Agalatiya 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 1:1-24

1Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa, 2pamodzi ndi abale onse amene ali nane,

Kulembera mipingo ya ku Galatiya:

3Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu. 4Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. 5Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni.

Uthenga Wabwino ndi Umodzi Wokha

6Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana, 7umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu. 8Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa! 9Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”

10Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.

Paulo Woyitanidwa ndi Mulungu

11Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi. 12Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.

13Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga. 14Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu. 15Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa 16kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense. 17Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.

18Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu. 19Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye. 20Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi. 21Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya. 22Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu. 23Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.” 24Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

Bibelen på hverdagsdansk

Galaterbrevet 1:1-24

Indledende hilsen

1Dette brev er fra Paulus, der er kaldet til at tjene Jesus som apostel. Min kaldelse kommer ikke fra et menneske eller en gruppe mennesker. Den kommer fra Jesus Kristus selv og fra Gud, vores Far, som oprejste ham fra de døde. 2Jeg og alle vennerne, som er sammen med mig her, sender mange hilsener til jer, som tilhører de kristne menigheder i provinsen Galatien. 3Nåde være med jer og fred fra Gud, vores Far, og Herren Jesus Kristus.

4I ved, hvordan Jesus gav sit liv, for at vi kunne få tilgivelse for vores synder og blive sat fri fra de onde tanker og vaner, som hører denne verden til. Han gik i døden for os, fordi det var Guds vilje, han, som er vores Far. 5Han skal have æren i al evighed. Amen.

Galaterne er ved at svigte det sande budskab om Guds nåde

6-7Jeg er chokeret over, at I så hurtigt har vendt jer fra Gud, som kaldte jer til at leve i Kristi nåde. Vi bragte jer det glædelige budskab om Jesus, men I har nu taget imod et andet budskab, som bestemt ikke er glædeligt. Der er nogen, der skaber forvirring iblandt jer ved at fordreje glædesbudskabet fra Kristus. 8Hvis nogen bringer jer et budskab, der går imod det, vi forkyndte for jer, bliver han ramt af Guds dom. Det gælder også, hvis vi selv eller en engel gør det. 9Lad mig sige det en gang til, fordi det er så vigtigt: Guds dom vil ramme enhver, der kommer med et andet budskab end det, I allerede har taget imod!

Paulus’ autoritet som apostel

10I kan godt se, at jeg ikke taler mennesker efter munden. Jeg ønsker kun at gøre Guds vilje og tjene ham. Hvis jeg bare sagde det, folk gerne vil høre, kunne jeg ikke tjene Kristus.

11-12Jeg understreger for jer, kære venner, at det budskab, jeg har forkyndt jer, ikke er noget, som mennesker har fundet på, eller noget, jeg har lært under mine studier. Det er Jesus Kristus selv, der har åbenbaret det for mig.

13I har hørt om, hvordan jeg engang levede som rettroende jøde. Jeg forfulgte de kristne af al magt og forsøgte at udrydde Guds menighed. 14Jeg var helt opslugt af at studere og følge vores jødiske traditioner, og jeg var langt mere fanatisk i min religiøse overbevisning end mine jævnaldrende. 15-16Men Gud besluttede at åbenbare sin Søn for mig, og da blev jeg klar over, at han, allerede før jeg blev født, havde udvalgt mig til at forkynde budskabet om Jesus for mennesker af alle folkeslag. Det gjorde han alene på grund af sin nåde og kærlighed. Da jeg fik den åbenbaring, spurgte jeg ikke straks mennesker til råds, 17og jeg tog ikke til Jerusalem for at blive belært af dem, som allerede var apostle før mig. Nej, jeg begav mig straks ud i den arabiske ødemark og vendte senere tilbage til Damaskus.

18Først tre år efter, at Jesus havde vist sig for mig, tog jeg til Jerusalem for at lære apostlen Peter at kende, og jeg blev hos ham i to uger. 19Jeg så ikke noget til de andre apostle, undtagen Jesu bror, Jakob. 20Gud er mit vidne på, at det, jeg skriver her, er den absolutte sandhed. 21Efter opholdet i Jerusalem tog jeg til Syrien og Kilikien. 22De kristne menigheder i Judæa havde aldrig mødt mig personligt. 23Men de havde gentagne gange hørt, at den mand, som før i tiden forfulgte dem, nu udbredte den selv samme tro, som han før prøvede at udrydde. 24Og de takkede Gud for, hvad der var sket med mig.