2 Mbiri 4 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 4:1-22

Zipangizo za mʼNyumba ya Mulungu

1Solomoni anapanga guwa lamkuwa limene mulitali mwake linali mamita asanu ndi anayi, mulifupi mwakenso mamita asanu ndi anayi ndipo msinkhu wake unali mamita anayi ndi theka. 2Kenaka iye anapanga mbiya yayikulu yachitsulo. Inali yozungulira ndipo pakamwa pake panali pa mamita anayi ndi theka, poyeza modutsa pakati pake. Msinkhu wake unali wopitirirapo mamita awiri. Thunthu lake linali mamita 13. 3Mʼmunsi mwa mkombero wa mbiyayo anajambulamo zithunzi zangʼombe zazimuna mozungulira, zithunzi khumi pa theka la mita. Ngʼombezo zimajambulidwa mʼmizere iwiri ndipo anazipangira kumodzi ndi mbiyayo.

4Mbiyayo anayisanjika pa ngʼombe zamkuwa khumi ndi ziwiri, zitatu zoyangʼana kumpoto, zitatu zoyangʼana kumadzulo, zitatu zoyangʼana kummwera ndipo zitatu zoyangʼana kummawa. Mbiyayo inakhazikika pamwamba pa ngʼombezo, ndipo miyendo yake yonse yakumbuyo ya ngʼombezo inkaloza mʼkati. 5Mbiyayo inali yochindikala ngati chikhatho ndipo mkombero wake unali ngati mkombero wa chikho, ngati duwa lokongola kwambiri. Mʼmbiyamo munkalowa madzi okwana malita 60,000.

6Kenaka anapanga mabeseni khumi otsukira zinthu ndipo asanu amawayika mbali ya kummwera, asanu mbali ya kumpoto. Mʼmenemo amatsukiramo zinthu zimene zimagwiritsidwa ntchito pa nsembe zopsereza koma mbiyamo ndi mʼmene ankasambiramo ansembe.

7Solomoni anapanga zoyikapo nyale khumi zagolide monga momwe kunalembedwera ndipo anaziyika mʼNyumba ya Mulungu, zisanu mbali ya kummwera, ndi zisanu mbali ya kumpoto.

8Iye anapanga matebulo khumi ndipo anawayika mʼNyumba ya Mulungu, asanu mbali ya kummwera ndi asanu mbali ya kumpoto. Iye anapanganso mabeseni agolide okwanira 100.

9Iye anapanga bwalo la ansembe, bwalo lalikulu ndi zitseko za bwalolo ndipo anakuta zitsekozo ndi mkuwa. 10Anayika mbiya ija mbali yakummwera pamene mbali ya kummawa ndi kummwera zimakumana.

11Iye anapanganso miphika ndi mafosholo ndi mabeseni owazira magazi.

Kotero Hiramu anatsiriza ntchito yonse ya ku Nyumba ya Mulungu imene ankagwirira Mfumu Solomoni:

12Nsanamira ziwiri;

mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

maukonde awiri okongoletsera mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

13makangadza 400 a maukonde awiri okongoletserawo (mizere iwiri ya makangadza pa ukonde uliwonse, kukongoletsa mbale za mitu yapamwamba pa nsanamira);

14miyendo pamodzi ndi mabeseni ake;

15mbiya pamodzi ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri zazimuna zosanjikapo mbiyayo.

16Miphika, mafosholo, mafoloko otengera nyama ndi ziwiya zina zonse.

Zipangizo zonse zimene Hiramu Abi anapangira Mfumu Solomoni za mʼNyumba ya Yehova zinali zamkuwa wonyezimira. 17Mfumu inapangitsa zimenezi mʼchigwa cha Yorodani, ku malo amtapo amene anali pakati pa Sukoti ndi Zaretani. 18Zinthu zonse zimene Solomoni anapanga zinali zochuluka kwambiri kotero kuti kulemera kwa mkuwa sikunadziwike.

