3 Yohane 1 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Yohane 1:1-15

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.

2Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu. 3Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi. 4Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.

5Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo. 6Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu. 7Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira. 8Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.

Za Diotrefe ndi Demetriyo

9Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera. 10Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.

11Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu. 12Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.

13Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. 14Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso.

15Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

Slovo na cestu

3. Janův 1:1-15

Boží děti žijí podle zásad evangelia

1-2Jan drahému Gájovi.

Milovaný příteli, ujišťuji tě o své lásce a modlím se za tebe, aby ses měl tak dobře na těle, jako se máš na duchu. 3Měl jsem velikou radost z vyprávění některých bratří, kteří se u mne zastavili a pověděli mi, že svým životem věrně následuješ pravdu. 4Nic mne nepotěší jako zpráva, že mé děti se drží Kristovy pravdy.

5Milovaný příteli, konáš opravdu záslužnou a dobrou práci, že se staráš o kazatele, kteří navštěvují váš sbor. 6Všude o tvé lásce vyprávějí. Dobře děláš, že jim umožňuješ další práci, jak si Bůh přeje. 7Pracují přece pro Krista, a proto nepřijímají podporu od nevěřících. 8Pro takové lidi máme mít otevřené dveře a tak napomáhat šíření pravdy.

9Napsal jsem vašemu sboru dopis, ale Diotrefés, který chce mít mezi vámi vždycky první i poslední slovo, neuznává naši autoritu. 10Až k vám přijdu, povolám ho k odpovědnosti za to, že nás ošklivě pomlouvá, nepřijímá naše posly a dokonce brání těm, kdo se jich ujímají, a vylučuje je ze sboru.

11Drahý příteli, drž se ne zlého, ale dobrého příkladu. Kdo jedná podle Boží vůle, je jeho dítě. Kdo jedná svévolně, Boha nezná. 12Demétria si váží a staví se za něj sám Bůh. I my za něho ručíme a vy víte, že naše svědectví je spolehlivé.

Janova závěrečná slova

13Rád bych napsal ještě více, ale je to zbytečné, 14protože doufám, že se brzo uvidíme a důkladně si o všem pohovoříme.

15Měj se dobře. Pozdravují tě přátelé a také ty pozdravuj každého z bratří.