2 Mbiri 16 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 16:1-14

Zaka Zotsiriza za Asa

1Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.

2Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko. 3Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”

4Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali. 5Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo. 6Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.

7Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu. 8Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. 9Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”

10Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.

11Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli. 12Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga. 13Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. 14Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 16:1-14

Asa’s Last Years

1Baasha was king of Israel. He marched out against Judah. It was in the 36th year of Asa’s rule over Judah. Baasha built up the walls of Ramah. He did it to keep people from leaving or entering the territory of Asa, the king of Judah.

2Asa took the silver and gold from among the treasures of the Lord’s temple and his own palace. He sent it to Ben-Hadad. Ben-Hadad was king of Aram. He was ruling in Damascus. 3“Let’s make a peace treaty between us,” Asa said. “My father and your father had made a peace treaty between them. Now I’m sending you silver and gold. So break your treaty with Baasha, the king of Israel. Then he’ll go back home.”

4Ben-Hadad agreed with King Asa. He sent his army commanders against the towns of Israel. His army captured Ijon, Dan, Abel Maim and all the cities in Naphtali where Baasha stored things. 5Baasha heard about it. So he stopped building up Ramah and left that place. 6Then King Asa brought all the men of Judah to Ramah. They carried away the stones and wood Baasha had been using. Asa used them to build up Geba and Mizpah.

7At that time Hanani the prophet came to Asa, the king of Judah. He said to him, “You trusted the king of Aram. You didn’t trust in the Lord your God. So the army of the king of Aram has escaped from you. 8The people of Cush and Libya had a strong army. They had large numbers of chariots and horsemen. But you trusted in the Lord. So he handed them over to you. 9The Lord looks out over the whole earth. He gives strength to those who commit their lives completely to him. You have done a foolish thing. From now on you will be at war.”

10Asa was angry with the prophet because of what he had said. In fact, he was so angry he put him in prison. At the same time, Asa treated some of his own people very badly.

11The events of Asa’s rule from beginning to end are written down. They are written in the records of the kings of Judah and Israel. 12In the 39th year of Asa’s rule his feet began to hurt. The pain was terrible. But even though he was suffering, he didn’t look to the Lord for help. All he did was go to the doctors. 13In the 41st year of Asa’s rule he joined the members of his family who had already died. 14He was buried in a tomb. He had cut it out for himself in the City of David. His body was laid on a wooden frame. It was covered with spices and different mixes of perfume. A huge fire was made to honor him.