2 Petro 3 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Petro 3:1-18

Kubwera kwa Ambuye

1Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera. 2Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.

3Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa. 4Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.” 5Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi. 6Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa. 7Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.

8Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi! 9Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.

10Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.

11Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu 12pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha. 13Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.

14Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye. 15Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa. 16Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.

17Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa. 18Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Петруса 3:1-18

День Вечного Повелителя

1Это, возлюбленные, уже моё второе послание к вам. Я написал эти послания для того, чтобы напоминанием призвать вас рассуждать здраво, 2чтобы вы помнили слова, сказанные в прошлом святыми пророками, и учение Повелителя и Спасителя, переданное Его посланниками.

3Прежде всего вы должны помнить о том, что в последнее время появятся наглые насмешники, идущие на поводу своих низменных желаний 4и говорящие: «Так как же насчёт обещания Его прихода? Ведь с тех пор, как умерли отцы, всё остаётся так, как было от начала творения». 5Но они сознательно пренебрегают тем, что некогда вселенная была создана словом Всевышнего, что воды были собраны и появилась суша3:5 Букв.: «из воды и водою»., 6а также тем, что посредством воды был разрушен прежний мир, будучи затоплен. 7А нынешний мир тем же словом Всевышнего сберегается для огня, он сохраняется до Судного дня и гибели безбожных людей.

8Не забывайте одного, возлюбленные: для Вечного Повелителя один день – как тысяча лет и тысяча лет – как один день3:8 См. Заб. 89:5.. 9Вечный Повелитель не откладывает исполнения того, что Он обещал, хоть некоторые и называют это промедлением. Он долго терпит вас и ждёт, не желая, чтобы кто-нибудь погиб, но чтобы все покаялись.

10День возвращения Вечного Повелителя придёт внезапно, словно вор. Тогда небосвод с громким шумом исчезнет и небесные тела растворятся в огне, также и земля, и все дела на ней будут сожжены3:10 Или: «будут обнаружены»..

11Если всё будет так разрушено, то какой святой и благочестивой жизнью вы должны жить, 12ожидая с нетерпением прихода3:12 Или: «ожидая и ускоряя приход». дня Всевышнего, когда небосвод будет разрушен огнём и небесные тела будут расплавлены в невыносимом жаре?! 13Но мы, по Его обещанию, ожидаем нового неба и новой земли3:13 См. Ис. 65:17; 66:22; Отк. 21:1., где обитает праведность.

14Поэтому, возлюбленные, в ожидании этого постарайтесь, чтобы Он нашёл вас в мире, незапятнанными и непорочными. 15Долготерпение нашего Вечного Повелителя рассматривайте как спасение. О том же самом, по данной ему Всевышним мудрости, писал вам и наш дорогой брат Павлус. 16Он пишет об этом во всех своих посланиях. В них есть много такого, что вовсе не легко понять, что невежественные и неутверждённые люди искажают, как и другие Писания, к своей собственной погибели.

17Поэтому, возлюбленные, зная об этом заранее, будьте бдительны, чтобы вас не увлекли заблуждения беззаконников и вы не лишились твёрдой опоры. 18Возрастайте в благодати и познании нашего Повелителя и Спасителя Исо Масеха. Ему принадлежит слава и сегодня, и в день вечности! Аминь.