2 Samueli 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 1:1-27

Davide Amva za Imfa ya Sauli

1Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri. 2Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.

3Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”

4Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?”

Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”

5Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”

6Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira. 7Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’ ”

8Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”

9“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’

10“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”

11Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo. 12Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.

13Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”

14Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”

15Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa. 16Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’ ”

Davide Alira Maliro a Sauli ndi Yonatani

17Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani. 18Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:

19“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda.

Taonani amphamvu agwa kumeneko!

20“Musakanene zimenezi ku Gati,

musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni,

kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale,

ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.

21“Inu mapiri a ku Gilibowa,

musakhalenso ndi mame kapena mvula,

kapena minda yobereka zopereka za ufa.

Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa,

chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.

22“Pa magazi a ophedwa,

pa mnofu wa amphamvu,

uta wa Yonatani sunabwerere,

lupanga la Sauli silinabwere chabe.

23“Sauli ndi Yonatani,

pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima,

ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe.

Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga,

anali ndi mphamvu zoposa mkango.

24“Inu ana aakazi a Israeli,

mulireni Sauli,

amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,

amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.

25“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!

Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.

26Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,

unali wokondedwa kwambiri kwa ine.

Chikondi chako pa ine chinali chopambana,

chopambana kuposa chikondi cha akazi.

27“Taonani amphamvu agwa!

Zida zankhondo zawonongeka!”

Священное Писание

2 Царств 1:1-27

Давуд узнаёт о смерти Шаула

1После смерти Шаула Давуд вернулся, победив амаликитян. Он пробыл в Циклаге два дня. 2На третий день из лагеря Шаула пришёл человек в разорванной одежде, а вся его голова была в пыли1:2 Такой внешний вид был знаком глубокой скорби.. Придя к Давуду, он поклонился ему, пав лицом на землю.

3– Откуда ты пришёл? – спросил его Давуд.

– Я спасся из стана исраильтян, – ответил он.

4– Что случилось? – спросил Давуд. – Расскажи мне.

Человек сказал:

– Народ бежал с поля боя. Многие пали. И Шаул, и его сын Ионафан мертвы.

5Давуд сказал юноше, который принёс ему это известие:

– Откуда ты знаешь, что Шаул и его сын Ионафан мертвы?

6– Я случайно оказался на горе Гильбоа, – сказал юноша, – и там был Шаул, который опирался на своё копьё, а колесницы и всадники приближались к нему. 7Обернувшись назад и увидев меня, он позвал меня, и я сказал: «Что мне сделать?» 8Он спросил меня: «Кто ты?» – «Амаликитянин», – ответил я. 9Тогда он сказал мне: «Подойди и убей меня! У меня агония, но я ещё жив». 10Я подошёл и убил его, потому что знал, что после своего поражения он не сможет жить. Я взял венец, который был у него на голове, и браслет с его руки и принёс их сюда, к моему господину.

11Тогда Давуд и все, кто был с ним, разорвали на себе одежду. 12Они рыдали, плакали и постились до вечера о Шауле, о его сыне Ионафане, о войске Вечного1:12 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь. и об Исраиле, потому что все они пали от меча. 13Давуд сказал юноше, который принёс ему известие:

– Откуда ты?

– Я сын чужеземца, амаликитянина, – ответил он.

14Давуд сказал ему:

– Как же ты не побоялся поднять руку на помазанника Вечного?

15Давуд позвал одного из своих людей и сказал ему:

– Подойди и убей его!

И тот убил его. 16А Давуд сказал, повернувшись к амаликитянину:

– Твоя кровь на твоей голове. Ты сам свидетельствовал против себя, когда сказал: «Я убил помазанника Вечного».

Плач Давуда о Шауле и Ионафане

17Давуд оплакивал Шаула и его сына Ионафана этой горестной песней 18и приказал научить жителей Иудеи этой «Песне лука» (она записана в «Книге Праведного»1:18 Букв.: «Книга Иашара». Эта древняя книга, не вошедшая в состав Священного Писания, не сохранилась до наших времён.):

19«Слава твоя, о Исраил, сражена на твоих высотах.

Как пали могучие!

20Не объявляйте об этом в Гате,

не разглашайте на улицах Ашкелона,

чтобы не радовались дочери филистимлян,

чтобы не ликовали дочери необрезанных.

21О горы Гильбоа,

пусть не будет вам ни росы, ни дождя,

ни щедрых полей.

Ведь там осквернён был щит могучих,

щит Шаула – не натираемый больше маслом.

22Без крови сражённых,

без плоти могучих

лук Ионафана не возвращался назад,

меч Шаула не возвращался даром.

23Шаул и Ионафан –

столь любимы и чтимы при жизни,

и в смерти не разлучились.

Были они быстрее орлов,

львов сильнее.

24О дочери Исраила,

оплакивайте Шаула,

который одевал вас в роскошные алые наряды,

который украшал ваши платья золотым убранством.

25Как пали могучие в бою!

Ионафан сражён на высотах твоих, Исраил.

26Я скорблю по тебе, Ионафан, мой брат,

ты был мне очень дорог.

Твоя любовь была для меня прекрасна,

прекраснее любви женщин.

27Как пали могучие!

Погибло оружие брани!»