2 Samueli 16 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 16:1-23

Davide ndi Ziba

1Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.

2Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?”

Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”

3Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?”

Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’ ”

4Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.”

Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”

Simei Atukwana Davide

5Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera. 6Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake. 7Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe! 8Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”

9Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”

10Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’ ”

11Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero. 12Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”

13Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi. 14Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.

Malangizo a Husai ndi Ahitofele

15Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye. 16Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”

17Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”

18Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse. 19Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”

20Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”

21Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.” 22Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.

23Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

Thai New Contemporary Bible

2ซามูเอล 16:1-23

ดาวิดและศิบา

1ดาวิดเพิ่งจะเสด็จผ่านยอดเขาก็ทรงพบศิบาหัวหน้าคนรับใช้ของเมฟีโบเชทมาคอยเฝ้า เขานำลาคู่หนึ่งผูกอานพร้อมบรรทุกขนมปังสองร้อยก้อน ขนมลูกเกดหนึ่งร้อยก้อน มะเดื่ออัดหนึ่งร้อยก้อน และเหล้าองุ่นหนึ่งถุงหนังมาด้วย

2ดาวิดตรัสถามเขาว่า “เอาของพวกนี้มาทำไม?”

ศิบาทูลว่า “ลานี้สำหรับให้คนในครัวเรือนของฝ่าพระบาทขี่ไป ขนมปังและผลไม้ไว้ให้คนของฝ่าพระบาทรับประทาน ส่วนเหล้าองุ่นไว้สำหรับฟื้นกำลังคนที่อ่อนระโหยในถิ่นกันดาร”

3กษัตริย์ตรัสถามว่า “หลานของนายเจ้าอยู่ที่ไหน?”

ศิบากราบทูลว่า “พักอยู่ที่กรุงเยรูซาเล็มพระเจ้าข้า เพราะเขาคิดว่า ‘ในวันนี้วงศ์วานอิสราเอลจะคืนอาณาจักรของเสด็จปู่ซาอูลให้แล้ว’ ”

4ดาวิดจึงตรัสกับศิบาว่า “บัดนี้ทุกอย่างในกรรมสิทธิ์ของเมฟีโบเชทเป็นของเจ้าแล้ว”

ศิบากราบทูลว่า “ขอถวายบังคม ขอให้ข้าพระบาทเป็นที่โปรดปรานในสายพระเนตรของฝ่าพระบาท”

ชิเมอีสาปแช่งดาวิด

5ขณะที่ดาวิดเสด็จใกล้จะถึงบาฮูริม ชายคนหนึ่งออกมาแช่งด่าดาวิด เขาคือชิเมอีบุตรเกรา เป็นคนหนึ่งในตระกูลของซาอูล 6เขาเอาก้อนหินขว้างดาวิดกับเหล่าข้าราชบริพาร ทั้งๆ ที่กองทหารและราชองครักษ์ขนาบข้างดาวิดทั้งซ้ายขวา 7ชิเมอีแช่งด่าว่า “ไปให้พ้นนะเจ้าฆาตกร เจ้าคนถ่อย! 8องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงคืนสนองสำหรับเลือดทุกหยดที่เจ้าทำให้หลั่งรินในราชวงศ์ซาอูลซึ่งเจ้าครองราชย์แทน องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงยกอาณาจักรให้อับซาโลมลูกของเจ้า ที่เจ้าต้องย่อยยับก็เพราะเจ้าเป็นคนกระหายเลือด!”

9อาบีชัยบุตรนางเศรุยาห์ทูลกษัตริย์ดาวิดว่า “ควรหรือที่สุนัขตายตัวนี้จะมาแช่งด่าฝ่าพระบาท ให้ข้าพระบาทออกไปตัดหัวมันเถิด”

10กษัตริย์ตรัสห้ามว่า “บุตรนางเศรุยาห์เอ๋ย เจ้าเกี่ยวข้องอะไรกับเรื่องนี้ ถ้าองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับเขาว่า ‘จงแช่งด่าดาวิด’ ใครเล่าจะไปถามว่า ‘ทำไมเจ้าจึงทำอย่างนี้?’ ”

11ดาวิดตรัสกับอาบีชัย และเหล่าข้าราชบริพารว่า “แม้แต่ลูกในไส้ของเราเองยังพยายามจะเอาชีวิตของเรา แล้วคนเบนยามินคนนี้จะไม่ยิ่งอยากเอาชีวิตของเราหรือ ปล่อยเขาไปเถิด ให้เขาแช่งด่าไป เพราะองค์พระผู้เป็นเจ้าคงใช้เขามา 12บางทีองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทอดพระเนตรเห็นความทุกข์ลำเค็ญของเรา และทรงอวยพรเราเพราะคำแช่งด่าที่เราได้รับในวันนี้”

13ดาวิดกับพวกจึงเดินทางต่อไปในขณะที่ชิเมอีเดินไปตามแนวเขาฝั่งตรงข้ามและแช่งด่าไป เอาก้อนหินขว้างปาและซัดฝุ่นธุลีเข้าใส่ดาวิดด้วย 14ทั้งกษัตริย์และข้าราชบริพารที่ตามเสด็จต่างก็อ่อนระโหยเมื่อมาถึงที่หมาย และหยุดพักอยู่ที่นั่น

คำแนะนำของหุชัยและอาหิโธเฟล

15ขณะเดียวกันอับซาโลมและชาวอิสราเอลทั้งปวงมาถึงกรุงเยรูซาเล็มพร้อมด้วยอาหิโธเฟล 16เมื่อหุชัยชาวอารคีสหายของดาวิดมาถึงก็เข้าเฝ้าอับซาโลมและทูลว่า “ขอกษัตริย์จงทรงพระเจริญ! ขอจงทรงพระเจริญ!”

17อับซาโลมถามหุชัยว่า “นี่หรือความรักที่ท่านมีให้เพื่อน? ทำไมท่านไม่ตามเพื่อนของท่านไป?”

18หุชัยทูลว่า “ข้าพระบาทจะอยู่ทำงานให้แต่กับคนที่องค์พระผู้เป็นเจ้ากับผู้นำเหล่านี้และชนอิสราเอลทั้งปวงได้เลือกไว้ 19ยิ่งกว่านั้นไม่ควรหรือที่ข้าพระบาทจะรับใช้พระราชโอรส? ข้าพระบาทเคยรับใช้ราชบิดามาแล้วอย่างไร บัดนี้ขอรับใช้ฝ่าพระบาทอย่างนั้น”

20อับซาโลมกล่าวกับอาหิโธเฟลว่า “ช่วยแนะนำว่าเราควรทำอย่างไรต่อไป?”

21อาหิโธเฟลจึงทูลว่า “ขอทรงไปหลับนอนกับบรรดาสนมของราชบิดาซึ่งเฝ้าวังอยู่ แล้วอิสราเอลทั้งปวงจะได้ทราบว่าฝ่าพระบาททรงเป็นที่เกลียดชังของราชบิดายิ่งนัก เพื่อคนของฝ่าพระบาทจะได้มีใจฮึกเหิมยิ่งขึ้น” 22ฉะนั้นพวกเขาจึงตั้งเต็นท์ขึ้นบนดาดฟ้าของวัง ให้อับซาโลมเข้าไปนอนกับบรรดาสนมของราชบิดาต่อหน้าต่อตาอิสราเอลทั้งปวง

23ครั้งนั้นทั้งดาวิดและอับซาโลมล้วนยึดถือคำแนะนำทุกอย่างของอาหิโธเฟล เสมือนกับทูลถามจากพระเจ้า