Ahebri 3 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 3:1-19

Yesu ndi Wamkulu Kuposa Mose

1Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza. 2Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu. 3Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo. 4Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu. 5Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo. 6Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.

Chenjezo pa Kusakhulupirira

7Tsono monga Mzimu Woyera akuti,

“Lero mukamva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu

ngati munachitira pamene munawukira,

pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.

9Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa,

ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.

10Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo,

ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera,

ndipo iwo sadziwa njira zanga.’

11Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti,

‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

12Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo. 13Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo. 14Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi. 15Monga kunanenedwa kuti,

“Lero ngati mumva mawu ake,

musawumitse mitima yanu

ngati momwe munachitira pamene munawukira.”

16Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto? 17Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja? 18Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja. 19Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

Nueva Versión Internacional

Hebreos 3:1-19

Jesús, superior a Moisés

1Por lo tanto, hermanos, ustedes que han sido santificados y que tienen parte en el mismo llamamiento celestial, fijen su atención en Jesús, el apóstol y sumo sacerdote de la fe que confesamos. 2Él fue fiel al que lo nombró, como lo fue también Moisés en toda la casa de Dios. 3De hecho, Jesús ha sido estimado digno de mayor honor que Moisés, así como el constructor de una casa recibe mayor honor que la casa misma. 4Porque toda casa tiene su constructor, pero el constructor de todo es Dios. 5Moisés fue fiel como siervo sobre toda la casa de Dios para dar testimonio de lo que Dios diría en el futuro. 6Cristo, en cambio, es fiel como Hijo al frente de la casa de Dios. Y esa casa somos nosotros, siempre y cuando mantengamos3:6 mantengamos. Var. mantengamos firme hasta el fin. nuestra confianza y la esperanza que nos enorgullece.

Advertencia contra la incredulidad

7Por eso, como dice el Espíritu Santo:

«Si ustedes oyen hoy su voz,

8no endurezcan sus corazones3:8 corazones. En la Biblia, corazón se usa para designar el asiento de las emociones, pensamientos y voluntad, es decir, el proceso de toma de decisiones del ser humano.

como sucedió en la rebelión,

en aquel día de prueba en el desierto.

9Allí sus antepasados me tentaron y me pusieron a prueba,

a pesar de haber visto mis obras cuarenta años.

10Por eso me enojé con aquella generación

y dije: “Siempre se alejan de mí3:10 Siempre se alejan de mí. Lit. su corazón siempre se extravía.

y no reconocen mis caminos”.

11Así que, en mi enojo, hice este juramento:

“Jamás entrarán en mi reposo”».3:11 Sal 95:7-11.

12Cuídense, hermanos, de que ninguno de ustedes tenga un corazón pecaminoso e incrédulo que los haga apartarse del Dios vivo. 13Más bien, mientras dure ese «hoy», anímense unos a otros cada día, para que ninguno de ustedes se endurezca por el engaño del pecado. 14Hemos llegado a tener parte con Cristo, si en verdad mantenemos firme hasta el fin la confianza que tuvimos al principio. 15Como se acaba de decir:

«Si ustedes oyen hoy su voz,

no endurezcan sus corazones

como sucedió en la rebelión».3:15 Sal 95:7,8.

16Ahora bien, ¿quiénes fueron los que oyeron y se rebelaron? ¿No fueron acaso todos los que salieron de Egipto guiados por Moisés? 17¿Y con quiénes se enojó Dios durante cuarenta años? ¿No fue acaso con los que pecaron, los cuales cayeron muertos en el desierto? 18¿Y a quiénes juró Dios que jamás entrarían en su reposo, sino a los que desobedecieron?3:18 los que desobedecieron. Alt. los que no creyeron. 19Como podemos ver, no pudieron entrar por causa de su incredulidad.