”

Gud har talt!

Dom over Juda

4Herren siger:

„Juda har gjort oprør gang på gang,

jeg vil ikke holde min straf tilbage.

De har forkastet mine bud

og gjort oprør mod mine befalinger.

De blev ført vild af de falske guder,

som deres forfædre besluttede at følge.

5Derfor sætter jeg ild til Juda,

nedbrænder Jerusalems fæstningsværker.”

Dom over Israel

6Herren siger:

„Israel har gjort oprør gang på gang,

jeg vil ikke holde min straf tilbage.

De sælger de fattige som slaver,

når de ikke kan betale deres gæld.

7De træder de svage ned i skidtet

og skubber de sagtmodige væk.

Far og søn krænker mit hellige navn

ved at gå ind til den samme luder,

8de lægger sig ved afgudsalteret

på kapper, de har taget i pant.

I afgudstemplerne svælger de i vin,

de har købt for penge, de har taget i bøder.

9Har I glemt, at jeg udryddede amoritterne foran jer?

De var høje som cedre og stærke som ege.

Jeg rev bladene af dem

og skar rødderne over.

10Var det ikke mig, som førte jer ud af Egypten

og holdt jer i live de 40 år i ørkenen?

Var det ikke mig, der hjalp jer,

så I kunne indtage amoritternes land?

11Jeg lod nogle af jeres sønner vokse op som profeter

og andre blev indviet som naziræere.

Er det ikke rigtigt, mit folk, Israel?

12Men I lokkede naziræerne til at drikke vin,

og I forbød profeterne at profetere.

13Derfor vil jeg knuse jer,

som en vogn læsset med neg knuser, hvad den kører over.

14Den hurtige når ikke at undslippe,

den stærke har ikke gavn af sine kræfter.

Krigeren kan ikke redde sit liv,

15bueskytten kan ikke holde stand.

De hurtigste løbere er for langsomme,

rytterne når ikke at slippe væk.

16Selv de modigste smider den dag deres våben

og flygter i håb om at redde livet.”

Gud har talt!