Afilipi 3 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 3:1-21

Osakhulupirira za Thupi

1Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.

2Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. 3Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi 4ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.

Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. 5Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. 6Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.

7Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. 8Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu 9ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.

Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro

12Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.

Kutsanzira Paulo

15Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

17Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.

Slovo na cestu

Filipským 3:1-21

Co má před Bohem cenu

1A tak ať se děje cokoliv, bratři, radujte se z toho, že patříte Bohu. Musím to opakovat znovu a znovu, protože v té radosti je vaše síla. 2A nedejte se zmást těmi svůdci, kteří jako psi pořád štěkají, že jste povinni řídit se starými tradicemi, jako je například židovská obřízka, a tvrdí, že jen podle toho se pozná, kdo patří Bohu. 3Poznávacím znamením Božího dítěte je sloužit Bohu a nechat se jím vést. My jsme Boží děti. Celý svůj život stavíme na Kristu a nespoléháme se na vnější znaky židovství.

4Kdyby oni měli pravdu, pak bych největší výsady u Boha musel mít já. Vždyť jsem narozen z čistokrevných židovských rodičů, jejichž rodokmen sahá až k Benjamínovi, 5obřezán jsem byl týden po narození. Může mít někdo židovštější původ? Navíc jsem byl jako farizej vychováván k nejpřísnějšímu dodržování zákona a tradic 6a sotva kdo byl v pronásledování křesťanů horlivější než já. Ze strany židovského náboženství mi nikdo nemohl nic vytknout. 7Ale to všechno, na čem jsem si kdysi zakládal, ztratilo pro mne jakoukoliv cenu, když jsem poznal Krista. 8Ve skutečnosti to všechno pokládám za nevýhodu, srovnám-li to s tím úžasným poznáním, že Ježíš Kristus je můj Pán.

Kvůli němu jsem to všechno zahodil jako odpadky, 9jen abych získal Krista a v něm zakotvil. Už se nestarám jako dříve, dokud jsem byl židem, jak si Boha naklonit zachováváním zákonů a nařízení, protože vím, že Bůh ode mne nevyžaduje nic jiného než víru v Krista. Věřit ovšem znamená: 10poznat Krista a moc jeho zmrtvýchvstání a podílet se na jeho utrpení. A tak chci i já podstoupit jeho smrt 11a dosáhnout tím i zmrtvýchvstání.

Jak dosáhnout cíle

12Nemyslím si, že bych toho všeho už dosáhl; to jistě ne. Snažím se však ze všech sil, abych to získal, když mne již získal Kristus. 13Bratři, opravdu si nenamlouvám, že bych již byl u cíle, ale o jedno mi jde: nechávám všechno za sebou a upírám se jen k tomu, co je přede mnou. 14Mířím přímo k cíli, kde mne čeká věnec vítězů – nový život, ke kterému mne Bůh prostřednictvím Ježíše Krista povolal.

15Doufám, že všichni, kdo jste už ve víře dorostli k dospělosti, díváte se na ty věci stejně jako já. Pokud byste měli ještě nějaké pochybnosti, Bůh vám i v tom dá časem jasno. 16Hlavně se pevně držte alespoň té pravdy, kterou už znáte. 17A tak, bratři, dělejte to jako já a řiďte se příkladem všech, kdo tak žijí.

I křesťan může prohrát věčnost

18Už jsem vám přece víckrát říkal – a dnes se mi chce přímo plakat při tom pomyšlení –, kolik je mezi námi lidí, kteří jsou ve skutečnosti Kristovými nepřáteli. Zbožňují jen svůj vlastní žaludek, chlubí se tím, zač by se měli stydět, a myslí jen na to, jak se mít na světě dobře. 19Ti svou věčnost prohráli. 20Naše pravá vlast je tam, kde je Ježíš Kristus, a my se těšíme, že se k nám odtud vrátí, 21aby naše slabá a smrtelná těla proměnil a dal jim stejnou podstatu, jakou mělo jeho tělo po vzkříšení. On je schopen to učinit, protože je Pánem vesmíru.