19Solomoni anapanganso ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Mulungu:

guwa lansembe lagolide;

matebulo pamene ankayikapo buledi woperekedwa kwa Mulungu;

20zoyikapo nyale zagolide ndi nyale zake zagolide weniweni, kuti ziziyaka mʼkati mwenimweni mwa malo opatulika monga analembera,

21maluwa agolide, nyale ndi mbaniro. (Zinali zagolide mmodzi);

22zozimitsira nyale zagolide weniweni, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zitseko zagolide za Nyumba ya Mulungu, chitseko cha ku Malo Opatulika Kwambiri ndi zitseko za ku chipinda chachikulu.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 4:1-22

Huram-Abi laver de øvrige ting til templet

1.Kong. 7,23-26.38-51

1Huram lavede et stort bronzealter, 9 m langt, 9 m bredt og 4,5 m højt. 2Han støbte også en stor, rund vandbeholder, bronzehavet, 2,25 m dyb, 4,5 m i diameter og 13,5 m i omkreds. 3På ydersiden lige under kanten hele vejen rundt blev der lavet to rækker okselignende4,3 Der skulle nok have stået „græskarlignende” som i 1.Kong. 7,24. (Fejlen skyldes sikkert, at de to hebraiske ord ligner hinanden meget.) udsmykninger med ca. 5 cm mellem hver, formet i ét med resten af bronzehavet. 4Den stod på 12 bronzeokser, der vendte halerne mod hinanden, således at okserne tre og tre så i retning af de fire verdenshjørner. 5Beholderens tykkelse var en håndsbred, og kanten var bølgeformet som toppen af en liljeblomst. Den rummede 3000 bat.4,5 Sandsynligvis en kopieringsfejl. Der skulle nok have stået „2000 bat” som i 1.Kong. 7,26. En bat er som før nævnt ca. 22 liter.

6Derefter lavede han ti store vandfade til brug under rengøringen af offerdyrene. De blev anbragt tæt ved det store bronzehav, fem på hver side. Præsterne brugte bronzehavet, når de skulle vaske sig i forbindelse med den ceremonielle renselse.

7Så støbte han ti guldlysestager efter de anvisninger, han havde fået. De blev anbragt inde i tempelrummet—fem langs hver væg. 8Han lavede desuden ti borde og placerede dem langs templets væg, fem på sydsiden og fem på nordsiden. Han støbte også 100 stænkeskåle i guld.

9Dernæst blev præsternes indre forgård og den ydre forgård gjort færdige. Dørene til begge forgårde blev belagt med bronze. 10Bronzehavet blev placeret ved templets sydøstlige hjørne.

11Det var også Huram, der lavede alle de forskellige redskaber til brug ved offerhandlingerne: askebakker, skovle og stænkeskåle. Således fuldførte han den opgave, kong Salomon havde pålagt ham: 12De to søjler; de to liljeformede søjlehoveder med tilhørende fletværk 13og de 400 granatæbler; 14rullebordene med tilhørende vandfade; 15bronzehavet og dets fundament bestående af 12 okser; 16askebakkerne, skovlene, kødgaflerne og de øvrige redskaber. Alle disse genstande var lavet af blankpoleret bronze4,16 Eller: „kobber”. Det er det samme ord på hebraisk. 17-18og støbt i lerforme i Jordandalen mellem Sukkot og Zereda. Totalvægten af den bronze, der blev brugt, vides ikke; der gik simpelt hen så meget bronze til, at man opgav at veje det.

19Salomon fik al inventaret til brug inde i selve templet belagt med rent guld—både redskaberne, røgelsesalteret, bordet til de hellige brød, 20lysestagerne til lamperne, som skulle brænde i rummet foran det allerhelligste ifølge forskrifterne, 21blomsterdekorationerne, lamperne, tængerne, 22vægesaksene, stænkeskålene, fadene og bakkerne til gløder. Både dørene ind til det allerhelligste rum og dørene ved templets hovedindgang blev belagt med guld.