Ahebri 3 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 3:1-19

Yesu ndi Wamkulu Kuposa Mose

1Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza. 2Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu. 3Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo. 4Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu. 5Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo. 6Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.

Chenjezo pa Kusakhulupirira

7Tsono monga Mzimu Woyera akuti,

“Lero mukamva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu

ngati munachitira pamene munawukira,

pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.

9Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa,

ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.

10Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo,

ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera,

ndipo iwo sadziwa njira zanga.’

11Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti,

‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

12Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo. 13Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo. 14Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi. 15Monga kunanenedwa kuti,

“Lero ngati mumva mawu ake,

musawumitse mitima yanu

ngati momwe munachitira pamene munawukira.”

16Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto? 17Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja? 18Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja. 19Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

Słowo Życia

Hebrajczyków 3:1-19

Jezus przewyższa Mojżesza

1Przyjaciele, jesteście święci i powołani do życia wiecznego. Pamiętajcie więc o Jezusie, Bożym posłańcu i najwyższym kapłanie naszej wiary. 2On był wierny Bogu, który Go powołał, podobnie jak Mojżesz, który wiernie służył całemu Bożemu ludowi. 3Budowniczy cieszy się jednak większym uznaniem niż budynek, który zbudował. Dlatego Jezus jest otoczony większą chwałą niż Mojżesz. 4Każdy dom ma swojego budowniczego, a stwórcą wszystkiego jest Bóg. 5Mojżesz wiernie służył Bożemu ludowi, ale był tylko sługą i zapowiadał to, co miało dopiero nastąpić. 6Chrystus natomiast, jako Syn Boży, panuje nad Bożym ludem, do którego należymy także my, jeśli ufamy Panu i pokładamy w Nim naszą nadzieję.

Ostrzeżenie przed niewiarą

7Dlatego właśnie Duch Święty mówi:

„Dziś, jeśli usłyszycie głos Boga,

8nie stawiajcie Mu oporu,

jak Izraelici podczas buntu,

gdy byli kuszeni na pustyni.

9Bóg powiedział bowiem:

Wasi przodkowie wystawiali mnie na próbę

chociaż na własne oczy widzieli to,

czego dokonałem.

Dlatego przez czterdzieści lat

10gniewałem się na to pokolenie

i powiedziałem sobie:

Ci ludzie wciąż błądzą

i nie chcą poznać mojej woli.

11Rozgniewałem się i powiedziałem:

Nie dotrą na miejsce,

w którym przygotowałem im odpoczynek”.

12Przyjaciele, uważajcie więc, aby u kogoś z was nie pojawiła się w sercu niewiara i aby nie odsunął się od żywego Boga. 13Codziennie zachęcajcie jedni drugich, dopóki trwa „dzisiaj”, aby nikt z was nie pozwolił okłamać się grzechowi i nie zaczął sprzeciwiać się Bogu. 14Mamy bowiem udział we wszystkim, co należy do Chrystusa, jeśli do końca będziemy Mu ufać. 15Właśnie dlatego powiedziano:

„Dziś, jeśli usłyszycie głos Boga,

nie stawiajcie Mu oporu,

jak Izraelici podczas buntu”.

16Kim byli ci, którzy słyszeli głos Boga, a jednak buntowali się? Czy nie byli to ludzie, którzy wcześniej pod wodzą Mojżesza wyszli z Egiptu? 17Na kogo przez czterdzieści lat gniewał się Bóg? Czy nie na tych, którzy zgrzeszyli i poumierali na pustyni? 18A jakich ludzi miał na myśli, mówiąc: „Nie dotrą na miejsce, w którym przygotowałem im odpoczynek”, jeśli właśnie nie tych, którzy okazali nieposłuszeństwo? 19Widzimy więc, że powodem, dla którego nie dotarli na miejsce, była ich niewiara!