2 Mbiri 11 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 11:1-23

1Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.

2Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti, 3“Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti, 4‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’ ” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.

Rehobowamu Akhwimitsa Chitetezo cha Yuda

5Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda: 6Betelehemu, Etamu, Tekowa, 7Beti Zuri, Soko, Adulamu, 8Gati, Maresa, Zifi, 9Adoraimu, Lakisi, Azeka, 10Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini. 11Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo. 12Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.

13Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu. 14Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova. 15Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga. 16Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo. 17Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.

Banja la Rehobowamu

18Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese. 19Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu. 20Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti. 21Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.

22Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu. 23Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Летопись 11:1-23

1Когда Реховоам прибыл в Иерусалим, он собрал сто восемьдесят тысяч лучших воинов из родов Иуды и Вениамина, чтобы воевать с Исроилом и вернуть себе царство. 2Но пророку Шемае было от Всевышнего такое слово:

3– Скажи Реховоаму, сыну Сулаймона, царю Иудеи, и всем исроильтянам в доме Иуды и Вениамина: 4Так говорит Вечный: «Не ходите воевать со своими братьями. Ступайте все по домам, потому что это произошло по Моей воле».

Они послушались слова Вечного и вернулись из похода против Иеровоама.

Реховоам укрепляет города Иудеи

5Реховоам жил в Иерусалиме и укрепил в Иудее города для защиты: 6Вифлеем, Етам, Текоа, 7Бет-Цур, Сохо, Адуллам, 8Гат, Мареша, Зиф, 9Адораим, Лахиш, Азеку, 10Цору, Аялон и Хеврон. Это укреплённые города в землях Иуды и Вениамина. 11Он укрепил их оборонительные сооружения, поставил в них военачальников и устроил во всех этих городах хранилища для хлеба, оливкового масла и вина. 12Он также снабдил щитами и копьями эти города и хорошо укрепил их. Земли Иуды и Вениамина остались под его контролем.

Переселение священнослужителей и левитов в Иудею

13Священнослужители и левиты из всех областей по всей земле Исроила встали на его сторону. 14Левиты даже оставили свои пастбища и всё добро и отправились в Иудею и Иерусалим, потому что Иеровоам со своими сыновьями отстранил их от служения Вечному. 15Он назначил своих жрецов в капища на возвышенностях, где он поставил идолов в образе козлов и тельцов, которых он сделал. 16А те из всех родов Исроила, кто отдал сердца тому, чтобы искать Вечного, Бога Исроила, последовали за левитами в Иерусалим, чтобы приносить жертвы Вечному, Богу их предков. 17Они укрепили царство Иудеи и поддерживали Реховоама, сына Сулаймона, три года, ходя путями Довуда и Сулаймона в течение этого времени.

Семья Реховоама

18Реховоам женился на Махалат, которая была дочерью Довудова сына Иеримота и Авихаиль, дочери Есеева сына Элиава. 19Она родила ему сыновей: Иеуша, Шемарию и Загама. 20Затем он женился на Маахе, внучке Авессалома, которая родила ему Авию, Аттая, Зизу и Шеломита. 21Реховоам любил Мааху, внучку Авессалома, больше всех своих жён и наложниц. Всего у него было восемнадцать жён и шестьдесят наложниц, двадцать восемь сыновей и шестьдесят дочерей.

22Реховоам поставил Авию, сына Маахи, вождём над его собственными братьями, чтобы сделать его царём. 23Он поступил мудро, разослав своих сыновей по всем землям Иудеи и Вениамина, по всем укреплённым городам. Он дал им в изобилии припасов и подыскал для них много жён.