Akolose 4 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 4:1-18

1Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.

Malangizo Ena

2Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika. 3Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende. 4Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera. 5Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo. 6Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.

Mawu Otsiriza

7Tukiko adzakuwuzani zonse za ine. Iye ndi mʼbale wokondedwa, mtumiki wokhulupirika ndiponso wantchito mnzanga mwa Ambuye. 8Ine ndikumutumiza kwa inu ndi cholinga choti mudziwe zimene tikukumana nazo ndiponso kuti alimbikitse mitima yanu. 9Iye akubwera ndi Onesimo, mʼbale wathu wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ndi mmodzi mwa inu. Iwo adzakuwuzani zonse zimene zikuchitika kuno.

10Aristariko, wamʼndende mnzanga akupereka moni, Marko akuperekanso moni, msuweni wa Barnaba. (Inu munawuzidwa kale za Iye. Iye akabwera kwanuko, mulandireni). 11Yesu wotchedwa Yusto, akuperekanso moni. Amenewa ndi Ayuda okhawo pakati pa atumiki anzanga mu ufumu wa Mulungu, ndipo aonetsa kuti ndi chitonthozo kwa ine. 12Epafra ndi mmodzi mwa inu ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu, akupereka moni. Iyeyu nthawi zonse amakupemphererani mwamphamvu, kuti mukhazikike pa chifuniro chonse cha Mulungu, mukhale okhwima ndi otsimikiza kwathunthu. 13Ine ndikumuchitira umboni kuti amagwira ntchito mwamphamvu chifukwa cha inu ndiponso kwa amene ali ku Laodikaya ndi Herapoli. 14Luka, dotolo wathu wokondedwa ndi Dema, akupereka moni. 15Perekani moni kwa abale a ku Laodikaya, ndiponso kwa Numfa ndi mpingo wa mʼnyumba mwake.

16Kalata iyi ikawerengedwa pakati panu, muonetsetse kuti ikawerengedwenso ku mpingo wa ku Laodikaya ndipo inunso muwerenge kalata yochokera ku Laodikaya.

17Uzani Arkipo kuti, “Wonetsetsa kuti wamaliza ntchito imene unayilandira mwa Ambuye.”

18Ine Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa moni uwu. Kumbukirani kuti ndili mu unyolo. Chisomo chikhale ndi inu.

Knijga O Kristu

Kološanima 4:1-18

1Gospodari, postupajte pravedno i pošteno prema svojim robovima. Ne zaboravite da i vi imate Gospodara—na nebu!

Poticaj na molitvu

2Molite se ustrajno i budno, sa zahvalnošću. 3Molite se i za nas, da nam Bog otvori vrata kako bismo mogli navješćivati Kristovo otajstvo zbog kojega sam u okovima 4te da ga navijestim onako kako treba.

5Mudro postupajte prema onima koji su vani; koristite svaku prigodu da činite dobro. 6Neka vaše riječi uvijek budu ljubazne, solju začinjene, da znate što kome treba reći.

Posljednje napomene i pozdravi

7Moj voljeni brat Tihik, vjerni sluga Gospodnji, ispričat će vam sve o meni. 8Šaljem ga k vama baš zato da znate kako smo i da vas ohrabri. 9Šaljem vam i vjernoga, dragog brata Onezima, vašega zemljaka. On i Tihik ispričat će vam kako je ovdje.

10Pozdravlja vas Aristarh, koji je sa mnom u zatvoru, te Barnabin nećak Marko, za kojega sam vas već prije uputio da ga lijepo primite dođe li k vama. 11Pozdravlja vas i Isus, kojega zovemo Just. To su jedini moji suradnici na kraljevstvu Božjemu koji su židovskoga podrijetla. Oni su mi bili utjeha.

12Pozdravlja vas vaš zemljak Epafra, sluga Krista Isusa. On se uvijek žarko moli za vas da, prema Božjoj volji, budete zreli i čvrsti u vjeri. 13Zaista vam mogu reći da se svojski trudi za vas, kao i za kršćane u Laodiceji i u Hierapolu.

14Pozdravljaju vas dragi liječnik Luka i Dema. 15Pozdravite braću i sestre u Laodiceji te Nimfu i Crkvu koja se sastaje u njezinu domu.

16Kad pročitate ovo pismo, neka ga pročitaju i u laodicejskoj Crkvi, a vi pročitajte ono koje sam njima napisao. 17Arhipu recite da obavlja službu koju mu je Gospodin dao.

18Evo i pozdrava mojom, Pavlovom rukom.

Sjećajte se mojih okova.

Neka je s vama Božja milost.