2 Mbiri 14 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 14:1-15

1Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.

Asa Mfumu ya Yuda

2Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake. 3Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera. 4Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake. 5Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake. 6Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.

7Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.

8Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.

9Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa. 10Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.

11Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”

12Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa, 13ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo. 14Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko. 15Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 14:1-14

Asa som konge over Juda

1.Kong. 15,11-15

1Asa gjorde, hvad der var godt og rigtigt i Herrens, hans Guds, øjne. 2Han nedbrød afgudsaltrene på offerhøjene og ødelagde frugtbarhedspælene og Asherapælene. 3Han opfordrede alle judæerne til at søge Herren, deres fædres Gud, og overholde Guds love og befalinger. 4Som følge af, at Asa fjernede alle røgelsesaltre og offersteder for afguderne rundt omkring i Judas byer, sørgede Gud for fred i landet. 5Herren sørgede for, at ingen af hans fjender gik til angreb på landet, så i denne fredelige periode greb Asa anledningen til at genopbygge forsvarsværkerne omkring Judas byer.

6Han sagde til Judas folk: „Nu er der fred i vores land, fordi vi har søgt Herren, og det er ham, der har givet os den fred. Lad os derfor benytte chancen til at befæste byerne med mure, tårne og forskansede porte.” Så gik de i gang med arbejdet, der forløb godt.

7Kong Asas hær bestod af 300.000 mænd fra Judas stamme, bevæbnet med spyd og aflange skjolde, og 280.000 mænd fra Benjamins stamme, bevæbnet med runde skjolde og buer. Alle Asas mænd var veltrænede og modige krigere.

8Engang rykkede en stor hær under ledelse af kushitten Zerach ud mod kong Asa. Hæren bestod af en million mænd og 300 stridsvogne, og de slog lejr ved byen Maresha. 9Asa rykkede ud imod dem med sin hær og lejrede sig i dalen nord for byen.

10„Herre,” bad Asa, „for dig er det uden betydning, om man har en stor eller lille hær. Du er vores Gud, og vi stoler på dig. I dit navn rykker vi ud imod den enorme hær. Lad ikke noget menneske besejre dig, Herre!”

11Derpå slog Herren fjendens hær for øjnene af Asa og hans mænd. Hæren flygtede, 12og judæerne forfulgte dem helt til Gerar, indtil hele den fjendtlige hær var udslettet, for Herren og hans hær dræbte dem alle. Derefter vendte den judæiske hær tilbage med et stort krigsbytte. 13Undervejs angreb de alle småbyerne i området, og alle indbyggerne blev grebet af frygt for Herren. Også fra disse byer tog judæerne et stort krigsbytte. 14Desuden plyndrede de nomadernes teltlejre og vendte tilbage til Jerusalem med masser af får, geder og kameler.