Agalatiya 2 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 2:1-21

Atumwi Alandira Paulo

1Kenaka, patatha zaka khumi ndi zinayi, ndinapitanso ku Yerusalemu, nthawi iyi ndinapita ndi Barnaba. Ndinatenganso Tito kuti apite nafe. 2Ine ndinapita chifukwa Mulungu anachita kundionetsera kuti ndipite ndipo ndinakakumana ndi atsogoleri mu msonkhano mwamseri ndi kuwafotokozera Uthenga Wabwino umene ndimalalikira pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinachita zimenezi kuti ndikhale ndi chitsimikizo kuopa kuti mwina ndinathamanga kapena ndimathamanga liwiro pachabe. 3Komatu ngakhale Tito, amene anali nane sanakakamizidwe kuti achite mdulidwe, ngakhale iyeyo anali Mgriki. 4Nkhani iyi inayambika chifukwa abale ena achinyengo amene analowerera pakati pathu kuti adzaone za ufulu umene tili nawo mwa Khristu Yesu ndikuti atisandutse akapolo. 5Ife sitinawagonjere ndi pangʼono pomwe, nʼcholinga chakuti choonadi cha Uthenga Wabwino chikhalebe ndi ife.

6Koma kunena za aja ankaoneka ngati ofunika kwambiri, chimene iwo anali sichisintha kanthu kwa ine; chifukwa Mulungu alibe tsankho, iwowo sanawonjezepo kanthu pa uthenga wanga. 7Makamaka anaona kuti ine ndinapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa anthu a mitundu ina monga momwe Petro anapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa Ayuda. 8Pakuti Mulungu, amene amagwira ntchito mu utumiki wa Petro monga mtumwi kwa Ayuda, amagwiranso ntchito mu utumiki wanga monga mtumiki kwa anthu a mitundu ina. 9Yakobo, Petro ndi Yohane, amene ankatengedwa ngati mizati, atazindikira chisomo chimene chinapatsidwa kwa ine, anagwirana chanza ndi ine ndi Barnaba kusonyeza chiyanjano chathu. Iwo anavomereza kuti ife tipite kwa anthu a mitundu ina ndipo iwo apite kwa Ayuda. 10Chimene iwo anapempha ndi chakuti ife tipitirize kukumbukira osauka, chinthu chimene ine ndinali okonzeka kuchichita.

Paulo Adzudzula Petro

11Petro atafika ku Antiokeya, ine ndinamudzudzula pa gulu chifukwa anapezeka wolakwa. 12Pakuti asanafike anthu otumidwa ndi Yakobo, iye ankadya pamodzi ndi anthu a mitundu ina. Koma atafika, iyeyo anachoka pakati pa anthuwo nakakhala pa yekha chifukwa ankaopa anthu a mʼgulu la mdulidwe. 13Ayuda enanso anamutsata pochita zachinyengozi, kotero kuti ngakhale Barnaba anasocheretsedwa chifukwa cha chinyengo chawocho.

14Koma nditaona kuti iwo sankachita molingana ndi choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinawuza Petro pamaso pa anthu onse kuti, “Iwe ndiwe Myuda koma ukukhala ngati munthu wa mtundu wina, osati Myuda. Nanga nʼchifukwa chiyani ukukakamiza anthu a mitundu ina kuti akhale ngati Ayuda?

15“Ife amene ndife Ayuda mwachibadwa, osati anthu a mitundu ina ochimwa, 16tikudziwa kuti munthu salungamitsidwa pochita ntchito za lamulo koma ndi chikhulupiriro mwa Yesu Khristu. Chomwecho, ifenso tinakhulupirira Khristu Yesu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro mwa Khristu ndipo osati pochita ntchito za lamulo, chifukwa palibe amene adzalungamitsidwa pochita ntchito za lamulo.

17“Tsono ngati ife, pamene tikufuna kulungamitsidwa mwa Khristu, zikuonekeratu poyera kuti ndifenso ochimwa, kodi zikutanthauza kuti Khristu amalimbikitsa uchimo? Ayi. Nʼkosatheka! 18Ngati ine ndimanganso chimene ndinachigumula, ndikuonetsa kuti ndine wophwanya lamulo.

