Ahebri 8 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 8:1-13

Mkulu wa Ansembe wa Pangano Latsopano

1Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba. 2Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.

3Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka. 4Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo. 5Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.” 6Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.

7Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake. 8Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati,

“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

9Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo,

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto

chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija

ndipo Ine sindinawasamalire,

akutero Ambuye.

10Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli:

Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye,

Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo,

ndi kulemba mʼmitima mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

11Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake,

kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye

chifukwa onse adzandidziwa,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.

12Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

13Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Евреям 8:1-13

Иса – Верховный Священнослужитель нового соглашения

1Главное из того, о чём мы вам говорим, – это то, что у нас есть такой Верховный Священнослужитель, Который находится на небесах по правую сторону от престола Всемогущего8:1 См. Заб. 109:1., 2служитель в святилище, в истинном священном шатре8:2 Священный шатёр – шатёр, служивший походным святилищем исраильтянам во время их странствия по пустыне., воздвигнутом не людьми, а Вечным.

3Каждый верховный священнослужитель определён на то, чтобы приносить приношения и жертвы, поэтому и наш Верховный Священнослужитель должен был иметь что-то, что можно было бы принести в жертву. 4Если бы Он был сейчас на земле, Он не был бы даже священнослужителем, потому что уже существуют священнослужители, приносящие жертвы в соответствии с Законом. 5Они совершают служение в святилище, которое служит лишь подобием и тенью небесного. Поэтому Муса, перед тем как строить священный шатёр, был предупреждён: «Смотри, – сказал Аллах, – сделай всё точно по образцу, который был тебе показан на горе»8:5 Исх. 25:40.. 6Но сейчас аль-Масиху поручено служение, которое намного превосходит служение земных священнослужителей, потому что Он – посредник лучшего священного соглашения Аллаха с человеком, основанного на лучших обещаниях.

7Если бы первое священное соглашение8:7 Первое священное соглашение – см. Исх. 19:3-8; Втор. 5. было без недостатков, то не было бы нужды во втором. 8Но Аллах, видя недостатки людей, говорит:

«Приближается время, – говорит Вечный, –

когда Я заключу новое священное соглашение

с народом Исраила и Иудеи.

9Это соглашение будет не таким,

какое Я заключил с их праотцами,

когда Я за руку вывел их из Египта.

Тому соглашению они не были верны,

и Я отвернулся от них, –

говорит Вечный. –

10Поэтому Я в будущем заключу с народом Исраила

такое соглашение, – говорит Вечный, –

законы Мои Я вложу в их разум

и запишу в их сердцах.

Я буду их Богом,

а они будут Моим народом.

11И уже не будет друг учить друга,

и брат – брата,

говоря ему: „Познай Вечного“,

потому что Меня будут знать все,

от мала до велика.

12Ведь Я прощу их беззакония

и больше не вспомню их грехов»8:8-12 Иер. 31:31-34..

13Он назвал это священное соглашение «новым» и тем самым показал, что первое священное соглашение устарело. А то, что устарело и обветшало, – скоро исчезнет.