2 Mbiri 29 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 29:1-36

Mfumu Hezekiya Ayeretsa Nyumba ya Mulungu

1Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.

3Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza. 4Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa 5ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika. 6Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira. 7Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli. 8Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino. 9Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo. 10Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere. 11Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”

12Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito:

Kuchokera ku banja la Kohati,

Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya;

kuchokera ku banja la Merari,

Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli;

kuchokera ku banja la Geresoni,

Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;

13kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani,

Simiri ndi Yeiyeli;

kuchokera kwa zidzukulu za Asafu,

Zekariya ndi Mataniya;

14kuchokera kwa zidzukulu za Hemani,

Yehieli ndi Simei;

kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni,

Semaya ndi Uzieli.

15Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova. 16Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni. 17Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.

18Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse. 19Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”

20Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova. 21Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova. 22Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe. 23Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo. 24Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.

25Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri. 26Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.

27Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli. 28Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.

29Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira. 30Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.

31Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.

32Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova. 33Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000. 34Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe. 35Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza.

Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso. 36Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 29:1-36

Hezekiah Purifies the Temple

1Hezekiah was 25 years old when he became king. He ruled in Jerusalem for 29 years. His mother’s name was Abijah. She was the daughter of Zechariah. 2Hezekiah did what was right in the eyes of the Lord, just as King David had done.

3In the first month of Hezekiah’s first year as king, he opened the doors of the Lord’s temple. He repaired them. 4He brought the priests and Levites in. He gathered them together in the open area on the east side of the temple. 5He said, “Levites, listen to me! Set yourselves apart to the Lord. Set apart the temple of the Lord. He’s the God of your people who lived long ago. Remove anything ‘unclean’ from the temple. 6Our people weren’t faithful. They did what was evil in the eyes of the Lord our God. They deserted him. They turned their faces away from the place where he lives. They turned their backs on him. 7They also shut the doors of the temple porch. They put the lamps out. They didn’t burn incense at the temple. They didn’t sacrifice burnt offerings there to the God of Israel. 8So the Lord has become angry with Judah and Jerusalem. He has made them look so bad that everyone is shocked when they see them. They laugh at them. You can see it with your own eyes. 9That’s why our fathers have been killed by swords. That’s why our sons and daughters and wives have become prisoners. 10So I’m planning to make a covenant with the Lord, the God of Israel. Then he’ll stop being angry with us. 11My sons, don’t fail to obey the Lord. He has chosen you to stand in front of him and work for him. He wants you to serve him and burn incense to him.”

12Here are the Levites who went to work.

Mahath and Joel were from the family line of Kohath.

Mahath was the son of Amasai. Joel was the son of Azariah.

Kish and Azariah were from the family line of Merari.

Kish was the son of Abdi. Azariah was the son of Jehallelel.

Joah and Eden were from the family line of Gershon.

Joah was the son of Zimmah. Eden was the son of Joah.

13Shimri and Jeiel were from the family line of Elizaphan.

Zechariah and Mattaniah were from the family line of Asaph.

14Jehiel and Shimei were from the family line of Heman.

Shemaiah and Uzziel were from the family line of Jeduthun.

15All these Levites gathered the other Levites together. They set themselves apart to the Lord. Then they went in to purify the Lord’s temple. That’s what the king had ordered them to do. They did what the Lord told them to. 16The priests went into the Lord’s temple to make it pure. They brought out to the temple courtyard everything that was “unclean.” They had found “unclean” things in the Lord’s temple. The Levites took them and carried them out to the Kidron Valley. 17On the first day of the first month they began to set everything in the temple apart to the Lord. By the eighth day of the month they reached the Lord’s porch. For eight more days they set the Lord’s temple itself apart to him. They finished on the 16th day of the first month.

18Then they went to King Hezekiah. They reported, “We’ve purified the whole temple of the Lord. That includes the altar for burnt offerings and all its tools. It also includes the table for the holy bread and all its objects. 19We’ve prepared all the things King Ahaz had removed. We’ve set them apart to the Lord. Ahaz had removed them while he was king. He wasn’t faithful to the Lord. Those things are now in front of the Lord’s altar.”

20Early the next morning King Hezekiah gathered together the city officials. They all went up to the Lord’s temple. 21They brought seven bulls, seven rams, seven male lambs and seven male goats with them. They sacrificed the animals as a sin offering for the kingdom, for the temple and for Judah. The king commanded the priests to offer them on the Lord’s altar. The priests were from the family line of Aaron. 22They killed the bulls. Then they splashed the blood against the altar. Next they killed the rams and splashed the blood against the altar. Then they killed the lambs and splashed the blood against the altar. 23The goats for the sin offering were brought to the king and the whole community. They placed their hands on them. 24Then the priests killed the goats. They put the blood on the altar as a sin offering. It paid for the sin of the whole nation of Israel. The king had ordered the burnt offering and the sin offering for the whole nation.

25Hezekiah stationed the Levites in the Lord’s temple. They had cymbals, harps and lyres. They did everything in the way King David, his prophet Gad, and Nathan the prophet had required. The Lord had given commands about all these things through his prophets. 26So the Levites stood ready with David’s musical instruments. And the priests had their trumpets ready.

27Hezekiah gave the order to sacrifice the burnt offering on the altar. The offering began. Singing to the Lord also began. The singing was accompanied by the trumpets and by the instruments of David. He had been king of Israel. 28The whole community bowed down. They worshiped the Lord. At the same time the musicians played their musical instruments. The priests blew their trumpets. All of that continued until the burnt offering had been sacrificed.

29So the offerings were finished. King Hezekiah got down on his knees. He worshiped the Lord. So did everyone who was with him. 30The king and his officials ordered the Levites to praise the Lord. They used the words of David and Asaph the prophet. They sang praises with joy. They bowed down and worshiped the Lord.

31Then Hezekiah said, “You have set yourselves apart to the Lord. Come and bring sacrifices and thank offerings to his temple.” So the whole community brought sacrifices and thank offerings. Everyone who wanted to brought burnt offerings.

32The whole community brought 70 bulls, 100 rams and 200 male lambs. They brought all of them as burnt offerings to the Lord. 33The total number of animals set apart as sacrifices to the Lord was 600 bulls and 3,000 sheep and goats. 34But there weren’t enough priests to skin all the burnt offerings. So their relatives, the Levites, helped them. They worked until the task was finished. By that time other priests had been set apart to the Lord. The Levites had been more careful than the priests when they set themselves apart. 35There were large numbers of burnt offerings, along with the drink offerings and the fat from the friendship offerings. They were offered along with the burnt offerings.

So the service of the Lord’s temple was started up again. 36Hezekiah and all the people were filled with joy. That’s because everything had been done so quickly. God had provided for his people in a wonderful way.