2 Mbiri 22 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 22:1-12

Ahaziya Mfumu ya Yuda

1Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.

2Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.

3Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika. 4Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake. 5Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu, 6kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu.

Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.

7Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu. 8Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha. 9Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.

Ataliya ndi Yowasi

10Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda. 11Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe. 12Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 22:1-12

Ahaziah King of Judah

1The people of Jerusalem made Ahaziah king in place of Jehoram. Ahaziah was Jehoram’s youngest son. Robbers had come with the Arabs into Jehoram’s camp. The robbers had killed all his older sons. So Ahaziah, the king of Judah, began to rule. He was the son of Jehoram.

2Ahaziah was 22 years old when he became king. He ruled in Jerusalem for one year. His mother’s name was Athaliah. She was a granddaughter of Omri.

3Ahaziah also followed the ways of the royal family of Ahab. That’s because Ahaziah’s mother gave him bad advice. She told him to do what was wrong. 4So he did what was evil in the eyes of the Lord. He did what the family of Ahab had done. After Ahaziah’s father died, the members of Ahab’s family became his advisers. That’s what destroyed him. 5He also followed their advice when he joined forces with Joram, the king of Israel. They went to war against Hazael at Ramoth Gilead. Joram was the son of Ahab. Hazael was king of Aram. The soldiers of Aram wounded Joram. 6So he returned to Jezreel to give his wounds time to heal. His enemies had wounded him at Ramoth in his battle against Hazael, the king of Aram.

Ahaziah, the son of Jehoram, went down to Jezreel. He went there to see Joram. That’s because Joram had been wounded. Ahaziah was king of Judah. Joram was the son of Ahab.

7Through Ahaziah’s visit to Joram, God caused Ahaziah to fall from power. When Ahaziah arrived, he rode out with Joram to meet Jehu, the son of Nimshi. The Lord had anointed Jehu to destroy the royal family of Ahab. 8So Jehu punished Ahab’s family, just as the Lord had told him to. While he was doing it, he found the officials of Judah and the sons of Ahaziah’s relatives. They had been serving Ahaziah. So Jehu killed them. 9Then he went to look for Ahaziah. Jehu’s men captured him while he was hiding in Samaria. Ahaziah was brought to Jehu and put to death. People buried him, because they said, “He was a grandson of Jehoshaphat, who followed the Lord with all his heart.” So no one in the royal family of Ahaziah was powerful enough to keep the kingdom.

Athaliah and Joash

10Athaliah was Ahaziah’s mother. She saw that her son was dead. So she began to wipe out the whole royal family of Judah. 11But Jehosheba went and got Joash, the son of Ahaziah. Jehosheba was the daughter of King Jehoram. She stole Joash away from among the royal princes. All of them were about to be murdered. She put Joash and his nurse in a bedroom. Jehosheba, the daughter of King Jehoram, was the wife of Jehoiada the priest. She was also Ahaziah’s sister. So Jehosheba hid the child from Athaliah. That’s why Athaliah couldn’t kill him. 12The child remained hidden with the priest and his wife at God’s temple for six years. Athaliah ruled over the land during that time.