2 Mbiri 17 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 17:1-19

Yehosafati Mfumu ya Yuda

1Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli. 2Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.

3Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala. 4Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli. 5Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri. 6Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.

7Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda. 8Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu. 9Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.

10Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati. 11Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.

12Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda 13ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu. 14Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere:

kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000;

mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;

15otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;

16otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.

17Kuchokera ku Benjamini:

Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;

18otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.

19Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

2 Летопись 17:1-19

Иосафат – царь Иудеи

1Иосафат, его сын, стал царём вместо него и укрепился против Исраила. 2Он поставил войска во всех укреплённых городах Иудеи и разместил отряды в Иудее и в городах Ефраима, которые захватил его отец Аса.

3Вечный был с Иосафатом, потому что в свои ранние годы он следовал путям своего предка Давуда. Он не вопрошал статуи Баала17:3 Баал – ханаанский бог плодородия и бог-громовержец., 4а искал Бога своего отца и поступал по Его повелениям, а не по обычаям Исраила. 5Вечный утвердил его царство, и вся Иудея принесла Иосафату дары, так что он стал почитаем и к тому же очень богат. 6Его сердце было предано путям Вечного. Он убрал в Иудее капища на возвышенностях и столбы Ашеры.

7На третьем году своего правления, он послал своих приближённых Бен-Хаиля, Авдия, Закарию, Нетанила и Михея учить в городах Иудеи. 8С ними были левиты: Шемая, Нетания, Зевадия, Асаил, Шемирамот, Ионафан, Адония, Тобия и Тов-Адония, и священнослужители Элишама и Иорам. 9Они учили в Иудее, имея с собой книгу Закона Вечного. Они обходили все города Иудеи и учили народ.

10Ужас перед Вечным охватил все царства земель, которые окружали Иудею, и они не воевали с Иосафатом. 11Некоторые из филистимлян приносили Иосафату дары и в дань – серебро, а арабы привели ему стада мелкого скота: семь тысяч семьсот баранов и семь тысяч семьсот козлов.

12Иосафат становился всё сильнее и сильнее. Он строил в Иудее крепости и города для хранения припасов 13и держал в городах Иудеи много припасов, а в Иерусалиме у него были опытные, могучие воины. 14Вот их список по кланам:

Из рода Иуды отрядами в тысячу человек командовали:

военачальник Аднах, у которого было 300 000 отличных воинов;

15за ним – военачальник Иоханан с 280 000 людей;

16за ним – Амасия, сын Зихри, который добровольно вызвался нести службу Вечного с 200 000 отличных воинов.

17Из рода Вениамина:

Элиада, могучий воин, с 200 000 людей, вооружённых луками и щитами;

18за ним – Иехозавад со 180 000 людей, вооружённых для битвы.

19Это воины, которые служили царю, помимо тех, кого он поставил в укреплённых городах по всей Иудее.