2 Atesalonika 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 2:1-17

Kubwera kwa Munthu Woyipitsitsa

1Pa za kubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikumane naye, abale, tikukupemphani 2kuti musagwedezeke msanga mʼmaganizo kapena kuopsezedwa ndi uneneri, mbiri kapena kalata yokhala ngati yachokera kwa ife, yonena kuti tsiku lija la Ambuye linafika kale. 3Musalole kuti wina aliyense akunamizeni mwa njira ina iliyonse. Pakuti tsikulo lisanafike, kudzakhala mpatuko waukulu kwambiri, ndipo kudzaoneka munthu woyipitsitsa uja, munthu woyenera kuwonongedwayo. 4Iyeyo adzatsutsa ndi kudziyika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza. Iyeyo adzadzikhazika mʼNyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.

5Kodi simukukumbukira kuti pamene ndinali nanu pamodzi ndinkakuwuzani zimenezi? 6Ndipo tsopano mukudziwa chimene chikumuletsa kuonekera, koma adzawululika pa nthawi yake yoyenera. 7Pakuti mphamvu yobisika yoyipitsitsa ikugwira ntchito ngakhale tsopano; koma amene akutchinga mphamvuyo adzapitiriza kutero mpaka pamene wotchingayo adzachotsedwe. 8Ndipo kenaka woyipitsitsayo adzaonekera, amene Ambuye Yesu adzamugonjetsa ndi mpweya otuluka mʼkamwa mwake ndi kumuwononga ndi ulemerero wa kubwera kwake. 9Woyipitsitsayo adzabwera ndi mphamvu za Satana. Adzaonetsa mphamvu zake pochita zizindikiro ndi zodabwitsa zachinyengo. 10Iye adzagwiritsa ntchito mtundu uliwonse wachinyengo kupusitsa amene akuwonongeka. Iwo akuwonongeka chifukwa akukana kukonda choonadi ndi kuti apulumutsidwe. 11Chifukwa cha chimenechi, Mulungu akuwatumizira chinyengo chachikulu kuti akhulupirire bodza. 12Choncho adzalangidwa onse amene sanakhulupirire choonadi, koma anakondwera mu zoyipa.

Imani Mwamphamvu

13Koma tiyenera kuyamika Mulungu chifukwa cha inu abale okondedwa mwa Ambuye, pakuti Mulungu anakusankhani pachiyambi pomwe kuti mupulumuke chifukwa cha ntchito yoyeretsa ya Mzimu ndi chikhulupiriro chanu mʼchoonadi. 14Iye anakuyitanirani zimenezi kudzera mwa uthenga wathu wabwino, kuti mulandire nawo ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu. 15Kotero tsono, abale, imani mwamphamvu ndi kugwiritsa ziphunzitso zimene tinakupatsani kudzera mʼmawu apakamwa kapena kudzera mʼkalata.

16Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, 17akulimbikitseni ndi kukupatsani mphamvu yogwirira ntchito ndi kuyankhula zabwino zilizonse.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Фессалоникийцам 2:1-17

О человеке зла

1Что касается прихода нашего Повелителя Исо Масеха и того, как мы будем собраны к Нему, то мы просим вас, братья, 2не спешите верить всему и не тревожьтесь ни от какого духа, слуха или послания, якобы написанного нами, которые говорят, что день Вечного Повелителя уже пришёл. 3Смотрите, чтобы вас никто не ввёл в заблуждение никаким образом: день этот не придёт до тех пор, пока не произойдёт великое отступление от Всевышнего и не откроется человек зла2:3 Человек зла, или противник Масеха, на Востоке известен также под именем Даджжал., осуждённый на погибель. 4Он будет противостоять всему, что называют божеством или святыней, и превозноситься над этим. Он даже займёт место в храме Всевышнего2:4 Храм Всевышнего – вероятно, здесь говорится о восстановленном в будущем храме в Иерусалиме. и будет выдавать себя за Него2:4 См. Ис. 14:13-14; Езек. 28:2; Дон. 9:26-27; 11:36-37..

5Разве вы не помните, что, когда я был у вас, я говорил вам об этом? 6Теперь вы знаете, что сдерживает этого человека, не позволяя ему открыться до того, как настанет его время. 7Тайные силы зла уже в действии, но сначала должен уйти с дороги тот, кто пока ещё сдерживает их2:7 Тот, кто сдерживает – не вполне ясно кто или что здесь имеется в виду. Возможно, здесь говорится о Святом Духе, Который, действуя через общину верующих в Исо Масеха, удерживает силы зла и приход врага Масеха.. 8Тогда человек зла проявит себя. Но Повелитель Исо истребит его Своим дыханием, уничтожит славой Своего пришествия2:8 Ср. Аюб 4:9; Ис. 11:4.. 9Приход человека зла – это дело сатаны. Он будет действовать, являя разнообразные силы, ложные знамения и чудеса 10и совершая всякие злостные обманы, которым с лёгкостью поддадутся люди, погибающие из-за того, что не захотели полюбить истину и получить через неё спасение2:10 Спасение – спасение от пламени ада (см. Иуда 1:23), от гнева Всевышнего и Его судов (см. Рим. 5:9), от суетной жизни (см. 1 Пет. 1:18), от греха (см. Мат. 1:21) и от дьявола (см. 2 Тим. 2:26).. 11Потому и посылает Всевышний таким людям сильное заблуждение, чтобы они поверили лжи, 12для того, чтобы были осуждены те, кто не поверил истине и полюбил грех.

Слова ободрения

13Нам следует всегда благодарить Всевышнего за вас, братья, любимые Повелителем, потому что Он ещё от начала избрал вас2:13 Или: «потому что Он избрал вас быть первыми плодами». См. сноску на Якуб 1:18. ко спасению через освящение Духом и через вашу веру в истину. 14Он призвал вас к этому через наше возвещение Радостной Вести, чтобы вы разделили славу нашего Повелителя Исо Масеха. 15Поэтому, братья, стойте твёрдо и будьте верны учению, которое мы вам передали и на словах, и в нашем послании.

16Пусть Сам наш Повелитель Исо Масех и Всевышний, наш Небесный Отец, Который полюбил нас и по благодати дал нам вечное утешение и светлую надежду, 17утешит ваши сердца и укрепит вас на всякое доброе дело и слово.