19“Pakuti pamene ndinayesera kutsatira lamulo, lamulolo linandionetsa kuti ndine wochimwa. Choncho ndinasiya kutsatira lamulo kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu. 20Ndinapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano mʼthupi lino, ndi moyo mwachikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu, amene anandikonda nadzipereka yekha chifukwa cha ine. 21Ine sindikukankhira kumbali chisomo cha Mulungu, chifukwa ngati chilungamo chikanapezeka pochita ntchito za lamulo, ndiye kuti Khristu anafa pachabe.”

Swedish Contemporary Bible

Galaterbrevet 2:1-21

Paulus möter församlingsledarna i Jerusalem

1Efter fjorton år kom jag tillbaka till Jerusalem tillsammans med Barnabas. Titus tog jag också med mig. 2Den gången reste jag dit därför att jag hade fått en uppenbarelse. Där presenterade jag i enskildhet inför församlingens ledare det evangelium som jag förkunnar bland hedningarna. Jag ville ju inte ha sprungit, eller fortsätta att springa förgäves. 3De krävde inte ens att min reskamrat Titus, som är grek, skulle omskäras.

4Det skulle ju de falska troende ha velat, som hade lurat sig in bland oss för att spionera på den frihet vi har i Kristus Jesus, för att de skulle kunna göra oss till slavar. 5Men inte ett ögonblick gav vi efter och ställde upp på deras krav, för att evangeliets sanning skulle bevaras hos er.

6De som ansågs vara något – vad de sedan varit bryr jag mig inte om, för i Guds ögon är alla lika – ville alltså inte lägga till något till min undervisning. 7Tvärtom insåg de att jag hade fått i uppdrag att sprida evangeliet till de oomskurna, precis som Petrus till de omskurna. 8Han som hade gett Petrus kraft att vara apostel bland de omskurna, hade ju gett mig kraft att vara det bland hedningarna. 9Så när de som ansågs vara pelare, Jakob, Kefas och Johannes, förstod vilken nåd som hade getts mig, räckte de mig och Barnabas handen som tecken på vårt samarbete. Vi skulle gå ut till hedningarna och de själva till de omskurna. 10Det enda de bad oss om var att vi skulle tänka på de fattiga, och det har jag verkligen försökt göra.

Paulus gick emot Petrus i Antiochia

11Men när Kefas kom till Antiochia gick jag emot honom helt öppet, eftersom han hade dömt sig själv. 12Innan det kom några från Jakob brukade han nämligen äta tillsammans med hedningarna, men när Jakobs följe kom drog han sig undan hedningarna av fruktan för dem som förespråkade omskärelsen. 13De andra judarna deltog i samma hyckleri, och till och med Barnabas drogs med.

14Men när jag såg att de handlade tvärtemot evangeliets sanning, sa jag till Kefas inför alla: ”Du är jude, men lever som hedningarna, inte som judarna. Varför vill du då tvinga hedningarna att leva som judar?2:14 Det är möjligt att Paulus tilltal till Petrus slutar här.

15Vi är födda judar, inte hedniska syndare.2:15 Med syndare menade judarna andra folk som saknade lagen. 16Vi vet att människan inte blir rättfärdig genom laggärningar utan genom tron på Kristus Jesus. Därför började vi själva tro på Kristus Jesus, så att vi skulle bli rättfärdiga genom tron på Kristus och inte genom laggärningar. Ingen kan ju någonsin bli rättfärdig genom laggärningar.

17Om vi som ville bli rättfärdiga genom Kristus visades vara syndare, skulle det betyda att Kristus är tjänare för synden? Naturligtvis inte! 18Om jag bygger upp det jag har rivit ner, då blir jag en överträdare. 19Jag har ju genom lagen dött bort från lagen för att leva för Gud. Jag har korsfästs tillsammans med Kristus. 20Och nu lever inte längre jag, utan Kristus lever i mig. Så länge jag lever här i min kropp, lever jag alltså genom tron på Guds Son, han som har älskat mig och gett sitt liv för mig. 21Jag förkastar inte Guds nåd, för om rättfärdigheten hade kunnat fås genom lagen, då hade ju inte Kristus behövt dö.”