2 Samueli 22 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 22:1-51

Nyimbo ya Mayamiko ya Davide

1Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. 2Iye anati,

“Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.

3Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo,

chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa.

Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga.

Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

4“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

5“Mafunde a imfa anandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

6Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

7“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinapemphera kwa Mulungu wanga.

Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.

8“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

maziko a miyamba anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

9Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

10Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

11Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

12Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

mitambo yakuda ya mlengalenga.

13Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake

munkachokera makala amoto alawilawi.

14Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

15Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

16Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera,

ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.

17“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

18Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.

19Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

20Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

21“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

22Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.

23Malamulo ake onse ali pamaso panga,

sindinasiye malangizo ake.

24Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

25Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.

26“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu,

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

27Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

28Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.

29Inu Yehova, ndinu nyale yanga;

Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

30Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo,

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

31“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa iye.

32Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

33Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

34Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

35Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

36Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso;

mumawerama kuti mundikweze.

37Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino,

kuti mapazi anga asaterereke.

38“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha;

sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.

39Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso;

Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.

40Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo;

munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.

41Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa;

ndipo ndinawononga adani anga.

42Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.

43Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi;

ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

44“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu;

Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

45Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine, amandigonjera.

46Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

47“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa.

Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!

48Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,

49amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

50Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

51“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake,

amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

Het Boek

2 Samuël 22:1-51

Het lied van David

1Nadat de Here David had gered van Saul en al zijn andere vijanden, zong hij het volgende lied voor de Here:

2‘De Here is mijn Rots, mijn Burcht en mijn Redder.

3Ik wil schuilen bij God, want Hij is mijn Rots en toevluchtsoord. Hij is mijn schild en mijn heil, mijn toevluchtsoord en hoge toren.

O mijn Redder, dat U mij redde van al mijn vijanden.

4Ik zal de Here loven, want Hij is het waard geprezen te worden, Hij zal mij redden van al mijn vijanden.

5De golven van de dood omspoelden mij, stormvloeden van kwaad stortten zich op mij.

6Ik zat in de val, onwrikbaar vastgebonden door hel en dood.

7Maar in mijn angst riep ik de Here en vanuit zijn tempel hoorde Hij mij. Mijn hulpgeroep bereikte Hem.

8Toen schokte en trilde de aarde, de fundamenten van de hemel beefden door zijn toorn.

9Er kwam rook uit zijn neus en vuurtongen schoten uit zijn mond. Zij verteerden allen die voor Hem stonden en zetten de wereld in vuur en vlam.

10Hij liet de hemel neerbuigen en kwam naar de aarde, lopend over donkere wolken.

11Hij reed op een engel en vloog, Hij zweefde op de vleugels van de wind.

12Duisternis omringde Hem, overal om Hem heen waren zware wolken

13en de aarde gloeide op door zijn glans.

14De Here liet het vanuit de hemel donderen, God, de Allerhoogste, sprak met zijn machtige stem.

15Hij schoot zijn bliksempijlen weg en maakte zijn vijanden angstig.

16Door zijn vreselijke adem en zijn bestraffende woord spleet de zee open en kwam de zeebodem bloot.

17Hij redde mij van bovenaf en trok mij op uit het water.

18Hij redde mij van sterke vijanden, van hen die mij haatten en van hen die sterker waren dan ik.

19Zij stortten zich op mij tijdens de dag van mijn ongeluk. Maar de Here was mijn heil.

20Hij bevrijdde en redde mij, want ik was goed in zijn ogen.

21De Here beloonde mij voor mijn goedheid, want mijn handen waren onbevuild.

22Ik heb de geboden van mijn God niet overtreden en ben van zijn weg niet afgeweken.

23Ik kende zijn wetten en gehoorzaamde deze.

24Ik was volgzaam tot en met en zorgde ervoor dat ik geen onrecht deed.

25Daarom heeft de Here zoveel voor mij gedaan, want Hij ziet dat ik vlekkeloos ben.

26U bent goed voor de goeden, U toont Zich onberispelijk tegenover de onberispelijken.

27U toont Zich rein tegenover de reinen en sluw tegenover de leugenaars.

28Wie het moeilijk hebben, redt U, maar U vernedert de hoogmoedigen, want U ziet alles wat zij doen.

29O Here, U bent mijn licht! U verlicht mijn duisternis.

30Door uw kracht kan ik een heel leger verslaan en spring ik over een hoge muur.

31Gods weg is volmaakt, het woord van de Here is waar. Hij beschermt allen die zich aan Hem toevertrouwen.

32Alleen onze Here is God, wie is een Rots buiten onze Here.

33God is mijn sterke Burcht, Hij heeft mij in veiligheid gebracht.

34Hij zorgt dat de goeden veilig kunnen lopen, als klipgeiten over de rotsen.

35Hij maakt mij bekwaam voor de strijd en geeft mij kracht om een koperen boog te spannen.

36U hebt mij het schild van uw heil gegeven. Door mij te verhoren, hebt U mij grootgemaakt.

37U hebt een pad voor mij gereedgemaakt, zodat ik niet kon uitglijden.

38Ik heb mijn vijanden achtervolgd en hen verslagen. Ik hield pas op toen zij allemaal waren verdwenen.

39Ik heb hen vernietigd, zodat er niet één meer kan opstaan. Zij zijn onder mijn voet ten val gekomen.

40Want U hebt mij kracht gegeven in de strijd en ervoor gezorgd dat ik iedereen die tegen mij opstond, kon onderwerpen.

41U liet mijn vijanden op de vlucht slaan en wegrennen. Ik heb hen allemaal verslagen.

42Zij zochten zonder resultaat naar hulp. Zij riepen tot God, maar Hij weigerde te antwoorden.

43Ik vermaalde hen tot stof, sloeg hen uiteen en doodde hen, ruimde hen op als waardeloos vuil in de straat.

44U hielp mij te ontkomen aan de opstandigheid van mijn volk. U liet mij voortbestaan zelfs aan het hoofd van heidense volken. Buitenlanders zullen mij dienen

45en zich snel aan mij onderwerpen als zij horen van mijn macht.

46Zij zullen de moed laten zakken en bevend bij mij komen vanuit hun schuilplaatsen.

47De Here leeft, gezegend zij mijn Rots. Geprezen zij Hij, de Rots van mijn heil.

48Gezegend zij God, die mijn tegenstanders verslaat

49en mij van mijn vijanden redt. Ja, U houdt mij veilig vast, zodat ik boven hen word verhoogd, U beschermt mij tegen het geweld.

50Daarom loof ik uw naam, o Here, onder de volken en zing tot uw eer.

51Hij redt zijn koning keer op keer op een wonderbaarlijke manier en is genadig voor de gezalfde, voor David en zijn familie, voor nu en altijd.’