2 Atesalonika 1 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 1:1-12

1Paulo, Silivano ndi Timoteyo.

Kulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

2Chisomo ndi mtendere kwa inu kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe. 4Nʼchifukwa chake, timayankhula monyadira mʼmipingo yonse ya Mulungu za kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pakati pa masautso onse ndi mayesero amene mukudutsamo.

5Zonsezi zikutsimikiza kuti Mulungu amaweruza molungama. Zotsatira zake ndi zakuti mudzatengedwa kukhala oyenera kulowa mu ufumu wa Mulungu umene mukuwuvutikira. 6Mulungu ndi wolungama ndipo adzalanga amene amakusautsaniwo 7ndikukupatsani mpumulo amene mukusautsidwa, pamodzi ndi ifenso. Izi zidzachitika Ambuye Yesu akadzaoneka mʼmalawi amoto kuchokera kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu. 8Iye adzalanga amene sadziwa Mulungu ndi amene samvera Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu. 9Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake 10pa tsiku limene iye adzabwera kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ndi kuyamikidwa ndi onse amene anakhulupirira. Inu mudzakhala nawo mʼgulumo chifukwa munakhulupirira umboni wathu.

11Nʼchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera mayitanidwe ake, ndi kuti mwa mphamvu zake akwaniritse cholinga chanu chilichonse chabwino ndi chilichonse chochitika mwachikhulupiriro. 12Ife timapempherera zimenezi kuti dzina la Ambuye athu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mulemekezedwe mwa Iyeyo. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha chisomo cha Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Swedish Contemporary Bible

2 Thessalonikerbrevet 1:1-12

Hälsning

1Från Paulus, Silvanus1:1 Samma person kallas Silas i Apostlagärningarna. och Timotheos.

Till församlingen i Thessalonike som lever i Gud, vår Fader, och Herren Jesus Kristus1:1 Se not till Matt 1:1..

2Nåd och frid från Gud, Fadern, och Herren Jesus Kristus.

Uppmuntran under förföljelse

3Syskon, vi måste alltid tacka Gud för er, och det finns goda skäl till det, för er tro fortsätter att växa och er kärlek till varandra blir hela tiden större. 4Därför berättar vi med stolthet om er i Guds församlingar, om er uthållighet och er tro mitt under alla de förföljelser och lidanden som drabbar er.

5Men de är tecken på Guds rättvisa dom, så att ni kan anses värdiga Guds rike, som ni nu lider för. 6Gud är rättfärdig och ger tillbaka plåga åt dem som nu plågar er. 7Ni som nu lider ska få vila ut tillsammans med oss när Herren Jesus kommer tillbaka från himlen och visar sig med sina mäktiga änglar, 8i flammande eld, för att straffa dem som inte vill veta av Gud och som inte lyssnar till evangeliet om vår Herre Jesus. 9Dessa människor ska straffas med evigt fördärv och skiljas från Herrens närvaro och hans makt och härlighet, 10den dag han kommer för att förhärligas i sina heliga och hyllas bland alla som tror. Och ni har ju trott på vårt vittnesbörd.

11Därför ber vi alltid för er, att vår Gud ska anse er värdiga hans kallelse och med sin kraft genomföra allt det goda ni planerar och vill göra på grund av er tro. 12Så blir Herren Jesus förhärligad i er och ni i honom, tack vare nåden från vår Gud och Herre Jesus Kristus.