2 Mbiri 11 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 11:1-23

1Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.

2Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti, 3“Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti, 4‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’ ” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.

Rehobowamu Akhwimitsa Chitetezo cha Yuda

5Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda: 6Betelehemu, Etamu, Tekowa, 7Beti Zuri, Soko, Adulamu, 8Gati, Maresa, Zifi, 9Adoraimu, Lakisi, Azeka, 10Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini. 11Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo. 12Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.

13Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu. 14Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova. 15Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga. 16Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo. 17Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.

Banja la Rehobowamu

18Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese. 19Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu. 20Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti. 21Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.

22Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu. 23Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.

New Russian Translation

2 Паралипоменон 11:1-23

1Когда Ровоам прибыл в Иерусалим, он собрал сто восемьдесят тысяч отборных воинов из дома Иуды и Вениамина, чтобы воевать с Израилем и вернуть себе царство.

2Но Шемае, Божьему человеку, было от Бога такое слово:

3– Скажи Ровоаму, сыну Соломона, царю Иудеи, и всем израильтянам в доме Иуды и Вениамина: 4«Так говорит Господь: Не ходите воевать со своими братьями. Ступайте все по домам, потому что это произошло по Моей воле».

Они послушались слова Господа и вернулись из похода против Иеровоама.

Ровоам укрепляет города Иудеи

5Ровоам жил в Иерусалиме и укрепил в Иудее города для защиты: 6Вифлеем, Етам, Текоа, 7Бет-Цур, Сохо, Адуллам, 8Гат, Марешу, Зиф, 9Адораим, Лахиш, Азеку, 10Цору, Айялон и Хеврон. Это укрепленные города в землях Иудеи и Вениамина. 11Он укрепил их оборонительные сооружения, поставил в них военачальников и устроил во всех этих городах хранилища для хлеба, оливкового масла и вина. 12Он также снабдил эти города щитами и копьями и хорошо укрепил их. Земли Иудеи и Вениамина остались под его контролем.

Переселение священников и левитов в Иудею

13Священники и левиты из всех областей земли Израиля встали на его сторону. 14Левиты даже оставили свои пастбища и все добро и отправились в Иудею и Иерусалим, потому что Иеровоам со своими сыновьями отстранил их от служения Господу. 15Он назначил своих жрецов в святилищах на возвышенностях, где он поставил идолов в образе козлов и тельцов, которых он сделал. 16Те изо всех родов Израиля, кто отдал сердца тому, чтобы искать Господа, Бога Израиля, последовали за левитами в Иерусалим, чтобы приносить жертвы Господу, Богу их отцов. 17Они укрепили царство Иудеи и поддерживали Ровоама, сына Соломона, три года, ходя путями Давида и Соломона в течение этого времени.

Семья Ровоама

18Ровоам женился на своей двоюродной сестре Махалате, которая была дочерью Давидова сына Иеримота и Авихаиль, дочери Иессеева сына Элиава. 19Она родила ему сыновей: Иеуша, Шемарию и Загама. 20Затем он женился на своей двоюродной сестре Маахе, внучке Авессалома, которая родила ему Авию, Аттая, Зизу и Шеломита. 21Ровоам любил Мааху, внучку Авессалома, больше всех своих жен и наложниц. Всего у него было восемнадцать жен и шестьдесят наложниц, двадцать восемь сыновей и шестьдесят дочерей.

22Ровоам поставил Авию, сына Маахи, вождем над его собственными братьями, чтобы сделать его царем. 23Он поступил мудро, разослав своих сыновей по всем землям Иудеи и Вениамина и по всем укрепленным городам. Он дал им в изобилии припасов и подыскал для них много жен.