2 Mbiri 30 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 30:1-27

Hezekiya Achita Chikondwerero cha Paska

1Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. 2Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri. 3Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu. 4Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse. 5Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.

6Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti,

“Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya. 7Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu. 8Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni. 9Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”

10Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe. 11Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu. 12Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.

13Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri. 14Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.

15Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova. 16Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi. 17Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova. 18Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense 19amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.” 20Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.

21Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.

22Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.

23Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala. 24Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa. 25Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda. 26Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu. 27Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.

Священное Писание

2 Летопись 30:1-27

Приготовления к празднику Освобождения

1Езекия послал объявить по всему Исраилу и Иудее, и написал письма Ефраиму и Манассе, приглашая их прийти в храм Вечного в Иерусалиме и отметить праздник Освобождения30:1 Праздник Освобождения – этот праздник отмечался в память об избавлении иудейского народа под руководством пророка Мусы из Египетского рабства (см. Исх. 12; 13:17-22; 14; Втор. 16:1-8)., установленный Вечным, Богом Исраила. 2Царь, его приближённые и всё собрание в Иерусалиме решили на совете отмечать праздник Освобождения во втором месяце (в середине весны). 3Они не могли отметить его в установленное время, потому что не хватало священнослужителей, которые успели бы освятиться, и народ ещё не собрался в Иерусалиме. 4Это решение понравилось и царю, и всему собранию. 5Они решили объявить по всему Исраилу, от Беэр-Шевы на юге до Дана на севере, чтобы народ шёл в Иерусалим отмечать праздник Освобождения, установленный Вечным, Богом Исраила, потому что его не отмечали всенародно, как было предписано. 6И гонцы с письмами от царя и его приближённых прошли по всему Исраилу и Иудее, возвещая повеления царя:

«Народ Исраила, вернитесь к Вечному, Богу Ибрахима, Исхака и Якуба30:6 Букв.: «Исраила». Всевышний дал Якубу новое имя – Исраил (см. Нач. 32:27-28)., чтобы Он вернулся к вам, оставшийся народ, уцелевший от рук царей Ассирии. 7Не будьте как ваши отцы и братья, которые нарушили верность Вечному, Богу их предков, за что Он предал их на опустошение, как вы и видите. 8Не будьте упрямыми, как ваши отцы, покоритесь Вечному. Придите в святилище, которое Он освятил навеки. Служите Вечному, вашему Богу, чтобы Его пылающий гнев на вас прекратился. 9Если вы вернётесь к Вечному, то взявшие в плен ваших родичей и детей пожалеют их, и они вернутся в эту страну, потому что Вечный, ваш Бог, милостив и милосерден30:9 Бог милостив и милосерден – это выражение основано на словах из Таурата (см. Исх. 34:6) и является родственным арабскому выражению: «бисмиллях-ир-рахман-ир-рахим», что переводится как: «Во имя Аллаха милостивого и милосердного». В доисламской Аравии христиане государства Набатея использовали похожее выражение, переняв его из иудейской традиции.. Он не отвернёт от вас Своего лица, если вы возвратитесь к Нему».

10Гонцы ходили из города в город в землях Ефраима и Манассы, до самых рубежей земли Завулона, но народ лишь насмехался и издевался над ними. 11И всё же, некоторые из родов Ашира, Манассы и Завулона смирили себя и пришли в Иерусалим. 12Да и в Иудее рука Всевышнего была на народе, даровав им единомыслие, чтобы им выполнить то, что по слову Вечного велели царь и его приближённые.

Езекия отмечает праздник Пресных хлебов

13Огромная толпа народа собралась в Иерусалиме отмечать праздник Пресных хлебов30:13 Праздник Пресных хлебов – этот праздник шёл сразу же за праздником Освобождения и длился семь дней. В эти дни предписывалось есть только пресный хлеб (см. Исх. 12:15-20; 13:3-10; Лев. 23:6-8; Чис. 28:17-25). во втором месяце. 14Они приступили к работе, и разрушили в Иерусалиме жертвенники идолам, и убрали все жертвенники для возжигания им благовоний, и бросили их в долину Кедрон. 15Они закололи жертвенного ягнёнка в четырнадцатый день второго месяца. Священнослужители и левиты, устыдившись, освятились и принесли в храм Вечного всесожжения. 16Они встали на свои обычные места, как предписано Законом пророка Мусы. Священнослужители кропили кровью, которую подавали им левиты. 17Так как многие в толпе не освятились, левитам пришлось закалывать жертвенных ягнят за всех, кто был ритуально нечист и не мог посвятить своего ягнёнка Вечному.

18Большая часть народа, где было много паломников из родов Ефраима, Манассы, Иссахара и Завулона, не очистилась, но ела жертвенное мясо, нарушая предписание. 19Но Езекия помолился за них, сказав:

– Пусть простит Вечный, Который благ, всякого, кто расположил своё сердце к поискам Вечного Бога, Бога его предков, даже если он нечист по закону святилища.

20Вечный услышал Езекию и исцелил народ. 21Исраильтяне, которые были в Иерусалиме, отмечали праздник Пресных хлебов семь дней с великой радостью, а левиты и священнослужители каждый день пели хвалебные песни Вечному под звуки музыкальных инструментов. 22Езекия милостиво говорил со всеми левитами, которые обнаружили хорошие познания в службе Вечного. В течение семи дней они ели полагавшуюся им долю, приносили жертвы примирения и открыто признавали свои грехи перед Вечным, Богом их предков.

23Затем всё собрание согласилось праздновать праздник ещё семь дней, так что они радостно праздновали и эти семь дней. 24Ведь царь Иудеи Езекия распорядился выдать собранию тысячу быков и семь тысяч овец и коз, а вельможи дали им тысячу быков и десять тысяч овец и коз. Много священнослужителей подготовилось к священной службе. 25Весь народ Иудеи радовался вместе со священнослужителями, и левитами, и всеми, кто собрался из Исраила, считая и чужеземцев, явившихся из Исраила и живших в Иудее. 26В Иерусалиме царила великая радость, ведь со дней исраильского царя Сулеймана, сына Давуда, в Иерусалиме не бывало ничего подобного. 27Священнослужители и левиты встали благословить народ, и Всевышний услышал их, потому что их молитва достигла небес, Его святого жилища.