Ahebri 4 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 4:1-16

Mpumulo wa Anthu a Mulungu

1Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo. 2Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira. 3Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti,

“Ndili wokwiya ndinalumbira kuti,

‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’ ”

Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi. 4Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.” 5Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”

6Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo. 7Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti,

“Lero mukamva mawu ake,

musawumitse mitima yanu.”

8Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina. 9Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu; 10Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira. 11Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.

12Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima. 13Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.

Yesu Mkulu wa Ansembe Wopambana

14Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza. 15Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe. 16Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.

La Bible du Semeur

Hébreux 4:1-16

1Ainsi donc, pendant que la promesse d’entrer dans le repos prévu par Dieu est toujours en vigueur, craignons que l’un d’entre vous se trouve coupable4.1 Autres traductions : estime être resté, ou : décide de rester. d’être resté en arrière4.1 Autre traduction : d’être arrivé trop tard.. 2Car nous aussi, nous avons entendu une Bonne Nouvelle, l’Evangile, tout comme eux. Mais le message qu’ils ont entendu ne leur a servi à rien, car ils ne se sont pas associés par leur foi à ceux qui l’ont reçu4.2 Certains manuscrits portent : car ce message n’a pas rencontré la foi chez ceux qui l’ont entendu.. 3En effet, c’est nous qui avons cru, qui entrons dans ce repos, conformément à la parole de Dieu, quand il a dit :

C’est pourquoi, dans ma colère,j’ai fait ce serment :

ils n’entreront pas dans le lieu de reposque j’avais prévu pour eux !

C’est ainsi que Dieu a parlé alors que ses œuvres étaient achevées depuis la création du monde. 4En effet, il est dit quelque part à propos du septième jour : Et Dieu se reposa le septième jour de toutes ses œuvres4.4 Gn 2.2..

5Et, dans notre texte, il dit : Ils n’entreront pas dans le lieu de repos que j’avais prévu pour eux !

6Il demeure donc établi que certains doivent entrer dans le repos. Or, ceux qui ont les premiers entendu cette Bonne Nouvelle n’y sont pas entrés parce qu’ils ont désobéi à Dieu, 7c’est pourquoi Dieu fixe de nouveau un jour, qu’il appelle aujourd’hui, lorsqu’il dit beaucoup plus tard, dans les psaumes de David, ces paroles déjà citées :

Aujourd’hui,si vous entendez la voix de Dieu,

ne vous endurcissez pas.

8En effet, si Josué avait assuré le repos aux Israélites, Dieu ne parlerait pas, après cela, d’un autre jour. 9C’est donc qu’un repos de sabbat4.9 Autre traduction : une célébration de sabbat. subsiste pour le peuple de Dieu. 10Car celui qui est entré dans le repos prévu par Dieu se repose de ses œuvres, comme Dieu s’est reposé des siennes.

11Empressons-nous donc d’entrer dans ce repos afin que personne ne tombe dans la désobéissance à l’exemple des Israélites. 12Car la Parole de Dieu est vivante et efficace. Elle est plus tranchante que toute épée à double tranchant et, pénétrant jusqu’à la division de l’âme ainsi que de l’esprit, et des jointures ainsi que de la moelle4.12 D’autres comprennent : elle pénètre jusqu’au point de division de l’âme et l’esprit, des jointures et de la moelle., elle juge les dispositions et les pensées du cœur. 13Nulle créature n’échappe au regard de Dieu, tout est à nu et à découvert aux yeux de celui à qui nous devons rendre compte.

Un grand-prêtre qui nous permet de nous approcher de Dieu

14Ainsi, puisque nous avons en Jésus, le Fils de Dieu, un grand-prêtre éminent qui a traversé les cieux, demeurons fermement attachés à la foi que nous reconnaissons comme vraie. 15En effet, nous n’avons pas un grand-prêtre qui serait incapable de compatir à nos faiblesses. Au contraire, il a été tenté en tout point comme nous le sommes, mais sans commettre de péché.

16Approchons-nous donc du trône du Dieu de grâce avec une pleine assurance. Là, Dieu nous accordera sa bonté et nous donnera sa grâce pour que nous soyons secourus au bon moment.