Aefeso 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 6:1-24

Ana ndi Makolo Awo

1Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera. 2“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo. 3Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.” 4Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.

Antchito ndi Mabwana Awo

5Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu. 6Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu. 7Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu. 8Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.

9Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.

Zida Zankhondo za Mulungu

10Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu. 11Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana. 12Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. 13Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu. 14Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa. 15Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato. 16Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo. 17Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu. 18Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.

19Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha. 20Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.

Mawu Otsiriza

21Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita. 22Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.

23Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse. 24Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

New International Reader’s Version

Ephesians 6:1-24

1Children, obey your parents as believers in the Lord. Obey them because it’s the right thing to do. 2Scripture says, “Honor your father and mother.” That is the first commandment that has a promise. 3“Then things will go well with you. You will live a long time on the earth.” (Deuteronomy 5:16)

4Fathers, don’t make your children angry. Instead, instruct them and teach them the ways of the Lord as you raise them.

5Slaves, obey your masters here on earth. Respect them and honor them with a heart that is true. Obey them just as you would obey Christ. 6Don’t obey them only to please them when they are watching. Do it because you are slaves of Christ. Be sure your heart does what God wants. 7Serve your masters with all your heart. Work as serving the Lord and not as serving people. 8You know that the Lord will give each person a reward. He will give it to them in keeping with the good they do. It doesn’t matter whether they are a slave or not.

9Masters, treat your slaves in the same way. When you warn them, don’t be too hard on them. You know that the God who is their Master and yours is in heaven. And he treats everyone the same.

God’s Armor for Believers

10Finally, let the Lord make you strong. Depend on his mighty power. 11Put on all of God’s armor. Then you can remain strong against the devil’s evil plans. 12Our fight is not against human beings. It is against the rulers, the authorities and the powers of this dark world. It is against the spiritual forces of evil in the heavenly world. 13So put on all of God’s armor. Evil days will come. But you will be able to stand up to anything. And after you have done everything you can, you will still be standing. 14So remain strong in the faith. Put the belt of truth around your waist. Put the armor of godliness on your chest. 15Wear on your feet what will prepare you to tell the good news of peace. 16Also, pick up the shield of faith. With it you can put out all the flaming arrows of the evil one. 17Put on the helmet of salvation. And take the sword of the Holy Spirit. The sword is God’s word.

18At all times, pray by the power of the Spirit. Pray all kinds of prayers. Be watchful, so that you can pray. Always keep on praying for all the Lord’s people. 19Pray also for me. Pray that whenever I speak, the right words will be given to me. Then I can be bold as I tell the mystery of the good news. 20Because of the good news, I am being held by chains as the Lord’s messenger. So pray that I will be bold as I preach the good news. That’s what I should do.

Final Greetings

21Tychicus is a dear brother. He is faithful in serving the Lord. He will tell you everything about me. Then you will know how I am and what I am doing. 22That’s why I am sending him to you. I want you to know how we are. And I want him to encourage you.

23May God the Father and the Lord Jesus Christ give peace to the brothers and sisters. May they also give the believers love and faith.

24May grace be given to everyone who loves our Lord Jesus Christ with a love that will never die.