2 Yohane 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Yohane 1:1-13

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. 2Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

3Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

4Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. 5Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. 6Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

7Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu. 8Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse. 9Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana. 10Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni. 11Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.

12Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.

13Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרתו השנייה של יוחנן השליח 1:1-13

1לכבוד המאמינה המשיחית, הגברת הבחירה, וילדיה האהובים עלי ועל כל הקהילה.

מאת יוחנן – הזקן בזקני הקהילה.

2‏-3אדוננו ואלוהינו יברך את כולנו בשלום, ברחמים ובאהבה, בזכות האמת החקוקה בלבנו לנצח.

4שמחתי מאוד לפגוש כאן אחדים מילדיך, ולהיווכח שהם מתנהגים כראוי, אוהבים את האמת ושומרים את מצוות ה׳.

5גברתי הנכבדה, ברצוני להזכיר לך את אחת המצוות הראשונות שציווה עלינו ה׳: לאהוב איש את רעהו. 6מי שבאמת אוהב את ה׳ עושה כל מה שה׳ מצווה עליו, והוא הרי ציווה עלינו מבראשית לאהוב איש את רעהו.

7היזהרו ממורי השקר שמסתובבים בכל מקום. אין הם מאמינים שישוע המשיח בא לעולם כבן־אדם בשר ודם. אנשים אלה הם אויבי האמת ושונאי המשיח. 8היזהרו לבל ישפיעו עליכם, פן תפסידו את הפרס שאתם ואני משתדלים מאוד להשיג. עשו הכול כדי לקבל את שכרכם המלא מהאדון. 9מי שמנסה להתחכם ולעבור על תורת המשיח – אין האלוהים איתו, ואילו אדם שנשאר נאמן לתורת המשיח – גם האלוהים וגם המשיח איתו.

10‏-11אם ירצה מישהו ללמד אתכם תורה ששונה מתורת המשיח, אל תזמינוהו לביתכם ואף אל תדברו איתו! שהרי כל מי שמעודד אותו נעשה שותף למעשיו הרעים.

12יש לי עוד הרבה לומר, אך לא אעלה זאת על הנייר, שכן אני מקווה לפגוש אתכם בקרוב פנים אל פנים, ואז נוכל לשוחח ולשמוח יחד.

13ילדי אחותך המאמינה מוסרים לך דרישת שלום חמה.