2 Timoteyo 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

2 Timotheo 1:1-18

11:1 1Tim 6:19; Tit 1:2; 1Kor 1:1; Efe 3:6; Ebr 9:15Paulo mtume wa Kristo Yesu kwa mapenzi ya Mungu, kulingana na ile ahadi ya uzima uliomo ndani ya Kristo Yesu.

21:2 Mdo 16:1; 1Tim 1:2Kwa Timotheo, mwanangu mpendwa:

Neema, rehema na amani itokayo kwa Mungu Baba, na kwa Kristo Yesu Bwana wetu.

Shukrani Na Kutiwa Moyo

31:3 Rum 1:10; Efe 1:16; Mdo 22:3; 23:1; 24:14; 27:23; Gal 1:14Ninamshukuru Mungu, ninayemtumikia kwa dhamiri safi, kama walivyofanya baba zangu, ninapokukumbuka usiku na mchana katika maombi yangu. 41:4 Mdo 20:37; 2Tim 4:9; 4:21Nikiyakumbuka machozi yako, ninatamani sana kukuona ili nipate kujawa na furaha. 51:5 1Tim 1:5; 2Tim 3:15Nimekuwa nikiikumbuka imani yako ya kweli, waliokuwa nayo bibi yako Loisi na mama yako Eunike na ambayo mimi ninasadiki sasa wewe pia unayo. 61:6 Mdo 6:6; 1The 5:19; 1Tim 4:14Kwa sababu hii nakukumbusha uchochee ile karama ya Mungu, iliyowekwa ndani yako nilipokuwekea mikono yangu. 71:7 Yer 42:11; Rum 8:15; Lk 24:49; Mdo 1:8Maana Mungu hakutupa roho ya woga, bali roho ya nguvu, ya upendo na ya moyo wa kiasi.

81:8 Rum 1:16; Efe 3:1; 2Tim 2:3-9; 4:5Kwa hiyo usione haya kushuhudia kuhusu Bwana wetu, wala usinionee haya mimi niliye mfungwa kwa ajili yake. Bali uishiriki pamoja nami taabu ya Injili, kwa kadiri ya nguvu ya Mungu, 91:9 Rum 8:28; 1Tim 1:1; Tit 3:4; 1The 4:7; Ebr 3:1; Rum 3:20; 9:11; Tit 3:5ambaye alituokoa na kutuita katika mwito mtakatifu: si kwa kadiri ya matendo yetu mema bali kwa sababu ya kusudi lake mwenyewe na neema yake. Neema hii tulipewa katika Kristo Yesu tangu milele. 101:10 Efe 1:9; 1Kor 15:26, 54; Rum 16:26; Kol 1:26; Tit 1:3; 1Pet 1:20; Ebr 2:14Lakini sasa imefunuliwa kwa kudhihirishwa kwake Mwokozi wetu, Kristo Yesu, ambaye amebatilisha mauti na kuleta uzima na kutokufa kwa njia ya Injili. 111:11 1Tim 2:7; Mdo 9:15; Efe 3:7, 8; 2Tim 4:17Nami nimewekwa kuwa mhubiri, mtume na mwalimu wa Injili hii. 121:12 1Tim 6:20; 1Kor 1:8; Efe 3:1; 2Tim 2:9; 1Pet 4:19; 1Tim 6:20; 2Tim 4:8Hii ndiyo sababu ninateseka namna hii, lakini sioni haya kwa maana ninamjua yeye niliyemwamini, na kusadiki ya kuwa anaweza kukilinda kile nilichokiweka amana kwake hadi siku ile.

131:13 Tit 1:9; 1Tim 1:14Shika kwa uthabiti kielelezo cha mafundisho yenye uzima yale uliyoyasikia kwangu, pamoja na imani na upendo katika Kristo Yesu. 141:14 Rum 8:9; 1Tim 6:20; Rum 8:11Ilinde ile amana uliyokabidhiwa kwa Roho Mtakatifu akaaye ndani yetu.

151:15 2Tim 4:10-16, 19; Mdo 19:10Unajua ya kuwa watu wote katika Asia wameniacha, miongoni mwao wamo Filego na Hermogene.

161:16 Mt 5:7; 2Tim 4:19; Flm 7; Mdo 28:20Bwana akawahurumie watu wa nyumbani mwa Onesiforo, kwa sababu aliniburudisha mara kwa mara wala hakuionea aibu minyororo yangu. 17Badala yake, alipokuwa Rumi, alinitafuta kwa bidii mpaka akanipata. 181:18 Ebr 6:10; Mt 25:34-40; 2The 1:10; 1Tim 1:18Bwana na amjalie kupata rehema zake siku ile! Nawe unajua vyema jinsi alivyonisaidia huko Efeso.