2 Samueli 23 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 23:1-39

Mawu Otsiriza a Davide

1Nawa mawu otsiriza a Davide:

“Mawu a Davide mwana wa Yese,

mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba,

munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo,

woyimba nyimbo za Israeli:

2“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine;

mawu ake anali pakamwa panga.

3Mulungu wa Israeli anayankhula,

Thanthwe la Israeli linati kwa ine:

‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo,

pamene alamulira moopa Mulungu,

4amakhala ngati kuwala kwa mmamawa,

mmawa wopanda mitambo,

monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa

imene imameretsa udzu mʼnthaka.’

5“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu?

Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine,

lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse?

Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa,

ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?

6Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga,

imene sitengedwa ndi manja.

7Aliyense amene wayikhudza mingayo

amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo;

nayitentha pa moto.”

Ankhondo Otchuka a Davide

8Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide:

Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.

9Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo. 10Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.

11Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo. 12Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.

13Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu. 14Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu. 15Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!” 16Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova. 17Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo.

Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.

18Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja. 19Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.

20Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango. 21Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe. 22Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja. 23Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.

24Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa:

Asaheli mʼbale wa Yowabu,

Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

25Sama Mharodi,

Elika Mherodi,

26Helezi Mpaliti,

Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,

27Abiezeri wa ku Anatoti,

Sibekai Mhusati,

28Zalimoni Mwahohi,

Maharai Mnetofa,

29Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,

30Benaya Mpiratoni,

Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.

31Abi-Aliboni Mwaribati,

Azimaveti Mbarihumi,

32Eliyahiba Msaaliboni,

ana a Yaseni,

Yonatani, 33mwana wa Sama Mharari,

Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,

34Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati,

Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,

35Heziro wa ku Karimeli,

Paarai Mwaribi,

36Igala mwana wa Natani wa ku Zoba,

mwana wa Hagiri,

37Zeleki Mwamoni,

Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,

38Ira Mwitiri,

Garebu Mwitiri,

39ndi Uriya Mhiti.

Onse pamodzi analipo 37.

Japanese Contemporary Bible

サムエル記Ⅱ 23:1-39

23

ダビデの最後のことば

1これは、ダビデの最後のことばです。

「エッサイの子ダビデは告げる。

ダビデ、神からすばらしい勝利と祝福を授けられた者。

ダビデ、ヤコブの神から油を注がれた(特別に選ばれた)者。

ダビデ、イスラエルの麗しい詩人。

2主の霊は私を通して語られた。

主のことばは私の舌にあった。

3イスラエルの岩である方が私に語られた。

『正しく治める者、神を恐れて治める者が来る。

4その人は、朝の光のよう、雲一つない朝焼けのようだ。

地に萌え出た若草に降り注ぐ

雨上がりの陽光のようだ。』

5まことに、神がわが家系をお選びくださった。

神は永遠の契約を、私と結んでくださった。

その約束は揺るがず、最後まで守られる。

神は常に、私の安全と成功を心にかけてくださる。

6しかし、神に背を向ける者は、

いばらのように投げ捨てられる。

7彼らは武装した者に切り捨てられ、

火で焼かれる。」

ダビデ軍の勇士たち

8ダビデ軍の中で最強の英雄三人の名を挙げるなら、筆頭はハクモニの子ヤショブアムで、一度の戦いで八百人を倒した勇士です。

9次は、ドドの子でアホアハ人のエルアザルです。彼も三勇士の一人で、ほかの者が逃げ出した時も、ダビデとともに踏みとどまってペリシテ人と戦いました。 10彼は次々にペリシテ人を打ち倒し、ついに手が疲れて、剣を握ることもできないほどでした。主は彼に輝かしい勝利を授けました。残りの兵士が引き返して来た時には、戦利品を集めるばかりになっていたのです。

11-12三人目は、ハラル出身のアゲの子シャマです。ペリシテ人が攻めて来た時、部下は彼を放って逃げ出しましたが、ただ一人レンズ豆畑の真ん中に踏みとどまって、敵を打ち倒したのです。こうして、主は大勝利をもたらしました。

13ダビデがアドラムのほら穴に潜み、攻め寄せるペリシテ人がレファイムの谷に陣取っていた時のことです。ちょうど刈り入れのころ、イスラエル軍の精鋭三十人の中から、この三人がダビデのもとを訪ねて来ました。 14当時、ダビデは要害に立てこもっていました。ペリシテ人の略奪隊がベツレヘム一帯を占領していたからです。 15そんなダビデの口をついて出るのは、いつも、「ああ、のどが渇いた。ベツレヘムの井戸のうまい水が飲みたい」ということばでした。その井戸は町の門のわきにありました。 16そこで三人の勇士は、ペリシテ人の陣営を突き破って井戸へ行き、くんで来た水をダビデに差し出しました。しかしダビデは、とてもその水を飲む気にはなれず、主にささげて注いだのです。 17ダビデは言いました。「主よ。どうしてこの水を飲めましょう。いのちをかけた人々の血ですから。」

18-19この三人のほかに、ツェルヤの子ヨアブの兄弟アビシャイも、非常に評判の高い人物でした。単身、三百人の敵を相手にして倒したこともありました。その武勲により、三勇士に負けないほどの名声を上げました。彼はイスラエル軍の幹部将校三十人の中では最もすぐれ、彼らのリーダーでした。

20このほか、エホヤダの子でベナヤというカブツェエル出身の勇士もいました。ベナヤは、モアブの豪傑二人を倒しました。ある時は、つるつるに凍った雪道にもかかわらず、ほら穴に下りて行き、中にいたライオンを殺しました。 21またある時は、杖一本で、槍を手にしたエジプト人戦士に立ち向かって倒しました。相手の手から槍をもぎ取って突き殺したのです。 22これらの手柄で、ベナヤは三勇士のように有名になりました。 23彼は、あの三勇士には及びませんでしたが、三十人の中で非常に評判の高い一人でした。ダビデは彼を護衛長に任じました。

24-39ヨアブの兄弟アサエルも、三十人の一人でした。そのほかの顔ぶれは次のとおりです。ベツレヘム出身で、ドドの子エルハナン。ハロデ出身のシャマ。ハロデ出身のエリカ。ペレテ出身のヘレツ。テコア出身で、イケシュの子イラ。アナトテ出身のアビエゼル。フシャ出身のメブナイ。アホアハ出身のツァルモン。ネトファ出身のマフライ。ネトファ出身で、バアナの子ヘレブ。ギブア出身で、ベニヤミン部族リバイの子イタイ。ピルアトン出身のベナヤ。ガアシュの谷出身のヒダイ。アラバ出身のアビ・アルボン。バルフム出身のアズマベテ。シャアルビム出身のエルヤフバ。ヤシェンの子たち。ヨナタン。ハラル出身のシャマ。アラル出身で、シャラルの子アヒアム。マアカ出身で、アハスバイの子エリフェレテ。ギロ出身で、アヒトフェルの子エリアム。カルメル出身のヘツライ。アラブ出身のパアライ。ツォバ出身で、ナタンの子イグアル。ガド出身のバニ。アモン出身のツェレク。ツェルヤの子ヨアブのよろい持ちで、ベエロテ出身のナフライ。エテル出身のイラ。エテル出身のガレブ。ヘテ人ウリヤ。以上合わせて三十七人です。