Ahebri 1 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Słowo Życia

Hebrajczyków 1:1-14

Syn Boży przewyższa aniołów

1W różnych momentach historii i w różny sposób Bóg przemawiał do naszych przodków poprzez swoich proroków. 2Teraz natomiast, w czasach ostatecznych, przemówił do nas przez swojego Syna, któremu poddał wszystko i przez którego stworzył wszechświat. 3On jaśnieje chwałą Boga i ukazuje Jego istotę, a potęgą swojego słowa utrzymuje cały świat. Gdy oczyścił ludzi z grzechów, zasiadł w niebie po prawej stronie Boga.

4On jest większy od wszystkich aniołów, bo otrzymał imię przewyższające wszystkie inne tytuły. 5Do którego bowiem anioła Bóg zwrócił się, mówiąc:

„Ty jesteś moim Synem,

Ciebie dziś zrodziłem”?

O żadnym z nich nie powiedział również:

„Ja będę Jego Ojcem,

a On będzie moim Synem”.

6A gdy posłał na ziemię swojego jedynego Syna, rozkazał:

„Niech Mu oddadzą pokłon

wszyscy aniołowie Boga”.

7O aniołach zaś Bóg powiedział tak:

„Jego aniołowie będą szybcy jak wiatr,

Jego słudzy jak płomienie ognia”.

8Natomiast do swojego Syna zwrócił się, mówiąc:

„Tron Twój, Boże, trwa na wieki,

a sprawiedliwość jest podstawą Twojego królestwa.

9Kochasz prawość i nienawidzisz zła.

Dlatego Twój Bóg, Boże, wybrał Cię

i obdarzył szczęściem

większym niż kogokolwiek innego”.

10Pismo mówi o Nim:

„To Ty, Panie, stworzyłeś na początku ziemię,

a niebo jest dziełem Twoich rąk.

11Ty trwasz, a ono przeminie

i zniszczy się jak ubranie.

12Zwiniesz je jak zużytą odzież i wyrzucisz.

Ty sam pozostajesz jednak niezmienny,

a Twoje życie nigdy się nie skończy”.

13Do którego z aniołów Bóg kiedykolwiek powiedział:

„Zasiądź po mojej prawej stronie,

aż rzucę Ci pod nogi wszystkich wrogów”?

14Czy wszyscy aniołowie nie są tylko duchowymi posłańcami, mającymi służyć tym, którzy otrzymają zbawienie?