Afilipi 4 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 4:1-23

1Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.

2Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye. 3Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.

Malangizo Otsiriza

4Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa! 5Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi. 6Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. 7Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

8Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka. 9Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.

Kuthokoza Chifukwa cha Mphatso

10Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi. 11Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo. 12Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi. 13Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

14Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga. 15Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu. 16Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga. 17Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu. 18Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu. 19Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

20Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Malonje Otsiriza

21Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo. 22Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.

23Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

New International Reader’s Version

Philippians 4:1-23

Remain Strong in the Lord

1My brothers and sisters, in this way remain strong in the Lord. I love you and long for you. Dear friends, you are my joy and my crown.

2Here is what I’m asking Euodia and Syntyche to do. I’m asking them to work together in the Lord. That’s because they both belong to the Lord. 3My true companion, here is what I ask you to do. Help these women, because they have served at my side. They have worked with me to spread the good news. So have Clement and the rest of those who have worked together with me. Their names are all written in the book of life.

Final Commands

4Always be joyful because you belong to the Lord. I will say it again. Be joyful! 5Let everyone know how gentle you are. The Lord is coming soon. 6Don’t worry about anything. No matter what happens, tell God about everything. Ask and pray, and give thanks to him. 7Then God’s peace will watch over your hearts and your minds. He will do this because you belong to Christ Jesus. God’s peace can never be completely understood.

8Finally, my brothers and sisters, always think about what is true. Think about what is noble, right and pure. Think about what is lovely and worthy of respect. If anything is excellent or worthy of praise, think about those kinds of things. 9Do what you have learned or received or heard from me. Follow my example. The God who gives peace will be with you.

Paul Gives Thanks for the Philippians’ Gifts

10At last you are concerned about me again. That makes me very happy. We belong to the Lord. I know that you were concerned. But you had no chance to show it. 11I’m not saying this because I need anything. I have learned to be content no matter what happens to me. 12I know what it’s like not to have what I need. I also know what it’s like to have more than I need. I have learned the secret of being content no matter what happens. I am content whether I am well fed or hungry. I am content whether I have more than enough or not enough. 13I can do all this by the power of Christ. He gives me strength.

14But it was good of you to share in my troubles. 15And you believers at Philippi know what happened when I left Macedonia. Not one church helped me in the matter of giving and receiving. You were the only one that did. That was in the early days when you first heard the good news. 16Even when I was in Thessalonica, you sent me help when I needed it. And you did it more than once. 17It is not that I want your gifts. What I really want is what is best for you. 18I have received my full pay and have more than enough. I have everything I need. That’s because Epaphroditus brought me the gifts you sent. They are a sweet-smelling offering. They are a gift that God accepts. He is pleased with it. 19My God will meet all your needs. He will meet them in keeping with his wonderful riches. These riches come to you because you belong to Christ Jesus.

20Give glory to our God and Father for ever and ever. Amen.

Final Greetings

21Greet all God’s people. They belong to Christ Jesus.

The brothers and sisters who are with me send greetings.

22All God’s people here send you greetings. Most of all, those who live in the palace of Caesar send you greetings.

23May the grace of the Lord Jesus Christ be with your spirit. Amen.