2 Samueli 1 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 1:1-27

Davide Amva za Imfa ya Sauli

1Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri. 2Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.

3Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”

4Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?”

Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”

5Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”

6Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira. 7Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’ ”

8Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”

9“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’

10“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”

11Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo. 12Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.

13Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”

14Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”

15Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa. 16Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’ ”

Davide Alira Maliro a Sauli ndi Yonatani

17Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani. 18Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:

19“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda.

Taonani amphamvu agwa kumeneko!

20“Musakanene zimenezi ku Gati,

musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni,

kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale,

ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.

21“Inu mapiri a ku Gilibowa,

musakhalenso ndi mame kapena mvula,

kapena minda yobereka zopereka za ufa.

Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa,

chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.

22“Pa magazi a ophedwa,

pa mnofu wa amphamvu,

uta wa Yonatani sunabwerere,

lupanga la Sauli silinabwere chabe.

23“Sauli ndi Yonatani,

pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima,

ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe.

Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga,

anali ndi mphamvu zoposa mkango.

24“Inu ana aakazi a Israeli,

mulireni Sauli,

amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,

amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.

25“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!

Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.

26Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,

unali wokondedwa kwambiri kwa ine.

Chikondi chako pa ine chinali chopambana,

chopambana kuposa chikondi cha akazi.

27“Taonani amphamvu agwa!

Zida zankhondo zawonongeka!”

Nova Versão Internacional

2 Samuel 1:1-27

Davi Recebe a Notícia da Morte de Saul

1Depois da morte de Saul, Davi retornou de sua vitória sobre os amalequitas. Fazia dois dias que ele estava em Ziclague 2quando, no terceiro dia, chegou um homem que vinha do acampamento de Saul, com as roupas rasgadas e terra na cabeça. Ao aproximar-se de Davi, prostrou-se com o rosto em terra, em sinal de respeito.

3Davi então lhe perguntou: “De onde você vem?”

Ele respondeu: “Fugi do acampamento israelita”.

4Disse Davi: “Conte-me o que aconteceu”.

E o homem contou: “O nosso exército fugiu da batalha, e muitos morreram. Saul e Jônatas também estão mortos”.

5Então Davi perguntou ao jovem que lhe trouxera as notícias: “Como você sabe que Saul e Jônatas estão mortos?”

6O jovem respondeu: “Cheguei por acaso ao monte Gilboa, e lá estava Saul, apoiado em sua lança. Os carros de guerra e os oficiais da cavalaria estavam a ponto de alcançá-lo. 7Quando ele se virou e me viu, chamou-me gritando, e eu disse: Aqui estou.

8“Ele me perguntou: ‘Quem é você?’

“Sou amalequita, respondi.

9“Então ele me ordenou: ‘Venha aqui e mate-me! Estou na angústia da morte!’.

10“Por isso aproximei-me dele e o matei, pois sabia que ele não sobreviveria ao ferimento. Peguei a coroa e o bracelete dele e trouxe-os a ti, meu senhor”.

11Então Davi rasgou suas vestes; e os homens que estavam com ele fizeram o mesmo. 12E se lamentaram, chorando e jejuando até o fim da tarde, por Saul e por seu filho Jônatas, pelo exército do Senhor e pelo povo de Israel, porque muitos haviam sido mortos à espada.

13E Davi perguntou ao jovem que lhe trouxera as notícias: “De onde você é?”

E ele respondeu: “Sou filho de um estrangeiro, sou amalequita”.

14Davi lhe perguntou: “Como você não temeu levantar a mão para matar o ungido do Senhor?”

15Então Davi chamou um dos seus soldados e lhe disse: “Venha aqui e mate-o!” O servo o feriu, e o homem morreu. 16Davi tinha dito ao jovem: “Você é responsável por sua própria morte. Sua boca testemunhou contra você, quando disse: ‘Matei o ungido do Senhor’ ”.

Davi Lamenta-se por Saul e Jônatas

17Davi cantou este lamento sobre Saul e seu filho Jônatas, 18e ordenou que se ensinasse aos homens de Judá; é o Lamento do Arco, que foi registrado no Livro de Jasar:

19“O seu esplendor, ó Israel, está morto sobre os seus montes.

Como caíram os guerreiros!

20“Não conte isso em Gate,

não o proclame nas ruas de Ascalom,

para que não se alegrem as filhas dos filisteus

nem exultem as filhas dos incircuncisos.

21“Ó colinas de Gilboa,

nunca mais haja orvalho

nem chuva sobre vocês,

nem campos que produzam trigo para as ofertas.

Porque ali foi profanado o escudo dos guerreiros,

o escudo de Saul, que nunca mais será polido com óleo.

22“Do sangue dos mortos,

da carne1.22 Hebraico: gordura. dos guerreiros,

o arco de Jônatas nunca recuou,

a espada de Saul sempre cumpriu a sua tarefa.

23“Saul e Jônatas, mui amados,

nem na vida nem na morte foram separados.

Eram mais ágeis que as águias,

mais fortes que os leões.

24“Chorem por Saul,

ó filhas de Israel!

Chorem aquele que as vestia de rubros ornamentos

e que suas roupas enfeitava com adornos de ouro.

25“Como caíram os guerreiros no meio da batalha!

Jônatas está morto sobre os montes de Israel.

26Como estou triste por você, Jônatas, meu irmão!

Como eu lhe queria bem!

Sua amizade era, para mim, mais preciosa

que o amor das mulheres!

27“Caíram os guerreiros!

As armas de guerra foram destruídas!”