Akolose 3 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 3:1-25

Moyo Watsopano

1Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu. 2Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi. 3Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. 4Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.

5Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano. 6Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera. 7Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja. 8Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa. 9Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake 10ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake. 11Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.

12Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira. 13Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu. 14Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.

15Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika. 16Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika. 17Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Malangizo a Moyo wa Mʼbanja la Chikhristu

18Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.

19Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.

20Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.

21Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.

22Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye. 23Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu. 24Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira. 25Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס השליח אל-הקולוסים 3:1-25

1הואיל וקמתם לחיים חדשים עם המשיח, רכזו את תשומת לבכם באוצרות ובברכות שבשמים, שם יושב המשיח לימין האלוהים. 2רכזו את מחשבותיכם בכל מה שנוגע למלכות השמים, ואל תדאגו לדברי העולם הזה, 3כי מתם עם המשיח, וחייכם שמורים איתו אצל אלוהים. 4וכאשר המשיח, שהוא חיינו, ישוב אלינו, אתם תקרינו כבוד והדר יחד איתו.

5לפיכך המיתו את התאוות והיצרים הרעים שחבויים בכם: זנות, ניאוף, מעשי זימה וטומאה, ואל תשתעבדו לחומרנות שבעולם, כי בעיני אלוהים זוהי עבודת אלילים, 6והוא יעניש בחומרה את כל מי שממרה את פיו בעניינים אלה. 7גם אתם עשיתם את המעשים הנוראים האלה לפני שהאמנתם במשיח, 8אך עתה עליכם להסיר מעליכם כל רוגז, כעס, רשע, שנאה, גידופים וניבול־פה.

9אל תשקרו איש לרעהו, שהרי הסרתם מעצמכם את הטבע הישן ואת כל הרוע הנובע ממנו. 10פתחתם בחיים חדשים לגמרי, שבהם אתם לומדים לעשות את הטוב והישר, ואתם לומדים יותר ויותר על טבעו ודמותו של המשיח, אשר העניק לכם את החיים הנפלאים האלה שממלאים אתכם. 11בחיים אלה אין כל חשיבות למין, דת, גזע, השכלה, מצב כלכלי או מעמד חברתי. חשובה רק האמונה במשיח שמזמינה אליה כל אדם.

12היות שאלוהים בחר בכם והעניק לכם חיים חדשים אלה, ומשום שהוא אוהב אתכם מאוד ודואג לכם, עליכם לנהוג בזולת ברוך וטוב־לב. אל תנסו לעשות רושם על איש, היו מוכנים לסבול בשקט ובסבלנות, 13היו אדיבים, סלחניים ואל תשמרו טינה לאיש. זכרו: עליכם לסלוח איש לרעהו כשם שהמשיח סלח לכם! 14אך מעל הכול, אהבו איש את רעהו אהבה אמיתית! אהבה כזאת תאחד את כולכם בהרמוניה שלמה. 15דאגו לכך שהשקט והשלווה הבאים מהמשיח ימלאו תמיד את לבכם ומצפונכם, כי זוהי זכותכם וחובתכם כאיברי גוף־המשיח, והודו לאלוהים תמיד.

16זכרו את דברי המשיח, כי דבריו וחוכמתו יעשירו את חייכם בתוכן ויחכימו אתכם; למדו אותם איש את רעהו, ושירו לה׳ בהכרת תודה מזמורי תהלים ושירים רוחניים. 17אמרו ועשו כל דבר בשם ישוע המשיח אדוננו, והודו לאלוהים האב באמצעותו.

18נשים, שמענה בקול בעליכן, כי זהו רצון האלוהים.

19בעלים, אהבו את נשותיכם ונהגו בהן בעדינות ולא בגסות.

20ילדים, אלוהים רוצה שתשמעו תמיד בקול הוריכם.

21אבות, אל תציקו לילדיכם יותר מדי, כי הם עלולים לאבד את סבלנותם ולמאוס בכל.

22‏-23עבדים, שמעו תמיד בקול אדוניכם! לא רק כשהם נמצאים לידכם, אלא כל הזמן! כי עליכם להשתדל למצוא־חן בעיני אלוהים ולא בעיני בני־אדם.

24וזכרו, אלוהים ישלם לכם מאוצרותיו גמול מלא על עבודתכם ושירותכם למען המשיח. 25אבל אוי לו לעושה הרע! הוא יקבל את מה שמגיע לו, כי אלוהים אינו נושא פנים.